< Eksodo 31 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
OLELO mai o Iehova ia Mose, i mai la,
2 “Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
E nana hoi, ua kahea aku au ma ka inoa, ia Bezalela, i ke keiki a Uri, i ka keiki a Hura, no ka ohana a Iuda.
3 Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
A ua hoopiha au ia ia i ka uhane o ke Akua, ma ke akamai, ma ka naauao, ma ka ike, a ma ka hana ana i na mea a pau,
4 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
E imi i na mea akamai, e hana hoi ma ke gala, a ma ke kala, a ma ke keleawe,
5 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
A i ke okioki pohaku, i mea kapili: a i ke kalai ana i ka laau e hana hoi i na hana a pau.
6 Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
A owau, aia hoi, ua haawi no wau ia Aholiaba nona, i ke keiki a Ahisamaka, no ka ohana a Dana; a ua haawi no wau i ke akamai maloko o ka naau o ka poe a pau i naauao, i hana lakou i na mea a pau a'u i kauoha aku at ia oe:
7 Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
I ka halelewa o ke anaina kanaka, a me ka pahu kanawai, a me ka noho aloha maluna iho, a me ka oihana a pau o ka halelewa,
8 tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
A me ka papaaina, a me kona oihana, a me ka ipukukui, me kona oihana a pau, a me ke kuahu no ka mea ala,
9 guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
A me ke kuahu no ka mohaikuni a me kona oihana a pau, a me ka ipu auau, a me kona kumu,
10 ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
A me na lole hana, a me na kahiko laa no Aarona ke kahuna, a me na kahiko no kana mau keikikane e lawelawe ai ma ka oihana kahuna,
11 ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
A me ka aila poni, a mo ka mea ala maikai no kahi laa; e like me na mea a pau a'u i kauoha aku ai ia oe, pela laua e hana'i.
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
Olelo mai la o Iehova ia Mose, i mai la,
13 “Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
E olelo aku oe i na mamo a Iseraela, e i aku, E malama io oukou i ko'u mau sabati, no ka mea, he hoailona ia mawaena o'u a me oukou, i ko oukou mau hanauna; i ike hoi oukou, owau no Iehova, ka mea hoolaa ia oukou.
14 “Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
Nolaila oukou e malama'i i ka sabati; no ka mea, ua hoanoia ia no oukou, O kela mea keia mea hoohaumia ia la, e oiaio no e pepehiia oia: no ka mea, o ka mea hana i ka hana ia la, e okiia kela kanaka, mai kona poe kanaka aku.
15 Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
Eono la e hanain'i ka hana, aka o ka hiku, he sabati ia e hoomaha'i, he mea laa no Iehova, o ka mea hana i kekahi hana i ka sabati, e oiaio no e pepehiia oia.
16 Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
A e malama na mamo a Iseraela i ka sabati e hooponopono i ka sabati, i ko lakou hanauna, i berita mau loa.
17 Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
He hoailona mau loa ia mawaena o'u a me na mamo a Iseraela; no ka mea, i na la eono i hana'i o Iehova i ka lani, a me ka honua, a i ka hiku o ka la, hoomaha oia, a oluolu iho la,
18 Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.
A i kona hoopau ana i ke kamailio me Mose, maluna o ka mauna o Sinai, haawi mai la oia ia ia i elua papa kanawai he mau papa pohaku, ua kahakahaia e ka lima o ke Akua.

< Eksodo 31 >