< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
Moses kaldte hele Israeliternes Menighed sammen og sagde til dem: Dette er, hvad HERREN har pålagt eder at gøre:
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
I seks Dage må der arbejdes, men på den syvende Dag skal I holde Helligdag, en fuldkommen Hviledag for HERREN. Enhver, der den Dag udfører noget Arbejde, skal lide Døden.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
På Sabbatsdagen må I ikke gøre Ild i nogen af eders Boliger.
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
Derpå sagde Moses til hele Israeliternes Menighed: Dette er, hvad HERREN har påbudt:
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
I skal tage en Offerydelse til HERREN af, hvad I ejer. Enhver, som i sit Hjerte føler sig tilskyndet dertil, skal komme med det, HERRENs Offerydelse, Guld, Sølv, Kobber,
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
violet og rødt Purpurgatn, karmoisinrødt Garn, Byssus, Gedehår,
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
rødfarvede Væderskind, Tahasjskind, Akacietræ,
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
Olie til Lysestagen, vellugtende Stofer til Salveolien og Røgelsen,
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
Sjohamsten og Ædelsten til Indfatning på Efoden og Brystskjoldet.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
Og alle kunstforstandige Mænd iblandt eder skal komme og lave alt, hvad HERREN har påbudt:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
Boligen med dens Teltdække og Dække, dens Kroge, Brædder, Tværstænger, Piller og Fodstykker,
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
Arken med Bærestængerne, Sonedækket og det indre Forhæng,
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
Bordet med dets Bærestænger og alt dets Tilbehør og Skuebrødene,
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
Lysestagen med dens Tilbehør, dens Lamper og Olien til Lysestagen,
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
Røgelsealteret med dets Bærestænger, Salveolien og Røgelsen. Forhænget til Boligens Indgang,
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
Brændofferalteret med Kobbergitteret, Bærestængerne og alt dets Tilbehør, Vandkummen med dens Fodstykke,
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
Forgårdens Omhæng, dens Piller og Fodstykker og Forhænget til Forgårdens Indgang,
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
Boligens og Forgårdens Pæle med Reb,
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
Pragtklæderne til Tjenesten i Helligdommen, de hellige Klæder til Præsten Aron og hans Sønners Klæder til Brug ved Præstetjenesten.
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
Da forlod hele Israeliternes Menighed Moses.
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
Og enhver, som i sit Hjerte følte sig drevet dertil, og hvis Ånd tilskyndede ham, kom med HERRENs Offerydelse til Opførelsen af Åbenbaringsteltet og til alt Arbejdet derved og til de hellige Klæder.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
De kom dermed, både Mænd og Kvinder; enhver, som i sit Hjerte følte sig tilskyndet dertil, kom med Spænder, Ørenringe, Fingerringe og Halssmykker, alle Hånde Guldsmykker. Og enhver, der vilde vie HERREN en Gave af Guld, kom dermed.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
Og enhver, i hvis Eje der fandtes violet og rødt Purpurgarn, karmoisinrødt Garn, Byssus, Gedehår, rødfarvede Væderskind eller Tahasjskind, kom dermed.
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Og enhver, der vilde give en Offerydelse af Sølv eller Kobber, kom med HERRENs Offerydelse. Og enhver, der ejede Akacietræ til alt Byggearbejdet, kom dermed.
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
Og alle kunstforstandige Kvinder spandt med egne Hænder og kom med deres Spind, violet og rødt Purpur, Karmoisin og Byssus.
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
Og alle Kvinder, som i Kraft af deres Kunstsnilde følte sig tilskyndede dertil i deres Hjerte, spandt Gedehårene.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
Og Øversterne kom med Sjohamstenene og Ædelstenene til Indfatningen på Efoden og Brystskjoldet
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
og de vellugtende Stoffer og Olien til Lysestagen og til Salveolien og Røgelsen.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
Enhver Mand og Kvinde af Israeliterne, som i sit Hjerte følte sig tilskyndet til at bringe, hvad der krævedes til Udførelsen af alt det Arbejde, HERREN gennem Moses havde påbudt, bragte det som en frivillig Gave til HERREN.
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
Derpå sagde Moses til Israeliterne: Se, HERREN har kaldet Bezal'el, en Søn af Hurs Søn Uri, af Judas Stamme
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
og fyldt ham med Guds Ånd, med Kunstsnilde, Kløgt og Indsigt i alskens Arbejde
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
til at udtænke Kunstværker og til at arbejde i Guld, Sølv og Kobber
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
og med Udskæring af Sten til Indfatning og med Træskærerarbejde, kort sagt til at udføre alskens Kunstarbejde.
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
Og tillige har han givet både ham og Oholiab, Ahisamaks Søn, af Dans Stamme Gaver til at lære fra sig.
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
Han har fyldt dem med Kunstsnilde til at udføre alskens Udskæringsarbejde, Kunstvævning, broget Vævning af violet og rødt Purpurgarn, karmoisinrødt Garn og Byssus og almindelig Vævning, så de kan udføre alt Slags Arbejde og udtænke Kunstværker.

< Eksodo 35 >