< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
Mojzes je zbral skupaj vso skupnost Izraelovih otrok ter jim rekel: »To so besede, ki jih je Gospod zapovedal, da naj bi jih vi delali.
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
Šest dni naj bo delo opravljano, toda na sedmi dan naj vam bo sveti dan, šabatni počitek Gospodu. Kdorkoli v njem opravlja delo, bo usmrčen.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
Vsepovsod po svojih prebivališčih na šabatni dan ne boste prižigali nobenega ognja.«
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
Mojzes je spregovoril vsej skupnosti Izraelovih otrok, rekoč: »To je stvar, ki jo je zapovedal Gospod, rekoč:
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
›Vzemite izmed vas daritev Gospodu. Kdorkoli je voljnega srca, naj jo prinese, daritev Gospodu: zlato, srebro, bron,
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
modro, vijolično, škrlatno in tanko laneno platno, kozjo dlako,
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
rdeče barvane ovnove kože, jazbečeve kože, akacijev les,
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
olje za svetlobo, dišave za mazilno olje in za dišeče kadilo,
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
oniksove kamne in kamne, da se pripravijo za efód in za naprsnik.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
Vsak, ki je izmed vas modrega srca, bo prišel in storil vse, kar je Gospod zapovedal:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
šotorsko svetišče, njegov šotor in njegovo pokrivalo, njegove zaponke in njegove deske, njegove zapahe, njegove stebre in njegove podstavke,
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
skrinjo in njena drogova s sedežem milosti in zagrinjalo pokrivala,
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
mizo in njena drogova, vse njene posode in hlebe navzočnosti,
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
tudi svečnik za svetlobo in njegovo opremo in njegove svetilke z oljem za svetlobo
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
in kadilni oltar in njegova drogova, mazilno olje in dišeče kadilo, tanko preprogo za vrata pri šotorskem vhodu šotorskega svetišča,
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
oltar žgalne daritve z njegovo bronasto rešetko, njegova drogova in vse njegove posode, [okrogel] umivalnik in njegovo vznožje,
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
tanke preproge dvora, njegove stebre in njihove podstavke in tanko preprogo za vrata dvora,
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
količke šotorskega svetišča, količke dvora in njihove vrvice,
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
službene obleke, da opravljajo službo na svetem kraju, sveta oblačila za duhovnika Arona in oblačila njegovih sinov, za služenje v duhovniški službi.‹«
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
Vsa skupnost Izraelovih otrok je odšla iz Mojzesove prisotnosti.
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
Prišli so, vsakdo, čigar srce ga je razvnelo in vsakdo, čigar duh ga je storil voljnega in prinesli so Gospodovo daritev h gradnji šotorskega svetišča skupnosti in za vso njegovo službo in za sveta oblačila.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Prišli so, tako moški kakor ženske, tako veliko kot jih je bilo voljnega srca in prinesli zapestnice, uhane, prstane, ogrlice, vse dragocenosti iz zlata. Vsak človek, ki je daroval, je daroval daritev zlata Gospodu.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
Vsak človek, pri katerem je bilo najdeno modro, vijolično, škrlatno in tanko laneno platno, kozja dlaka, rdeča koža ovnov in jazbečeve kože, jih je prinesel.
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Vsak, kdor je daroval daritev srebra in brona, je prinesel Gospodovo daritev. Vsak človek, pri komer se je našel akacijev les za katerokoli delo službe, ga je prinesel.
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
Vse ženske, ki so bile modrega srca, so predle s svojimi rokami in prinesle to, kar so napredle, tako iz modrega, iz vijoličnega in iz škrlata in iz tankega lanenega platna.
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
Vse ženske, ki jih je srce razvnelo v modrosti, so predle kozjo dlako.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
Voditelji so prinesli oniksove kamne in kamne, da se pripravijo za efód in za naprsnik,
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
dišavo in olje za svetlobo in za mazilno olje in za dišeče kadilo.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
Izraelovi otroci so prinesli voljno daritev Gospodu, vsak moški in ženska, katerega srce jih je storilo voljne, da prinesejo za vse vrste dela, ki ga je Gospod zapovedal, da bo storjeno po Mojzesovi roki.
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
Mojzes je Izraelovim otrokom rekel: »Glejte, Gospod je po imenu poklical Becaléla, Urijájevega sina, Hurovega sina, iz Judovega rodu
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
in ga napolnil z Božjim duhom, v modrosti, v razumevanju, v znanju in v vseh vrstah rokodelstva
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
in da snuje nenavadna dela, da dela v zlatu, v srebru, v bronu,
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
v rezanju kamnov, da se jih vdela in v rezbarjenju lesa, da naredi vsake vrste spretno delo.
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
V njegovo srce je položil, da lahko poučuje, tako on in Oholiáb, Ahisamáhov sin, iz Danovega rodu.
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
Napolnil ju je s srčno modrostjo, da opravljata vse vrste dela, od graverja do spretnega delavca in od tistega, ki izveze v modri, v vijolični, v škrlatni in v tankem lanenem platnu do tkalca, celó izmed teh, ki opravljajo katerokoli delo in izmed teh, ki snujejo spretno delo.«

< Eksodo 35 >