< Eksodo 33 >

1 Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’
Yahweh said to Moses/me, “Leave this place and go with the people whom you led out of Egypt. Go to the land that I promised Abraham, Isaac, and Jacob that I would give to their descendants.
2 Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
I will send my angel ahead of you all, and I will expel [from that land] the Canaan, Amor, Heth, Periz, Hiv, and Jebus people-groups.
3 Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”
You will go to a land that will be very good for raising livestock and growing crops [IDM]. But I will not go with you myself, because [if I did that], I might get rid of you while you are traveling, because you are very stubborn [IDM] people.”
4 Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera.
Yahweh said to Moses/me, “Tell the Israeli people, ‘You are very stubborn [IDM]. If I would go with you for even a moment, I would completely (get rid of you/wipe you out). Now take off your jewelry [to show that you are sorry for having sinned]. Then I will decide how I will punish you (OR, if I should punish you).’” So when Moses/I told to the people what God said, they started to mourn, and they all took off their jewelry.
5 Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.”
6 Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.
After the Israeli people left Sinai Mountain, they did not wear jewelry any more.
7 Tsono Mose ankatenga tenti ndi kukayimanga kunja kwa msasa chapatalipo, ndipo ankayitcha “tenti ya msonkhano.” Aliyense wofuna kukafunsa kanthu kwa Yehova amapita ku tenti ya msonkhano kunja kwa msasa.
[When the Israeli people traveled], whenever they stopped and set up their tents, Moses/I had them set up a tent outside the camp, far from the camp. I called it ‘the Sacred Tent where God and I talk together’. Everyone who wanted Yahweh to decide something for them would go out of the camp to the Sacred Tent.
8 Ndipo nthawi ina iliyonse imene Mose amapita ku tenti anthu onse amanyamuka ndi kuyimirira pa makomo amatenti awo, kumuyangʼana Mose mpaka atalowa mu tentimo.
Whenever Moses/I went out to the Sacred Tent, all the people would stand at the entrances of their tents and watch him/me until he/I had entered the Sacred Tent.
9 Mose akamalowa mu tenti, chipilala cha mtambo chimatsika ndi kukhala pa khomo pamene Yehova amayankhula ndi Mose.
When Moses/I entered the Sacred Tent, the tall cloud that looked like a fire would come down and stay at the entrance of the Sacred Tent, and then Yahweh would talk with Moses/me.
10 Nthawi zonse anthu akaona chipilala cha mtambo chitayima pa khomo la tentiyo amayimirira ndi kupembedza, aliyense ali pa khomo la tenti yake.
When the people saw the tall cloud at the entrance of the Sacred Tent, they would all prostrate themselves on the ground and worship Yahweh.
11 Yehova amayankhula ndi Mose maso ndi maso ngati mmene munthu amayankhulira ndi bwenzi lake. Kenaka Mose amabwerera ku msasa koma womuthandiza wake, Yoswa, mwana wa Nuni samachoka pa tentiyo.
Yahweh would speak to Moses/me directly, like someone speaks to his friend. Then Moses/I would return to the camp. But his/my young helper, Joshua, the son of Nun, stayed in the Sacred Tent.
12 Mose anati kwa Yehova, “Inu mwakhala mukundiwuza kuti, ‘Tsogolera anthu awa,’ koma simunandiwuze amene mudzamutuma kuti apite pamodzi nane. Inu mwanena kuti, ‘Ndikukudziwa bwino kwambiri ndipo wapeza chisomo pamaso panga.’
Moses/I said to Yahweh, “It is true that you have told me, ‘Lead the people to the land [that I will show you],’ and you have said that you know me well and that you are pleased with me, but you have not told me whom you will send with me!
13 Ngati mwakondwera nane ndiphunzitseni njira zanu kuti ndikudziweni ndi kupitiriza kupeza chisomo pamaso panu. Kumbukirani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.”
So now, if you are truly pleased with me, I ask you, tell me the things that you intend/plan to do, in order that I will know you [better] and continue to please you. Also, do not forget that the [Israeli] people are the people whom you chose to belong to you.”
14 Yehova anayankha kuti, “Ine ndemwe ndidzapita pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakupatsa mpumulo.”
Yahweh replied, “I will go with you, and I will give you inner peace.”
15 Kenaka Mose anati kwa Yehova, “Ngati inu simupita nafe, musatitumize kuti tipite, kutichotsa pano.
Moses/I replied, “If you do not go with me, do not force us to leave this place.
16 Kodi wina adzadziwa bwanji kuti inu mwandikomera mtima pamodzi ndi anthu awa ngati simupita nafe? Kodi nʼchiyani chomwe chidzatisiyanitse pakati pa anthu onse amene ali pa dziko lapansi?”
The only way that [other] people will know that you are pleased with me and with your people is if you go with us [RHQ]! (If you go with us, [that will show that] we are different from all the other people on the earth./If you do not go with us, what will show that we are different from all the other people on the earth?)” [RHQ]
17 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzachita zimene iwe wandipempha chifukwa Ine ndikukondwera nawe, ndikukudziwa bwino lomwe.”
Yahweh replied to Moses/me, “What you have asked is exactly what I will do, because I know you well and I am pleased with you.”
18 Kenaka Mose anati, “Tsopano ndionetseni ulemerero wanu.”
Then Moses/I said, “Please let me see your glorious presence!”
19 Ndipo Yehova anati, “Ine ndidzakuonetsa ulemerero wanga wonse ndipo ndidzatchula dzina langa lakuti Yehova pamaso pako. Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
Yahweh replied, “I will let you see how great and glorious I am, and I will tell you clearly that my name is Yahweh. I will act very kindly and be merciful to all those whom I choose.
20 Iye anati, “Koma iwe sungaone nkhope yanga, pakuti palibe munthu amene amaona Ine nakhala ndi moyo.”
But you are not allowed to see my face, because anyone who sees my face will (die/not continue to stay alive).
21 Ndipo Yehova anati, “Pali malo pafupi ndi ine pomwe ungathe kuyima pa thanthwe.
[But look]! Here is a place close to me where you can stand on a [large] rock.
22 Pamene ulemerero wanga udutsa, ndidzakuyika mʼphanga la thanthwe ndi kukuphimba ndi dzanja langa mpaka nditadutsa.
When my glorious presence comes past you, I will put you in a large crevice/opening in the rock, and I will cover your face with my hand until I have passed by.
23 Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”
Then I will take my hand away, and you will see my back, but you will not see my face.”

< Eksodo 33 >