< Eksodo 31 >
1 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
UThixo wathi kuMosi,
2 “Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
“Khangela, sengikhethe uBhezaleli indodana ka-Uri oyindodana kaHuri owesizwe sikaJuda
3 Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
ngamgcwalisa ngomoya kaNkulunkulu, ukuhlakanipha, ukuqedisisa lolwazi ekwenzeni yonke imisebenzi yobungcitshi
4 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
ukuze adwebe imisebenzi yobungcitshi ngesimo sezinto ezenziwa ngegolide, isiliva kanye lethusi,
5 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
abaze amatshe awabeke kuhle, abaze izigodo kanye lokwenza yonke imisebenzi yomuntu oleminwe lobungcwethi.
6 Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
Phezu kwalokho, ngikhethe lo-Oholiyabhi indodana ka-Ahisamakhi, owesizwe sikaDani ukuba amncedise. Nginike ulwazi kuzozonke izingcitshi ukuba zenze konke engikulaye ukuba kwenziwe:
7 Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
ithente lokuhlangana, umtshokotsho wobufakazi, isihlalo somusa esikuwo, lakho konke okunye okokuhlobisa ithente:
8 tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
itafula lezitsha zalo, uluthi lwesibane lwegolide elicolekileyo lezitsha zalo zonke, i-alithari lempepha,
9 guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
i-alithari lomnikelo wokutshiswa kanye lezitsha zalo zonke, lomkolo kanye lezinyawo zawo
10 ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
lezembatho ezelukiweyo, lezembatho ezingcwele zika-Aroni umphristi kanye lezembatho zamadodana akhe ezomsebenzi wabo wobuphristi,
11 ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
lamafutha okugcobela isikhundla, lempepha enuka mnandi eyeNdawo eNgcwele. Kumele bakwenze njengoba ngikulayile.”
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
UThixo wasesithi kuMosi,
13 “Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
“Batshele abako-Israyeli uthi, ‘Kumele ligcine amaSabatha ami. Lokhu kuzakuba luphawu phakathi kwami lani kuzizukulwane zenu ezizayo, ukuze lazi ukuthi mina nginguThixo olenza libengcwele.
14 “Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
Gcinani iSabatha ngoba lingcwele kini. Lowo olonayo kumele abulawe, lalowo osebenzayo ngalolosuku uzasuswa ebantwini bakibo.
15 Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
Umsebenzi kawenziwe okwensuku eziyisithupha, kodwa usuku lwesikhombisa luliSabatha lokuphumula, lungcwele kuThixo. Lowo osebenzayo ngosuku lweSabatha kumele abulawe.
16 Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
Abako-Israyeli kumele bagcine iSabatha, baligcine kuzizukulwane zabo ezizayo njengesivumelwano esingapheliyo.
17 Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
Lizakuba luphawu phakathi kwami labako-Israyeli nini lanini. Ngoba ngezinsuku eziyisithupha uThixo wenza amazulu lomhlaba, kwathi ngosuku lwesikhombisa waphumula.’”
18 Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.
Kwathi lapho uThixo eseqedile ukukhuluma loMosi entabeni yaseSinayi wamnika izibhebhedu ezimbili zamatshe obufakazi, izibhebhedu zamatshe alotshwe ngomunwe kaNkulunkulu.