< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
Natonto’ i Mosè i valobohò’ Israele iabiy vaho nanoa’e ty hoe, Hoe ty tsara linili’ Iehovà hanoe’ areo.
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
Eneñ’ andro ty fitoloñan-draha, fe andro havahe’ areo ty andro fahafito, i Sabatam-pitofà am’ Iehovày. Hakoromake ze ondaty mifanehak’ ama’e.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
Ko mamiañe afo ndra aia’aia amo kivoho’ areoo ami’ty andro Sabotse.
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
Le nisaontsie’ i Mosè i hene valobohò’ Israeley: Inao ty nandilia’ Iehovà:
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
Aneseo boak’ ama’ areo ao, le ibanabanao am’ Iehovà; ze mirearea an-troke ro hañenga am’ Iehovà: ty volamena naho volafoty vaho torisìke;
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
naho manga naho malòmavo naho mena mañabarà naho leny marerarera vaho volon’ ose;
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
le holi’ añondrilahy linoko mena naho holin-trozofisoitse naho mendorave;
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
naho solike ho ami’ty hazavañe naho hafiriañe ho ami’ty menake fañorizañe naho ho ami’ ty emboke mandrifondrifoñe;
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
naho vato sohàme naho vatosoa ho reketeñe amy kitam­bey naho amy takon’ arañañey.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
Le homb’etoañ’ iaby ze mahihi-tro hi­tsene o raha linili’ Iehovà iabio:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
i kivohoy, i kibohotsey naho i rako’ey, o vitra’eo naho o varambañeo, o saka’eo, o ana-kòre’eo naho o vave’eo;
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
i vatam-pañinay naho o bao-pitakona’eo, i toem-pijebañañey naho i lamba fañefetsey;
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
i rairaiy naho o bao’eo naho o harao’eo naho o mofo-miatrekeo;
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
le i fitàn-jiroy ho amy hazavàñey naho o harao’eo naho o jiro’eo naho ty mena’ i hazavàñey;
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
naho i kitrelim-pañembohañey naho o bao’eo naho i mena-pañorizañey naho i menake mañitsey naho i lamba fañefe’ i lala-pizilihañe amy kivohoiy;
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
ty kitrely fisoroñañe rekets’ i tsingarakara’e torisìkey, o bao’eo naho o hene fanakeo, i fanasàñey rekets’ i foto’ey;
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
o firadoradoañe an-kiririsao, o anakòre’eo naho o vave’eo naho ty lamba fañefe’ i lalambein-kiririsay;
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
o tsato’ i kivohoio naho o tsato’ i kiririsaio vaho o tali’ iareoo;
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
o fisiky hitoloñañe amy toe-miavakeio: o saro-miava’ i Aharone mpisoroñeo; ty fisaro’ o ana’eo hitoloña’ iareo ho mpisoroñeo.
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
Aa le nienga boak’ aolo’ i Mosè o ana’ Israele iabio.
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
Le nimb’eo ze hene niroroten-troke naho ze nampirea­rean-arofo, nanese banabana am’ Iehovà ho ami’ty fitoloñañe i kibo­hom-pamantañañey naho ho amy ze hene fitoroñañe ama’e vaho amo saro-miavakeo.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Songa nimb’eo an-joton-troke ty lahilahy naho ampela, ninday ravake naho kiviron-oroñe naho kiviron-tsofy, bange fitomboke naho hareañe, ze bijim-bolamena iaby; vaho ze nanokañe engam-bolamena am’ Iehovà.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
Ze ondaty amam-pole manga ndra malòmavo ndra mena mañabarà ndra fole leny matify ndra volon’ ose ndra holin’ añondrilahy linoko mena ndra holin-trozofisoitse, le sambe ninday.
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Ze ondaty nañenga volafoty ndra torisìke songa nibanabana aze am’ Iehovà; naho ze nahatendrehañe mendoraveñe ho amy fitoloñañe i asaiy, sindre ninday.
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
Nandrorotse fole am-pità’e ze rakemba nahihi-tro, le nendese’e i nirorote’ey, ty manga naho ty malòmavo naho ty mena mañabarà vaho ty leny matify.
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
Le nandrorotse volon-ose ze rakemba nonjone’ ty tro’e an-kihitse.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
O mpifeheo ninday vato sohàme naho vato soa harekets’ amy kitam­bey naho amy kalan’ arañañey;
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
ty emboke; naho ty menake ho amy hazavàñey, ho amy mena-pañorizañey vaho ho amy emboke mañitsey.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
Nibanabana enga an-tsatrin’ arofo am’ Iehovà ze hene ana’ Israele ndra lahi­lahy ndra rakemba nihavàtse añ’ arofo, hanolora’e amo tolon-draha linili’ Iehovà hanoeñe am-pità’ i Mosèo.
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
Le hoe t’i Mosè amo ana’ Israeleo: Ingo te kinanji’ Iehovà ami’ty tahina’e t’i Betsalale, ana’i Orý, ana’ i Kore, fifokoa’ Iehodà;
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
naho nilifore’e ami’ty Arofon’ Añahare an-kihitse naho faharendrehañe, an-kilala naho amy ze satam-pitoloñañe iaby,
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
hisafiry naho hamoroñe, hitoloñe am-bolamena naho volafoty vaho torisìke
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
naho hampisilake vatosoa ho reketeñe naho hanokitse an-katae vaho hitoloñe amy ze hene karaza satam-pitàñe.
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
Le napo’e añ’arofo’e ao ty hañòke, ie naho i Oholiabe ana’ i Ahisamake, fifokoa’ i Dane.
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
Ie songa lilifore’e hihitse añ’arofo hanoa’e ze satam-panokitse naho mpamoroñe, le hamahotse am-pole manga naho malò mavo naho mena mañabarà naho leny matify hitoloñe am-panenoñañe; hitoloñe amy ze hene tolon-draha vaho hamoroñe o nisafirieñeo.

< Eksodo 35 >