< Eksodo 34 >

1 Yehova anati kwa Mose, “Sema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija, ndipo Ine ndidzalembapo mawu amene anali pa miyala yoyamba ija, imene unayiphwanya.
UThixo wathi kuMosi, “Baza ezinye izibhebhedu zamatshe ezimbili zifanane lezakuqala. Ngizabhala kuzo amazwi ayesezibhebhedwini zakuqala owaziphahlazayo.
2 Ukonzeke mmamawa, ndipo ubwere ku Phiri la Sinai. Udzaonekera pamaso panga pamwamba pa phiri.
Ube usulungile ekuseni, ubuye phezulu entabeni iSinayi, uziveze kimi engqongweni yentaba.
3 Palibe amene abwere nawe kapena kuoneka pena paliponse pafupi ndi phiri. Ndipo ngakhale nkhosa kapena ngʼombe zisadye mʼmbali mwa phirilo.”
Akungabi lamuntu oza lawe kumbe oke abonakale loba kungaphi entabeni; ngitsho lezimvu lenkomo kazingadli phambi kwaleyontaba.”
4 Choncho Mose anasema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija ndipo anapita ku Phiri la Sinai mmawa atanyamula miyala iwiri mʼmanja mwake monga momwe Yehova anamulamulira.
Ngakho uMosi wabaza izibhebhedu zamatshe ezimbili zaba njengezakuqala, wakhwela entabeni iSinayi ekuseni kakhulu njengokulaywa kwakhe nguThixo ephethe izibhebhedu ezimbili zamatshe ezandleni zakhe.
5 Ndipo Yehova anatsika mu mtambo ndi kuyima pamodzi ndi Mose ndi kulengeza dzina lake lakuti Yehova.
UThixo wehla ngeyezi wema khonapho laye wamemezela ibizo lakhe esithi, “UThixo.”
6 Ndipo Iye anadutsa kutsogolo kwa Mose akulengeza kuti, “Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima, wosapsa mtima msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika,
Wedlula phambi kukaMosi ememezela esithi, “UThixo, uThixo; uNkulunkulu olesihawu lomusa, ophuzayo ukuthukuthela, ogcwele uthando lobuqotho,
7 waonetsa chikondi chosasinthika kwa anthu miyandamiyanda, wokhululukira zoyipa, kuwukira, ndiponso tchimo, komatu salekerera ochimwa kuti asalangidwe. Iye amalanga ana ndi zidzukulu chifukwa cha machimo a makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi.”
olothando olungapheliyo kuzinkulungwane ethethelela ububi, iziphosiso lezono. Ikanti abalamacala kabayekeli bengajeziswanga; wehlisela ububi baboyise phezu kwabantwana, laphezu kwabantwana babantwana kusiya kusizukulwane sesithathu lesesine.”
8 Pamenepo Mose anawerama pansi napembedza.
UMosi waphanga wakhothamisela ikhanda lakhe phansi, wakhonza.
9 Iye anati, “Chonde Ambuye, ngati ndapeza chisomo pamaso panu, lolani Ambuye kuti mupite nafe pamodzi. Ngakhale kuti anthuwa ndi nkhutukumve, khululukirani zoyipa ndi machimo athu, ndipo mutenge ife kukhala anthu anu.”
Wathi, “Awu Thixo, nxa ngithole umusa kuwe, ngiyacela, uThixo kahambe lathi. Lanxa abantu laba bentamo zilukhuni, sithethelele ububi bethu lezono zethu, usithathe njengelifa lakho.”
10 Choncho Yehova anati: “Ine ndikuchita nanu pangano. Ndidzachita zodabwitsa pamaso pa anthu onse zimene sizinachitikenso ndi mtundu wina uliwonse wa anthu pa dziko lonse lapansi. Anthu amene mudzakhala pakati pawo adzaona kuopsa kwa ntchito imene Ine Yehova ndidzakuchitireni.
UThixo wasesithi, “Sengisenza isivumelwano lawe. Phambi kwabantu bakho bonke ngizakwenza izimangaliso ezingakaze zenziwe lanini lakusiphi isizwe emhlabeni wonke. Abantu ohlala phakathi kwabo bazabona ukuthi umangalisa njani umsebenzi, mina Thixo, engizakwenzela wona.
11 Mverani zimene ndikukulamulirani lero. Ine ndidzathamangitsa pamaso panu Aamori, Akanaani, Ahiti, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi.
Lalela lokhu engikulaya khona lamhla. Ngizawaxotsha phambi kwakho ama-Amori, amaKhenani, amaHithi, amaPherizi, amaHivi lamaJebusi.
12 Musamale kuti musakachite mgwirizano ndi anthu amene akukhala mʼdziko limene mukupitalo, chifukwa mukadzatero iwo adzakhala ngati msampha pakati panu.
Qaphela ukuba kungabi lesivumelwano osenza lalabo abahlala elizweni oya kulo ngoba bangaba yisifu kini.
13 Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, ndipo mukadule mitengo yawo ya Asera.
Adilizeni ama-alithare abo, libhidlize lezithombe zabo, liqume lezinsika zika-Ashera wabo abamkhonzayo.
14 Musapembedze mulungu wina, pakuti Yehova amene dzina lake ndi Nsanje, ndi Mulungu wa nsanje.
Lingakhonzi omunye unkulunkulu, ngoba uThixo, obizo lakhe linguBukhwele, nguNkulunkulu olobukhwele.
15 “Musamale kuti musakachite mgwirizano ndi anthu amene akukhala mʼdziko limene mukupitalo, chifukwa iwo akamakachita zadama ndi milungu yawo ndi kupereka nsembe, adzakuyitanani ndipo inu mudzadya nsembe zawo.
Qaphelani lingenzi isivumelwano lalabo abahlala elizweni lelo ngoba nxa bephinga labonkulunkulu babo benikela iminikelo kubo, bazalinxusa beselisidla imihlatshelo yabo.
16 Ndipo inu mukasankha ena mwa ana awo aakazi kukhala akazi a ana anu, akaziwo akakachita zadama ndi milungu yawo, akatsogolera ana anu aamuna kuchita chimodzimodzi.
Njalo lapho likhetha amanye amadodakazi abo ukuba abe ngabafazi bamadodana enu kuzakuthi lapho amadodakazi lawo esezibhixa kubonkulunkulu bawo, ahugele amadodana enu ekwenzeni okunjalo.
17 “Musadzipangire milungu yosungunula.
Lingazenzeli onkulunkulu ababunjiweyo.
18 “Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga momwe ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi pa nthawi yoyikika mwezi wa Abibu, pakuti mwezi umenewu inu munatuluka mʼdziko la Igupto.
Gcinani uMkhosi weSinkwa esingelaMvubelo. Okwensuku eziyisikhombisa dlanini isinkwa esenziwe kungekho mvubelo, njengokulaya kwami. Lokho kwenzeni ngesikhathi esimisiweyo enyangeni ka-Abhibhi, ngoba ngaleyonyanga laphuma eGibhithe.
19 “Mwana aliyense woyamba kubadwa ndi wanga, pamodzi ndi ziweto zoyamba kubadwa zazimuna kuchokera ku ngʼombe kapena nkhosa.
Inzalo yakuqala yonke ezelweyo ngeyami, kanye lamazibulo wonke amaduna ezifuyo zenu, loba engawenkomo kumbe awezimvu.
20 Muziwombola mwana woyamba kubadwa wa bulu popereka mwana wankhosa. Mukapanda kumuwombola mupheni. Muziwombola ana anu onse aamuna. “Palibe ndi mmodzi yemwe adzaonekere pamaso panga wopanda kanthu mʼdzanja lake.
Izibulo likababhemi lihlengeni ngezinyane. Kodwa nxa lingangalihlengi lephuleni intamo yalo. Ahlengeni wonke amadodana enu angamazibulo. Kakho ozakuza phambi kwami engaphethe lutho.
21 “Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri, musagwire ntchito ina iliyonse, Ngakhale nthawi yolima ndi yokolola muyenera kupuma.
Lizasebenza insuku eziyisithupha, kodwa ngosuku lwesikhombisa lizaphumula; langesikhathi sokulima lesokuvuna kuzamele liphumule.
22 “Muzichita Chikondwerero cha Masabata, chifukwa ndi chikondwerero cha tirigu woyambirira kucha, ndiponso ndi chikondwerero cha kututa zokolola pakutha pa chaka.
Thakazelelani uMkhosi wamaViki lokolibo kokuvuna kwenu ingqoloyi loMkhosi wokuButhelela ekupheleni komnyaka.
23 Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu wa Israeli, katatu pa chaka.
Kathathu ngomnyaka bonke abesilisa bakho kumele babonakale phambi kukaThixo Wobukhosi, uNkulunkulu ka-Israyeli.
24 Ine ndidzapirikitsa mitundu inayo pamene inu mukufikako ndi kukulitsa malire anu. Palibe ndi mmodzi yemwe adzafune kulanda dziko lanu ngati inu muzidzapita katatu pa chaka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, chaka chilichonse.
Ngizaxotsha izizwe eziphambi kwenu njalo ngiqhelise ilizwe lenu, kakho ozahawukela ilizwe lenu ngesikhathi lisiyabonakala kathathu ngomnyaka phambi kukaThixo uNkulunkulu wenu.
25 “Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti, ndipo musasunge nsembe ya pa Chikondwerero cha Paska mpaka mmawa.
Linganikeli igazi lomhlatshelo kimi ndawonye laloba yini elemvubelo, njalo akungabi lomhlatshelo woMkhosi wePhasika ogcinwa kuze kuse.
26 “Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu. “Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.”
Lethani okolibo kwenu okuhle kakhulu endlini kaThixo uNkulunkulu wenu. Lingapheki izinyane lembuzi ngochago lukanina.”
27 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba mawu awa pakuti potsatira mawuwa, ine ndipangana pangano ndi iwe ndi Israeli.”
UThixo wasesithi kuMosi, “Loba amazwi la, ngoba ngamazwi la sengenze isivumelwano lawe kanye lo-Israyeli.”
28 Mose anakhala kumeneko pamodzi ndi Yehova masiku 40, usana ndi usiku, wosadya kanthu kapena kumwa madzi. Ndipo iye analemba pa miyala ija mawu a pangano, malamulo khumi.
UMosi wayekhonale loThixo insuku ezingamatshumi amane lobusuku obungamatshumi amane engadli sinkwa kumbe ukunatha amanzi. Amazwi esivumelwano ayimiThetho eliTshumi, wawaloba ezibhebhedwini zamatshe.
29 Mose anatsika kuchokera mʼPhiri la Sinai pamodzi ndi miyala iwiri ija ya pangano mʼmanja mwake. Iye sanazindikire kuti nkhope yake imanyezimira pakuti anayankhula ndi Yehova.
Kwathi lapho uMosi esehla entabeni yeSinayi ephethe izibhebhedu ezimbili zamatshe obufakazi, wayengazi ukuthi ubuso bakhe babukhazimula ngenxa yokuthi wayekhulume loThixo.
30 Aaroni ndi Aisraeli ataona kuti nkhope ya Mose imanyezimira anaopa kumuyandikira.
Kwathi u-Aroni labo bonke abako-Israyeli bebona uMosi, ubuso bakhe bukhazimula, besaba ukusondela kuye.
31 Koma Mose anawayitana. Kotero Aaroni ndi atsogoleri onse a gululo anabwera kwa iye, ndipo anawayankhula.
Kodwa uMosi wababiza; ngakho u-Aroni lezinduna zonke zabantu beza kuye, wakhuluma labo.
32 Kenaka Aisraeli onse anamuyandikira, ndipo anawapatsa malamulo onse omwe Yehova anamupatsa pa Phiri la Sinai.
Emva kwalokho bonke abako-Israyeli basondela kuye wabanika yonke imilayo kaThixo ayemuphe yona entabeni yeSinayi.
33 Mose atamaliza kuyankhula nawo anaphimba nkhope yake.
UMosi eseqedile ukukhuluma labo, wamboza ubuso bakhe ngeveli.
34 Koma nthawi zonse popita pamaso pa Yehova kukayankhula naye amachotsa chophimbacho mpaka atatuluka. Ndipo akatuluka kudzawuza Aisraeli zimene walamulidwa,
Kodwa kwakusithi lapho esengena ukuba abe phambi kukaThixo ukuze akhulume laye, wayelisusa iveli aze aphume. Wayesithi angaphuma, njalo esebatshelile abako-Israyeli lokho ayekulayiwe,
35 iwo amaona nkhope yake ikunyezimira. Choncho Mose amaphimba nkhope yake ngakhale pamene amapita kukayankhula ndi Yehova.
babebona ukuthi ubuso bakhe babukhazimula. Lapho-ke uMosi wayebumboza njalo ubuso bakhe ngeveli aze angene esiyakhuluma loThixo.

< Eksodo 34 >