< Eksodo 31 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
See I have called by name Bezalel [the] son of Uri [the] son of Hur of [the] tribe of Judah.
3 Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
And I have filled him [the] spirit of God with skill and with understanding and with knowledge and with all workmanship.
4 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
To design designs to work in gold and in silver and in bronze.
5 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
And in carving of stone to fill and in carving of wood to work in all workmanship.
6 Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
And I here! I have appointed with him Oholiab [the] son of Ahisamach of [the] tribe of Dan and in [the] heart of every [person] skillful of heart I have put skill and they will make all that I have commanded you.
7 Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
- [the] tent of Meeting and the ark of the testimony and the atonement cover which [will be] on it and all [the] articles of the tent.
8 tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
And the table and articles its and the lampstand pure and all articles its and [the] altar of incense.
9 guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
And [the] altar of the burnt offering and all articles its and the laver and base its.
10 ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
And [the] garments of the woven material and [the] garments of the holiness for Aaron the priest and [the] garments of sons his to serve as priests.
11 ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
And [the] oil of anointing and [the] incense of the perfume for the holy place according to all that I have commanded you they will do.
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
And he said Yahweh to Moses saying.
13 “Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
And you speak to [the] people of Israel saying surely sabbaths my you will observe for [is] a sign it between me and between you to generations your to know that I [am] Yahweh [who] sets apart you.
14 “Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
And you will observe the sabbath for [is] a holy thing it to you [those who] profane it certainly he will be put to death for every [one who] does on it work and it will be cut off the person that from [the] midst of kinspeople its.
15 Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
Six days it will be done work and [will be] on the day seventh a sabbath of sabbath observance a holy thing to Yahweh every [one who] does work on [the] day of the sabbath certainly he will be put to death.
16 Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
And they will observe [the] people of Israel the sabbath by celebrating the sabbath to generations their a covenant of perpetuity.
17 Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
Between me and between [the] people of Israel [is] a sign it for ever for six days he made Yahweh the heavens and the earth and on the day seventh he rested and he refreshed himself.
18 Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.
And he gave to Moses when finished he to speak with him on [the] mountain of Sinai [the] two [the] tablets of the testimony tablets of stone written by [the] finger of God.

< Eksodo 31 >