< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
Mojsije sazva svu zajednicu sinova Izraelovih pa im reče: “Ovo vam je Jahve naložio da činite:
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
Neka se posao obavlja šest dana. Sedmi dan neka vam bude sveti dan, dan potpunog počinka u čast Jahvi. Tko bi radio u taj dan neka se kazni smrću.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
Na subotnji dan ni vatre ne ložite po svojim stanovima.”
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
Nadalje Mojsije reče svoj zajednici izraelskoj: “Ovo je Jahve naredio:
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
Među sobom pokupite prinos Jahvi! Tko god je plemenita srca neka Jahvi donese prinos: zlata, srebra i tuča;
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
ljubičastog, crvenog i tamnocrvenog prediva i prepredenog lana;
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
učinjenih ovnujskih koža, onda finih koža, bagremova drva,
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
ulja za svjetlo, mirodija za ulje pomazanja i miomirisni tamjan;
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
oniksa i drugoga dragog kamenja za umetanje u oplećak i naprsnik.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
A svi koji su među vama vješti neka dođu praviti što je Jahve naredio:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
Prebivalište, njegov Šator i pokrov; njegove kuke i trenice, njegove priječnice i stupce; njegova podnožja;
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
njegov Kovčeg i motke; Pomirilište pa zavjesu za zaklon;
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
stol s njegovim motkama i sve njegove potrepštine; prinesene hljebove;
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
svijećnjak za svjetlo, njegov pribor i njegove svijeće, onda ulje za svjetlo;
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
kadioni žrtvenik i njegove motke; ulje za pomazanje i miomirisni tamjan; zastorak na ulazu u Prebivalište;
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
žrtvenik za žrtve paljenice s njegovom rešetkom od tuča; motke za nj i sav njegov pribor; umivaonik i njegov stalak;
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
zastore za dvorište; stupce i njihova podnožja, pa zastor na ulazu u dvorište;
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
kočiće za Prebivalište i kočiće za dvorište s njihovim uzicama;
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
svečano ruho za vršenje službe u Svetištu - posvećena odijela za svećenika Arona i odijela za svećeničku službu njegovih sinova.”
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
Nato se sva izraelska zajednica povuče ispred Mojsija.
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
A onda svatko koga je srce vuklo i duša poticala dođe noseći svoj prinos u čast Jahvi za gradnju Šatora sastanka, za svaku službu u njemu i za posvećena odijela.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Strčaše se muževi i žene: svi koje je srce vuklo donesoše zapinjača, naušnica, prstenja, narukvica, ogrlica i svakovrsna zlatnog nakita; svi koji bijahu zavjetovali kakvu zlatninu u čast Jahvi.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
Svi kod kojih se našlo ljubičastog, crvenog i tamnocrvenog prediva i prepredenog lana, učinjenih ovnujskih koža ili finih koža donesoše svoje.
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Nadalje, svatko tko je mogao dati kakav dar u srebru ili tuču donese to kao prinos u čast Jahvi. Svatko u koga se našlo bagremova drva za upotrebu u bilo kojem poslu, donese ga.
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
Sve žene koje su bile vješte prele su svojim rukama i donosile što bijahu oprele: ljubičastog, crvenog i tamnocrvenog prediva i prepredenog lana.
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
Sve opet žene koje je njihovo srce poticalo zbog njihove vještine prele su kostrijet.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
Glavari su donosili oniksa i drugoga dragog kamenja za umetanje u oplećak i naprsnik;
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
pa mirodije i ulje za svjetlo, ulje za pomazanje i miomirisni tamjan.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
I tako Izraelci - svi ljudi i sve žene koje je srce poticalo da pridonesu bilo što poslu koji je Jahve po Mojsiju naredio da se izvrši - donesoše to kao dragovoljan prinos u čast Jahvi.
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
Potom reče Mojsije Izraelcima: “Vidite! Jahve je po imenu pozvao Besalela, sina Urijeva, od koljena Hurova a iz plemena Judina.
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
Njega je napunio duhom Božjim, dao mu umješnost, sposobnost i razumijevanje u svim poslovima:
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
da zamišlja nacrte i da radove izvodi od zlata, srebra i tuča;
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
da reže dragulje za umetanje; da urezuje u drvetu i da umješno radi svaki posao.
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
Njemu i Oholiabu, sinu Ahisamakovu, od plemena Danova, udijeli i sposobnost da poučavaju druge.
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
Obdari ih umještvom u svakom poslu rezbarskom, krojačkom, veziljskom i tkalačkom; oni tkaju tkanine od ljubičastog, crvenog i tamnocrvenog prediva i prepredenog lana, sposobni su u svakom poslu i vješti u nacrtima.

< Eksodo 35 >