< Eksodo 33 >

1 Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’
UThixo wasesithi kuMosi, “Suka kule indawo wena labantu owabakhupha elizweni laseGibhithe, uye elizweni engalithembisa u-Abhrahama lo-Isaka loJakhobe ngifunga ngisithi, ‘Ngizalinika inzalo yakho.’
2 Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
Ngizathuma ingilosi ihambe phambi kwakho ixotshe amaKhenani, ama-Amori, amaHithi, amaPherizi, amaHivi lamaJebusi.
3 Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”
Yana elizweni eligeleza uchago loluju. Kodwa mina angiyikuhamba lani ngoba lingabantu abantamo zilukhuni, hlezi ngilibhubhise endleleni.”
4 Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera.
Kwathi lapho abantu sebezwe amazwi la adabukisayo baqalisa ukukhala, akwaze kwaba loyedwa owagqiza izigqizo zakhe.
5 Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.”
Phela uThixo wayethe kuMosi, “Tshela abako-Israyeli uthi, ‘Lina lingabantu abantamo zilukhuni. Nxa ngingahamba lani loba okomzuzwana nje, ngingalibhubhisa. Khathesi khululani izigqizo zenu; ngizakwenza isinqumo ukuthi ngenzeni ngani.’”
6 Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.
Ngakho-ke abako-Israyeli bazikhipha izigqizo zabo entabeni yeHorebhi.
7 Tsono Mose ankatenga tenti ndi kukayimanga kunja kwa msasa chapatalipo, ndipo ankayitcha “tenti ya msonkhano.” Aliyense wofuna kukafunsa kanthu kwa Yehova amapita ku tenti ya msonkhano kunja kwa msasa.
UMosi wayejwayele ukuthatha ithente ayelimisa ngaphandle bucwadlana lezihonqo. Walibiza ngokuthi “lithente lokuhlangana.” Ubani lobani owayedinga uThixo wayesiya ethenteni lokuhlangana ngaphandle kwezihonqo.
8 Ndipo nthawi ina iliyonse imene Mose amapita ku tenti anthu onse amanyamuka ndi kuyimirira pa makomo amatenti awo, kumuyangʼana Mose mpaka atalowa mu tentimo.
Kwakusithi-ke lapho uMosi ephuma esiya kulelothente abantu bonke babesukuma bame eminyango yamathente abo bakhangele uMosi aze angene ethenteni.
9 Mose akamalowa mu tenti, chipilala cha mtambo chimatsika ndi kukhala pa khomo pamene Yehova amayankhula ndi Mose.
Kwakusithi uMosi esengena ethenteni insika yeyezi yehlele phansi ime emnyango wethente lapho uThixo ekhuluma loMosi.
10 Nthawi zonse anthu akaona chipilala cha mtambo chitayima pa khomo la tentiyo amayimirira ndi kupembedza, aliyense ali pa khomo la tenti yake.
Kwakusithi abantu bangabona insika yeyezi isimi emnyango wethente basukume bonke bakhonze; lowo lalowo emnyango wethente lakhe.
11 Yehova amayankhula ndi Mose maso ndi maso ngati mmene munthu amayankhulira ndi bwenzi lake. Kenaka Mose amabwerera ku msasa koma womuthandiza wake, Yoswa, mwana wa Nuni samachoka pa tentiyo.
UThixo wayekhuluma loMosi ubuso ngobuso njengomuntu ekhuluma lomngane wakhe. Ngemva kwalokho uMosi wayebuyela ezihonqweni, kodwa umncedisi wakhe owayesesemncane, uJoshuwa indodana kaNuni, wayengasuki ethenteni.
12 Mose anati kwa Yehova, “Inu mwakhala mukundiwuza kuti, ‘Tsogolera anthu awa,’ koma simunandiwuze amene mudzamutuma kuti apite pamodzi nane. Inu mwanena kuti, ‘Ndikukudziwa bwino kwambiri ndipo wapeza chisomo pamaso panga.’
UMosi wathi kuThixo, “Ubulokhu ungitshela usithi, ‘Khokhela abantu laba,’ kodwa kawungazisanga ukuthi ngubani ozamthuma ukuba ahambe lami. Utshilo wathi, ‘Ngiyakwazi ngebizo, njalo ufumene umusa kimi.’
13 Ngati mwakondwera nane ndiphunzitseni njira zanu kuti ndikudziweni ndi kupitiriza kupeza chisomo pamaso panu. Kumbukirani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.”
Nxa uthokoza ngami, ngifundisa izindlela zakho ukuze ngikwazi, ngiqhubeke ngithola umusa kuwe. Khumbula futhi lokuthi isizwe lesi singabantu bakho.”
14 Yehova anayankha kuti, “Ine ndemwe ndidzapita pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakupatsa mpumulo.”
UThixo waphendula wathi, “NgoBukhona bami ngizahamba lawe ngikuphumuze.”
15 Kenaka Mose anati kwa Yehova, “Ngati inu simupita nafe, musatitumize kuti tipite, kutichotsa pano.
UMosi wathi kuye, “Nxa uBukhona bakho bungahambi lathi, ungasisusi lapha.
16 Kodi wina adzadziwa bwanji kuti inu mwandikomera mtima pamodzi ndi anthu awa ngati simupita nafe? Kodi nʼchiyani chomwe chidzatisiyanitse pakati pa anthu onse amene ali pa dziko lapansi?”
Umuntu angakwazi njani ukuthi mina labantu bakho sifumene umusa kuwe ngaphandle kokuba uhamba lathi na? Kuyini okunye okungasiphawula, mina labantu bakho, kwabanye abantu bonke emhlabeni na?”
17 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzachita zimene iwe wandipempha chifukwa Ine ndikukondwera nawe, ndikukudziwa bwino lomwe.”
UThixo wathi kuMosi, “Ngizakwenza khona kanye lokhu okucelileyo ngoba ngiyathokoza ngawe, njalo ngikwazi ngebizo.”
18 Kenaka Mose anati, “Tsopano ndionetseni ulemerero wanu.”
UMosi wasesithi, “Ngicela ukuba ungitshengise inkazimulo yakho.”
19 Ndipo Yehova anati, “Ine ndidzakuonetsa ulemerero wanga wonse ndipo ndidzatchula dzina langa lakuti Yehova pamaso pako. Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
UThixo wasesithi, “Ngizakwenza ukulunga kwami kudlule phambi kwakho, njalo ngizamemezela ibizo lami, uThixo, phambi kwakho. Ngizakuba lesihawu kulowo engizakuba lesihawu kuye njalo ngibe lesisa kulowo engizakuba lesisa kuye.”
20 Iye anati, “Koma iwe sungaone nkhope yanga, pakuti palibe munthu amene amaona Ine nakhala ndi moyo.”
UThixo waqhubeka wathi, “Kodwa, ubuso bami awungeke ububone, ngoba kakho ongangibona aphile.”
21 Ndipo Yehova anati, “Pali malo pafupi ndi ine pomwe ungathe kuyima pa thanthwe.
UThixo wabuya wathi, “Kulendawo phansi kwami lapho ongema khona phezu kwedwala.
22 Pamene ulemerero wanga udutsa, ndidzakuyika mʼphanga la thanthwe ndi kukuphimba ndi dzanja langa mpaka nditadutsa.
Kuzakuthi lapho inkazimulo yami isedlula eduze, ngizakufaka emnkenkeni wedwala ngikusithe ngesandla sami ngize ngidlule.
23 Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”
Emva kwalokho ngizasusa isandla sami ubone umhlane wami; kodwa ubuso bami akumelanga ububone.”

< Eksodo 33 >