< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
Moses [Drawn out] assembled all the congregation of the children of Israel [God prevails], and said to them, “These are the words which Adonai has enjoined, that you should do them.
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
‘Six days shall work be done, but on the seventh day there shall be a holy day for you, a Sabbath of solemn rest to Adonai: whoever does any work in it shall be put to death.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
You shall kindle no fire throughout your habitations on the Sabbath day.’”
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
Moses [Drawn out] spoke to all the congregation of the children of Israel [God prevails], saying, “This is the thing which Adonai enjoined, saying,
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
‘Take from among you an offering to Adonai. Whoever is of a willing heart, let him bring it, Adonai’s offering: gold, silver, bronze,
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
blue, purple, scarlet, fine linen, goats’ hair,
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
rams’ skins dyed red, sea cow hides, acacia wood,
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
oil for the light, spices for the anointing oil and for the sweet incense,
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
onyx stones, and stones to be set for the ephod and for the breastplate.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
“‘Let every wise-hearted man among you come, and make all that Adonai has enjoined:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
the tabernacle, its outer covering, its roof, its clasps, its boards, its bars, its pillars, and its sockets;
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
the ark, and its poles, the mercy seat, the veil of the screen;
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
the table with its poles and all its utensils, and the show bread;
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
the menorah ·lamp· also for the light, with its utensils, its lamp candles, and the oil for the light;
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
and the altar of incense with its poles, the anointing oil, the sweet incense, the screen for the door, at the door of the tabernacle;
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
the altar of burnt offering, with its grating of bronze, it poles, and all its utensils, the basin and its base;
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
the hangings of the court, its pillars, their sockets, and the screen for the gate of the court;
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
the pins of the tabernacle, the pins of the court, and their cords;
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
the finely worked garments, for ministering in the holy place, the holy garments for Aaron [Light-bringer] the priest, and the garments of his sons, to minister in the priest’s office.’”
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
All the congregation of the children of Israel [God prevails] departed from the presence of Moses [Drawn out].
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
They came, everyone whose heart stirred him up, and everyone whom his spirit made willing, and brought Adonai’s offering, for the work of the Tent of Meeting, and for all of its service, and for the holy garments.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
They came, both men and women, as many as were willing-hearted, and brought brooches, earrings, signet rings, and armlets, all jewels of gold; even every man who offered an offering of gold to Adonai.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
Everyone, with whom was found blue, purple, scarlet, fine linen, goats’ hair, rams’ skins dyed red, and sea cow hides, brought them.
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Everyone who offered an offering of silver and bronze brought Adonai’s offering; and everyone, with whom was found acacia wood for any work of the service, brought it.
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
All the women who were wise-hearted spun with their hands, and brought that which they had spun, the blue, the purple, the scarlet, and the fine linen.
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
All the women whose heart stirred them up in wisdom spun the goats’ hair.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
The rulers brought the onyx stones, and the stones to be set, for the ephod and for the breastplate;
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
and the spice, and the oil for the light, for the anointing oil, and for the sweet incense.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
The children of Israel [God prevails] brought a free will offering to Adonai; every man and woman, whose heart made them willing to bring for all the work, which Adonai had enjoined to be made by Moses [Drawn out].
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
Moses [Drawn out] said to the children of Israel [God prevails], “Behold, Adonai has called by name Bezalel the son of Uri, the son of Hur, of the tribe of Judah [Praised].
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
He has filled him with the Spirit of God, in wisdom, in understanding, in knowledge, and in all kinds of workmanship;
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
and to make skillful works, to work in gold, in silver, in bronze,
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
in cutting of stones for setting, and in carving of wood, to work in all kinds of skillful workmanship.
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
He has put in his heart that he may teach, both he, and Oholiab, the son of Ahisamach, of the tribe of Dan [He judged].
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
He has filled them with wisdom of heart, to work all kinds of workmanship, of the engraver, of the skillful workman, and of the embroiderer, in blue, in purple, in scarlet, and in fine linen, and of the weaver, even of those who do any workmanship, and of those who make skillful works.

< Eksodo 35 >