< Eksodo 36 >
1 Choncho Bezaleli, Oholiabu pamodzi ndi anthu aluso onse amene Yehova anawapatsa luso ndi nzeru zodziwira kupanga zofunika zonse zomangira malo opatulika, adzapanga zonse iwowo, monga momwe Yehova analamulira.”
Tedy dělal Bezeleel a Aholiab i všeliký muž vtipný, jimž dal Hospodin moudrost a rozumnost, aby uměli dělati všeliké dílo k službě svatyně, všecko, což přikázal Hospodin.
2 Ndipo Mose anayitana Bezaleli ndi Oholiabu ndiponso munthu aliyense waluso amene Yehova anamupatsa luso ndiponso amene anali ndi mtima wofuna kugwira ntchito.
Povolal pak Mojžíš Bezeleele a Aholiaba i každého muže vtipného, v jehož srdce dal Hospodin moudrost, každého také, kohož ponoukalo srdce jeho, aby přistoupil ku práci díla toho.
3 Iwo analandira kuchokera kwa Mose zopereka zonse Aisraeli anabweretsa kuti agwirire ntchito yomanga malo wopatulika. Ndipo anthu anapitirira kupereka zopereka zaufulu mmawa uliwonse.
A vzali od Mojžíše všecky dary, kteréž přinesli synové Izraelští k dílu služebnému svatyně, aby dělali je. Ale oni vždy předce přinášeli k němu každého jitra dary dobrovolné.
4 Kotero amisiri onse amene amagwira ntchito yonse ya malo wopatulika anasiya ntchitoyo
Tedy přišli všickni vtipní dělníci díla svatyně, každý od díla svého, kteréž dělali,
5 ndipo anati kwa Mose, “Anthu akubweretsa kuposa zimene zikufunika kugwirira ntchito imene Yehova analamulira kuti ichitike.”
A mluvili k Mojžíšovi těmi slovy: Mnohem více přináší lid, nežli potřebí jest k dělání díla, kteréž přikázal Hospodin dělati.
6 Choncho Mose analamulira ndipo analengeza mu msasa onse, “Mwamuna kapena mayi aliyense asaperekenso chopereka chilichonse cha ku malo wopatulika.” Choncho anthu analetsedwa kubweretsa zambiri,
I rozkázal Mojžíš, aby provoláno bylo v vojště takto: Muž ani žena, žádný nepřinášej více oběti k svatyni. I zbráněno jest lidu, aby nenosili.
7 chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.
Nebo měli potřeb hojně dosti k dělání všelikého díla, tak že zbývalo.
8 Anthu onse aluso pakati pa anthu ogwira ntchitoyo anapanga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso anapeta pa nsaluzo Akerubi.
I dělal každý vtipný z dělníků těch dílo to, příbytek z desíti čalounů, kteříž byli z bílého hedbáví přesukovaného, a z postavce modrého a šarlatu, a z červce dvakrát barveného, cherubíny dílem řemeslným udělal na nich.
9 Nsalu zonse zinali zofanana. Mulitali mwake zinali mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
Dlouhost čalounu jednoho osm a dvadceti loktů, a čtyř loktů širokost čalounu jednoho; všickni čalounové byli jednostejné míry.
10 Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
Potom spojil pět čalounů jeden s druhým, a pět jiných čalounů spojil jeden s druhým.
11 Kenaka anapanga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
Nadělal i ok z hedbáví modrého po kraji čalounu jednoho na konci, kde se spojovati má s druhým, a tolikéž udělal na kraji čalounu druhého na konci v spojení druhém.
12 Iwo anasokerera zokolowekamo makumi asanu pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Anapanga kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
Padesáte ok udělal na čalounu jednom, a padesáte ok udělal po kraji čalounu, kterýmž připojen byl k druhému; oko jedno proti druhému bylo.
13 Kenaka anapanga ngowe zagolide 50 zolumikizira nsalu ziwirizo kotero kuti zinapanga chihema chimodzi.
Udělal i padesáte haklíků zlatých a spojil čalouny jeden s druhým haklíky těmi; a tak udělán jest příbytek jeden.
14 Iwo anapanga nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zinalipo khumi ndi imodzi.
Nadto nadělal houní z srstí kozích na stánek, k přistírání příbytku po vrchu; jedenácte houní udělal.
15 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zinali zofanana. Mulitali mwake munali mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake munali mamita awiri.
Dlouhost houně jedné třidceti loktů, a širokost houně jedné čtyř loktů; jednostejná míra byla těch jedenácti houní.
16 Iwo analumikiza nsalu zisanu kukhala nsalu imodzi ndipo nsalu zinazo zisanu ndi imodzi, analumikizanso kukhala nsalu imodzinso.
A spojil pět houní obzvláštně, a šest houní obzvláštně.
17 Kenaka anasokerera zokolowekamo makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija ndiponso anapanga zokolowekamo zina makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
Udělal také padesáte ok po kraji houně na konci, kdež se spojovati má, a padesáte ok udělal po kraji houně v spojení druhém.
18 Iwo anapanga ngowe 50 zamkuwa zolowetsa mu zokolowekazo ndipo anaphatikiza nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
Udělal k tomu haklíků měděných padesáte k spojení stánku, aby byl jedno.
19 Ndipo anapanga chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake anapanganso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
Nadto udělal přikrytí stánku z koží skopcových na červeno barvených, a přikrytí z koží jezevčích svrchu.
20 Iwo anapanga maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
Nadělal k příbytku i desk z dříví setim stojatých.
21 Feremu iliyonse inali yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake munali masentimita 69.
Desíti loktů dlouhost dsky, a půl druhého širokost dsky každé.
22 Thabwa lililonse linali ndi zolumikizira ziwiri. Iwo anapanga maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
Dva čepy měla dska jedna, podobně jako stupně u schodu spořádané, jeden proti druhému; tak udělal u všech desk příbytku.
23 Anapanga maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho,
Zdělal i dsky k příbytku, dvadceti desk k straně polední, k větru polednímu.
24 ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
A čtyřidceti podstavků stříbrných udělal pode dvadceti desk, dva podstavky pod jednu dsku ke dvěma čepům jejím, a dva podstavky pod dsku druhou pro dva čepy její.
25 Iwo anapanganso maferemu makumi awiri a mbali yakumpoto ya chihemacho,
Na druhé pak straně příbytku k straně půlnoční udělal dvadceti desk,
26 ndiponso matsinde makumi anayi asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
A čtyřidceti podstavků jejich stříbrných, dva podstavky pod jednu dsku a dva podstavky pod dsku druhou.
27 Anapanganso maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo,
Na straně pak příbytku k západu udělal šest desk.
28 ndiponso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
Dvě dsky udělal v úhlech po obou stranách příbytku.
29 Pa ngodya ziwirizi panali maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba atalumikizidwa pa ngowe imodzi. Maferemu onse anali ofanana.
A byly spojené po spodu a tolikéž spojené svrchu k jednomu kruhu; tak udělal po obou stranách ve dvou úhlech.
30 Choncho panali maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri anali pansi pa feremu iliyonse.
A tak bylo osm desk a podstavků jejich stříbrných šestnácte, dva podstavkové pod každou dskou.
31 Iwo anapanganso mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha. Mitanda isanu inali ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
Nadělal i svlaků z dřívi setim, pět ke dskám straně příbytku jedné,
32 mitanda isanu inanso inali ya maferemu a mbali inayo ndipo mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
A pět svlaků ke dskám druhé strany příbytku, a pět svlaků ke dskám strany příbytku západní, dosahujících k oběma úhlům.
33 Anapanga mtanda wapakati omwe umachokera pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
A svlak prostřední udělal, aby šel po prostředku desk od jednoho kraje k druhému.
34 Iwo anakuta maferemuwo ndi golide ndiponso anapanga mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso anayikuta ndi golide.
Dsky pak obložil zlatem a kruhy jejich udělal z zlata, aby v nich svlaky byly; a obložil svlaky zlatem.
35 Anapanga nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo inali yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso anapetapo zithunzi za Akerubi.
Udělal také oponu z postavce modrého a šarlatu, a z červce dvakrát barveného, a z bílého hedbáví přesukovaného; dílem řemeslným udělal ji s figurami cherubínů.
36 Iwo anapanga nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide. Anapanganso ngowe zagolide za nsanamirazo ndi matsinde asiliva anayi.
A udělal pro ni čtyři sloupy z dříví setim, a obložil je zlatem; hákové pak jejich byli zlatí, a slil k nim čtyři podstavky stříbrné.
37 Anapanga nsalu ya pa chipata cholowera mu chihema, yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira yomwe inali yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
Udělal také zastření ke dveřům stánku z postavce modrého, z šarlatu a z červce dvakrát barveného a z bílého hedbáví přesukovaného, dílem krumpéřským,
38 Anapanga nsanamira zisanu ndi ngowe zake. Anakuta pamwamba pa nsanamirazo ndi zomangira zake ndi golide, ndipo anapanganso matsinde asanu amkuwa.
A sloupů k tomu zastření pět s háky jejich, (obložil pak makovice a přepásaní jich zlatem), a podstavků pět měděných.