< Eksodo 31 >
1 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
2 “Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
»Poglej, po imenu sem poklical Becaléla, Urijájevega sina, Hurovega sina, iz Judovega rodu.
3 Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
Napolnil sem ga z Božjim duhom, v modrosti, v razumnosti, v znanju in v vseh vrstah rokodelstva,
4 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
da snuje spretna dela, da dela z zlatom, s srebrom, z bronom
5 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
in v rezanju kamnov, da se jih vdela in v rezbarjenju lesa, da dela v vseh vrstah rokodelstva.
6 Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
Glej, jaz sem dal z njim Oholiába, Ahisamáhovega sina, iz Danovega rodu, in v srca vseh tistih, ki so modrega srca, sem položil modrost, da bodo lahko naredili vse to, kar sem ti zapovedal:
7 Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
šotorsko svetišče skupnosti, skrinjo pričevanja, sedež milosti, ki je na njem, vso opremo šotorskega svetišča,
8 tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
mizo in njeno opremo, čisti svečnik z vso njegovo opremo, kadilni oltar,
9 guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
oltar žgalne daritve z vso njegovo opremo, [okrogel] umivalnik in njegovo vznožje,
10 ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
službene obleke in sveta oblačila za duhovnika Arona in oblačila njegovih sinov, za služenje v duhovniški službi
11 ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
ter mazilno olje in dišeče kadilo za sveti kraj. Storili bodo glede na vse to, kar sem ti zapovedal.«
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
13 “Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
»Govori tudi Izraelovim otrokom, rekoč; ›Resnično, ohranjali boste moje šabate, kajti to je znamenje med menoj in vami skozi vaše rodove, da boste vi lahko vedeli, da jaz sem Gospod, ki vas posvečujem.
14 “Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
Zato boste ohranjali šabat, kajti ta vam je svet. Vsak kdor ga omadežuje, ta bo zagotovo usmrčen, kajti kdorkoli v njem dela kakršnokoli delo, ta duša bo iztrebljena izmed svojega ljudstva.
15 Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
Šest dni naj se opravlja delo, toda na sedmi je šabatni počitek, sveto Gospodu. Kdorkoli na šabatni dan počne kakršno koli delo, bo zagotovo usmrčen.
16 Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
Zatorej bodo Izraelovi otroci ohranjali šabat, da šabat obeležujejo skozi njihove rodove za večno zavezo.
17 Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
To je znamenje med menoj in Izraelovimi otroki na veke, kajti v šestih dneh je Gospod naredil nebo in zemljo in na sedmi dan je počival in bil osvežen.‹«
18 Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.
Mojzesu je dal, ko je z njim končal posvetovanje na gori Sinaj, dve plošči pričevanja, kamniti plošči, popisani z Božjim prstom.