< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
Et Moïse réunit toute l’assemblée des fils d’Israël, et leur dit: Ce sont ici les choses que l’Éternel a commandé de faire:
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
Pendant six jours le travail se fera, mais le septième jour sera pour vous un [jour] saint, un sabbat de repos [consacré] à l’Éternel: quiconque fera une œuvre ce jour-là, sera mis à mort.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
Vous n’allumerez point de feu, dans toutes vos habitations, le jour du sabbat.
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
Et Moïse parla à toute l’assemblée des fils d’Israël, en disant: Voici ce que l’Éternel a commandé, disant:
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
Prenez, de ce qui est à vous, une offrande pour l’Éternel; que tout homme qui a un esprit libéral apporte l’offrande élevée de l’Éternel: de l’or, et de l’argent, et de l’airain;
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
et du bleu, et de la pourpre, et de l’écarlate, et du coton blanc, et du poil de chèvre;
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
et des peaux de béliers teintes en rouge, et des peaux de taissons, et du bois de sittim;
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
et de l’huile pour le luminaire, et des aromates pour l’huile de l’onction et pour l’encens des drogues odoriférantes;
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
et des pierres d’onyx, et des pierres à enchâsser pour l’éphod et pour le pectoral.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
– Et que tous les hommes intelligents parmi vous viennent, et fassent tout ce que l’Éternel a commandé:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
le tabernacle, sa tente, et sa couverture, ses agrafes, et ses ais, ses traverses, ses piliers, et ses bases;
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
l’arche et ses barres, le propitiatoire, et le voile qui sert de rideau;
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
la table et ses barres, et tous ses ustensiles, et le pain de proposition;
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
et le chandelier du luminaire, et ses ustensiles, et ses lampes, et l’huile du luminaire;
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
et l’autel de l’encens et ses barres; et l’huile de l’onction, et l’encens des drogues odoriférantes; et le rideau de l’entrée, pour l’entrée du tabernacle;
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
l’autel de l’holocauste et la grille d’airain qui lui appartient, ses barres et tous ses ustensiles; la cuve et son soubassement;
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
les tentures du parvis, ses piliers, et ses bases, et le rideau de la porte du parvis;
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
les pieux du tabernacle, et les pieux du parvis, et leurs cordages;
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
les vêtements de service pour servir dans le lieu saint, les saints vêtements pour Aaron, le sacrificateur, et les vêtements de ses fils pour exercer la sacrificature.
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
Et toute l’assemblée des fils d’Israël sortit de devant Moïse.
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
Et tout homme que son cœur y porta, et tous ceux qui avaient un esprit libéral, vinrent et apportèrent l’offrande de l’Éternel pour l’œuvre de la tente d’assignation, et pour tout son service, et pour les saints vêtements.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Et les hommes vinrent avec les femmes: tout homme qui offrit une offrande tournoyée d’or à l’Éternel, tous ceux qui avaient un esprit libéral apportèrent des anneaux de nez, et des pendants d’oreille, et des anneaux, et des colliers, toutes sortes d’objets d’or.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
Et tout homme chez qui se trouva du bleu, et de la pourpre, et de l’écarlate, et du coton blanc, et du poil de chèvre, et des peaux de béliers teintes en rouge, et des peaux de taissons, les apporta.
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Tout [homme] qui offrit une offrande élevée d’argent et d’airain, apporta l’offrande de l’Éternel; et tout [homme] chez qui se trouva du bois de sittim pour toute l’œuvre du service, l’apporta.
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
Et toute femme intelligente fila de sa main, et apporta ce qu’elle avait filé: le bleu, et la pourpre, et l’écarlate, et le fin coton;
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
et toutes les femmes habiles que leur cœur y porta filèrent du poil de chèvre.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
Et les princes apportèrent les pierres d’onyx et les pierres à enchâsser pour l’éphod et pour le pectoral;
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
et les aromates, et l’huile pour le luminaire, et pour l’huile de l’onction, et pour l’encens des drogues odoriférantes.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
Les fils d’Israël, tout homme et toute femme qui eurent un esprit libéral pour apporter pour toute l’œuvre que, par Moïse, l’Éternel avait commandé de faire, apportèrent une offrande volontaire à l’Éternel.
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
Et Moïse dit aux fils d’Israël: Voyez, l’Éternel a appelé par nom Betsaleël, fils d’Uri, fils de Hur, de la tribu de Juda;
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
et il l’a rempli de l’esprit de Dieu, en sagesse, en intelligence, et en connaissance, et pour toute espèce d’ouvrages;
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
et pour faire des inventions, pour travailler en or, et en argent, et en airain;
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
et pour tailler des pierres à enchâsser, et pour tailler le bois, afin d’exécuter des dessins en toutes sortes d’ouvrages;
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
et à lui et à Oholiab, fils d’Akhisamac, de la tribu de Dan, il a mis au cœur d’enseigner;
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
il les a remplis de sagesse de cœur pour faire tout ouvrage de graveur et d’inventeur, et de brodeur en bleu et en pourpre, en écarlate et en fin coton, et [tout ouvrage] de tisserand, faisant toute espèce de travail, et inventant des dessins.

< Eksodo 35 >