< Eksodo 36 >

1 Choncho Bezaleli, Oholiabu pamodzi ndi anthu aluso onse amene Yehova anawapatsa luso ndi nzeru zodziwira kupanga zofunika zonse zomangira malo opatulika, adzapanga zonse iwowo, monga momwe Yehova analamulira.”
Og Besalel og Oholiab og alle kunstforstandige menn, som Herren hadde gitt forstand og kunnskap, så de forstod sig på alt det arbeid som skulde til for å få helligdommen ferdig, gjorde i ett og alt som Herren hadde sagt.
2 Ndipo Mose anayitana Bezaleli ndi Oholiabu ndiponso munthu aliyense waluso amene Yehova anamupatsa luso ndiponso amene anali ndi mtima wofuna kugwira ntchito.
For Moses kalte Besalel og Oholiab og alle kunstforstandige menn, som Herren hadde gitt kunstnergaver, alle hvis hjerte drev dem, til å skride til verket for å fullføre det.
3 Iwo analandira kuchokera kwa Mose zopereka zonse Aisraeli anabweretsa kuti agwirire ntchito yomanga malo wopatulika. Ndipo anthu anapitirira kupereka zopereka zaufulu mmawa uliwonse.
Og de fikk hos Moses hele den gave som Israels barn hadde båret frem til det arbeid som skulde utføres for å få helligdommen ferdig. Men folket bar fremdeles frivillige gaver frem til ham hver morgen.
4 Kotero amisiri onse amene amagwira ntchito yonse ya malo wopatulika anasiya ntchitoyo
Da kom alle de kunstforstandige menn som utførte alt arbeidet ved helligdommen, enhver fra det arbeid han var i ferd med,
5 ndipo anati kwa Mose, “Anthu akubweretsa kuposa zimene zikufunika kugwirira ntchito imene Yehova analamulira kuti ichitike.”
og de sa til Moses: Folket bærer frem meget mere enn det trenges til det arbeid som Herren har befalt å fullføre.
6 Choncho Mose analamulira ndipo analengeza mu msasa onse, “Mwamuna kapena mayi aliyense asaperekenso chopereka chilichonse cha ku malo wopatulika.” Choncho anthu analetsedwa kubweretsa zambiri,
Da lot Moses rope ut i hele leiren: Ingen, hverken mann eller kvinne, skal lenger bære noget frem som gave til helligdommen! Så holdt folket op med å bære frem gaver.
7 chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.
Men det som var gitt, var nok til hele det arbeid som skulde fullføres, ja mere enn nok.
8 Anthu onse aluso pakati pa anthu ogwira ntchitoyo anapanga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso anapeta pa nsaluzo Akerubi.
Så gjorde da alle de kunstforstandige blandt dem som var med i arbeidet, tabernaklet av ti tepper; av fint, tvunnet lingarn og blå og purpurrød og karmosinrød ull blev de gjort med kjeruber på i kunstvevning.
9 Nsalu zonse zinali zofanana. Mulitali mwake zinali mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
Hvert teppe var åtte og tyve alen langt og fire alen bredt; alle teppene holdt samme mål.
10 Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
Fem av teppene festet de sammen, det ene til det andre, og likeså de andre fem tepper.
11 Kenaka anapanga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
Og de gjorde hemper av blå ull i kanten på det ene teppe, ytterst der hvor sammenfestingen skulde være; likeså gjorde de i kanten på det ytterste teppe, der hvor den andre sammenfesting skulde være.
12 Iwo anasokerera zokolowekamo makumi asanu pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Anapanga kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
Femti hemper gjorde de på det ene teppe, og femti hemper gjorde de ytterst på det teppe som var der hvor den andre sammenfesting skulde være; hempene var like mot hverandre, den ene mot den andre.
13 Kenaka anapanga ngowe zagolide 50 zolumikizira nsalu ziwirizo kotero kuti zinapanga chihema chimodzi.
Og de gjorde femti gullkroker og festet teppene til hverandre med krokene, så tabernaklet blev et sammenhengende telt.
14 Iwo anapanga nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zinalipo khumi ndi imodzi.
Så gjorde de tepper av gjetehår til et dekke over tabernaklet; elleve sådanne tepper gjorde de.
15 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zinali zofanana. Mulitali mwake munali mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake munali mamita awiri.
Hvert teppe var tretti alen langt og fire alen bredt; alle de elleve tepper holdt samme mål.
16 Iwo analumikiza nsalu zisanu kukhala nsalu imodzi ndipo nsalu zinazo zisanu ndi imodzi, analumikizanso kukhala nsalu imodzinso.
Og de festet fem av teppene sammen for sig og seks for sig.
17 Kenaka anasokerera zokolowekamo makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija ndiponso anapanga zokolowekamo zina makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
De gjorde femti hemper i kanten på det ene teppe, ytterst der hvor sammenfestingen skulde være, og likeså femti hemper i kanten på det andre teppe, der hvor sammenfestingen skulde være.
18 Iwo anapanga ngowe 50 zamkuwa zolowetsa mu zokolowekazo ndipo anaphatikiza nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
Og de gjorde femti kobberkroker til å feste teppene sammen med så det blev ett dekke.
19 Ndipo anapanga chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake anapanganso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
Over dekket gjorde de et varetak av rødfarvede værskinn og ovenpå det et varetak av takasskinn.
20 Iwo anapanga maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
Plankene til tabernaklet gjorde de av akasietre og reiste dem på ende.
21 Feremu iliyonse inali yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake munali masentimita 69.
Hver planke var ti alen lang og halvannen alen bred.
22 Thabwa lililonse linali ndi zolumikizira ziwiri. Iwo anapanga maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
På hver planke var det to tapper, med en tverrlist imellem; således gjorde de med alle plankene til tabernaklet.
23 Anapanga maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho,
Og av plankene som de gjorde til tabernaklet, reiste de tyve planker på den side som vendte mot syd;
24 ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
og firti fotstykker av sølv gjorde de til å sette under de tyve planker, to fotstykker under hver planke til å feste begge tappene i.
25 Iwo anapanganso maferemu makumi awiri a mbali yakumpoto ya chihemacho,
Likeså gjorde de tyve planker til tabernaklets andre side, den som vendte mot nord,
26 ndiponso matsinde makumi anayi asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
og til dem firti fotstykker av sølv, to fotstykker under hver planke.
27 Anapanganso maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo,
Til baksiden av tabernaklet, mot vest, gjorde de seks planker.
28 ndiponso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
Og to planker gjorde de til tabernaklets hjørner på baksiden;
29 Pa ngodya ziwirizi panali maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba atalumikizidwa pa ngowe imodzi. Maferemu onse anali ofanana.
de var dobbelte nedenfra og likeledes begge dobbelte helt op, til den første ring; således gjorde de med dem begge på begge hjørnene.
30 Choncho panali maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri anali pansi pa feremu iliyonse.
Således blev det åtte planker med sine fotstykker av sølv - seksten fotstykker, to under hver planke.
31 Iwo anapanganso mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha. Mitanda isanu inali ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
Så gjorde de tverrstenger av akasietre, fem til plankene på den ene side av tabernaklet
32 mitanda isanu inanso inali ya maferemu a mbali inayo ndipo mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
og fem til plankene på den andre side, og fem til plankene på baksiden av tabernaklet, mot vest.
33 Anapanga mtanda wapakati omwe umachokera pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
Og den mellemste tverrstang satte de således at den gikk tvert over midt på plankeveggen, fra den ene ende til den andre.
34 Iwo anakuta maferemuwo ndi golide ndiponso anapanga mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso anayikuta ndi golide.
Plankene klædde de med gull, og ringene på dem, som tverrstengene skulde stikkes i, gjorde de helt av gull; tverrstengene klædde de også med gull.
35 Anapanga nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo inali yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso anapetapo zithunzi za Akerubi.
Så gjorde de forhenget av blå og purpurrød og karmosinrød ull og fint, tvunnet lingarn; de gjorde det i kunstvevning med kjeruber på.
36 Iwo anapanga nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide. Anapanganso ngowe zagolide za nsanamirazo ndi matsinde asiliva anayi.
Og de gjorde fire stolper av akasietre til forhenget og klædde dem med gull; hakene på dem var av gull, og de støpte fire fotstykker av sølv til dem.
37 Anapanga nsalu ya pa chipata cholowera mu chihema, yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira yomwe inali yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
Til teltdøren gjorde de et teppe av blå og purpurrød og karmosinrød ull og fint, tvunnet lingarn med utsydd arbeid,
38 Anapanga nsanamira zisanu ndi ngowe zake. Anakuta pamwamba pa nsanamirazo ndi zomangira zake ndi golide, ndipo anapanganso matsinde asanu amkuwa.
og til teppet fem stolper med sine haker, og de klædde stolpehodene og stengene med gull; og til stolpene gjorde de fem fotstykker av kobber.

< Eksodo 36 >