< Eksodo 36 >

1 Choncho Bezaleli, Oholiabu pamodzi ndi anthu aluso onse amene Yehova anawapatsa luso ndi nzeru zodziwira kupanga zofunika zonse zomangira malo opatulika, adzapanga zonse iwowo, monga momwe Yehova analamulira.”
И стаде радити Веселеило и Елијав и сви људи вешти, којима беше Господ дао мудрост и разум да умеју радити сваки посао за службу у светињи, и све што је заповедио Господ.
2 Ndipo Mose anayitana Bezaleli ndi Oholiabu ndiponso munthu aliyense waluso amene Yehova anamupatsa luso ndiponso amene anali ndi mtima wofuna kugwira ntchito.
И позва Мојсије Веселеила и Елијава и све људе веште, којима Господ даде мудрост у срце, које год подиже срце њихово да дођу да раде тај посао.
3 Iwo analandira kuchokera kwa Mose zopereka zonse Aisraeli anabweretsa kuti agwirire ntchito yomanga malo wopatulika. Ndipo anthu anapitirira kupereka zopereka zaufulu mmawa uliwonse.
И узеше од Мојсија све прилоге, које донесоше синови Израиљеви да се уради дело за службу у светињи. Али још доношаху к њему драговољне прилоге свако јутро.
4 Kotero amisiri onse amene amagwira ntchito yonse ya malo wopatulika anasiya ntchitoyo
Тада дођоше сви вешти људи, који рађаху дело за светињу, сваки од свог посла, који рађаху,
5 ndipo anati kwa Mose, “Anthu akubweretsa kuposa zimene zikufunika kugwirira ntchito imene Yehova analamulira kuti ichitike.”
И рекоше Мојсију говорећи: Више доноси народ него што треба да се уради дело, које је Господ заповедио да се уради.
6 Choncho Mose analamulira ndipo analengeza mu msasa onse, “Mwamuna kapena mayi aliyense asaperekenso chopereka chilichonse cha ku malo wopatulika.” Choncho anthu analetsedwa kubweretsa zambiri,
И заповеди Мојсије да се огласи по логору говорећи: Ни човек ни жена да не доноси више прилоге за светињу. И забрани се народу да не доноси.
7 chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.
Јер беше свега доста да се уради све дело, и још претецаше.
8 Anthu onse aluso pakati pa anthu ogwira ntchitoyo anapanga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso anapeta pa nsaluzo Akerubi.
И људи вешти између оних, који радише ово дело, начинише шатор од десет завеса од танког платна узведеног и од порфире и од скерлета и од црвца, с херувимима, вешто везеним начинише.
9 Nsalu zonse zinali zofanana. Mulitali mwake zinali mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
У дужину беше један завес од двадесет и осам лаката а у ширину од четири лакта; сви завеси беху једне мере.
10 Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
И саставише пет завеса један с другим, и пет других завеса саставише један с другим.
11 Kenaka anapanga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
И начинише петље од порфире по крају првог завеса на оној страни где ће се саставити с другим; и тако начинише на сваком завесу по крају где ће се саставити с другим.
12 Iwo anasokerera zokolowekamo makumi asanu pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Anapanga kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
Педесет петаља начинише на првом завесу, и педесет петаља начинише на крају сваког завеса где се саставља с другим; петље беху једна према другој.
13 Kenaka anapanga ngowe zagolide 50 zolumikizira nsalu ziwirizo kotero kuti zinapanga chihema chimodzi.
И начинише педесет златних кука, и саставише кукама завесе један с другим; тако се шатор састави.
14 Iwo anapanga nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zinalipo khumi ndi imodzi.
И начинише завесе од кострети за наслон над шатором; једанаест таквих завеса начинише.
15 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zinali zofanana. Mulitali mwake munali mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake munali mamita awiri.
У дужину беше један завес од тридесет лаката а у ширину од четири лакта; једне мере беше свих једанаест завеса.
16 Iwo analumikiza nsalu zisanu kukhala nsalu imodzi ndipo nsalu zinazo zisanu ndi imodzi, analumikizanso kukhala nsalu imodzinso.
И саставише пет завеса заједно, а других шест завеса заједно.
17 Kenaka anasokerera zokolowekamo makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija ndiponso anapanga zokolowekamo zina makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
И начинише педесет петаља по крају једног завеса где се саставља са другим, и педесет петаља начинише по крају другог завеса да се састави.
18 Iwo anapanga ngowe 50 zamkuwa zolowetsa mu zokolowekazo ndipo anaphatikiza nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
И начинише педесет кука од бронзе да се састави наслон.
19 Ndipo anapanga chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake anapanganso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
И начинише покривач на наслон од кожа овнујских црвених обојених, и покривач од кожа јазавичијих озго.
20 Iwo anapanga maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
И начинише даске шатору од дрвета ситима, које ће стајати право.
21 Feremu iliyonse inali yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake munali masentimita 69.
Даска беше дуга десет лаката а подруг лакта широка свака даска.
22 Thabwa lililonse linali ndi zolumikizira ziwiri. Iwo anapanga maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
По два чепа беху на дасци, један према другом; тако начинише на свим даскама за шатор.
23 Anapanga maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho,
А ових дасака за шатор начинише двадесет дасака за јужну страну;
24 ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
И четрдесет стопица сребрних начинише под двадесет дасака, две стопице под једну даску за два чепа њена, а две стопице под другу даску за два чепа њена.
25 Iwo anapanganso maferemu makumi awiri a mbali yakumpoto ya chihemacho,
Тако и на другој страни шатора, према северу, начинише двадесет дасака,
26 ndiponso matsinde makumi anayi asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
И четрдесет стопица сребрних под њих, две стопице под једну даску а две стопице под другу даску.
27 Anapanganso maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo,
А на западној страни шатора начинише шест дасака;
28 ndiponso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
И још две даске начинише на углове шатору с обе стране;
29 Pa ngodya ziwirizi panali maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba atalumikizidwa pa ngowe imodzi. Maferemu onse anali ofanana.
Оне беху састављене оздо, и беху састављене озго биочугом; тако начинише с обе стране на два угла.
30 Choncho panali maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri anali pansi pa feremu iliyonse.
И тако беше осам дасака и шеснаест стопица њихових сребрних, по две стопице под сваку даску.
31 Iwo anapanganso mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha. Mitanda isanu inali ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
И начинише преворнице од дрвета ситима: пет за даске на једној страни шатора,
32 mitanda isanu inanso inali ya maferemu a mbali inayo ndipo mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
И пет преворница за даске на другој страни шатора, и пет преворница за даске на западној страни шатора до оба угла.
33 Anapanga mtanda wapakati omwe umachokera pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
И начинише преворницу средњу да иде преко среде дасака од једног краја до другог.
34 Iwo anakuta maferemuwo ndi golide ndiponso anapanga mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso anayikuta ndi golide.
А даске оковаше златом, и биочуге на њих начинише од злата, да у њима стоје преворнице, и оковаше златом преворнице.
35 Anapanga nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo inali yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso anapetapo zithunzi za Akerubi.
И начинише завес од порфире и од скерлета и од црвца и од танког платна узведеног, с херувимима вешто везеним начинише га.
36 Iwo anapanga nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide. Anapanganso ngowe zagolide za nsanamirazo ndi matsinde asiliva anayi.
И начинише за њ четири ступа од дрвета ситима, и оковаше их златом, а куке на њима беху од злата, и салише им четири стопице од сребра.
37 Anapanga nsalu ya pa chipata cholowera mu chihema, yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira yomwe inali yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
И начинише завес на врата наслону од порфире и од скерлета и од црвца и од танког платна узведеног везен,
38 Anapanga nsanamira zisanu ndi ngowe zake. Anakuta pamwamba pa nsanamirazo ndi zomangira zake ndi golide, ndipo anapanganso matsinde asanu amkuwa.
И пет ступова за њ с кукама њиховим, и врхове им и појасе оковаше златом, и пет стопица под њих од бронзе.

< Eksodo 36 >