< Eksodo 31 >
1 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
2 “Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
See, I have called by name Bezalel the son of Uri, the son of Chur, of the tribe of Judah:
3 Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
And I have filled him with the spirit of God, in wisdom, and in understanding, and in knowledge, and in all manner of workmanship,
4 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
To devise works of art, to work in gold, and in silver, and in copper,
5 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
And in the cutting of stones, to set them, and in the carving of wood, to work in all manner of workmanship.
6 Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
And behold, I have also given with him Aholiab, the son of Achissamach, of the tribe of Dan, and in the heart of all that are wise-hearted have l put wisdom; and they shall make all that I have commanded thee;
7 Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
The tabernacle of the congregation, and the ark of the testimony, and the cover that is thereupon, and all the vessels of the tabernacle;
8 tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
And the table and its vessels, and the pure candlestick with all its vessels, and the altar of incense;
9 guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
And the altar of burnt-offering with all its vessels, and the laver and its foot;
10 ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
And the cloths of service, and the holy garments for Aaron the priest, and the garments of his sons, to minister therein;
11 ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
And the anointing oil, and the incense of spices for the holy place: all as I have commanded thee shall they do.
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
And the Lord said unto Moses as followeth,
13 “Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
And thou shalt speak unto the children of Israel, saying, Above all, my sabbaths shall ye keep; for a sign it is between me and you throughout your generations; that ye may know that I am the Lord who doth sanctify you.
14 “Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
And ye shall keep the sabbath, for it is holy unto you; every one that defileth it shall surely be put to death; for whosoever doeth any work thereon, that soul shall be cut off from among his people.
15 Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
Six days may work be done; but on the seventh is the sabbath of rest, holy to the Lord: whosoever doeth any work on the sabbath-day, shall surely be put to death.
16 Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
And the children of Israel shall keep the sabbath, to observe the sabbath throughout their generations, for a perpetual covenant.
17 Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
Between me and the children of Israel it shall be a sign for ever; for in six days the Lord made the heavens and the earth, and on the seventh day he rested, and was refreshed:
18 Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.
And he gave unto Moses, when he had finished speaking with him upon mount Sinai, the two tables of the testimony, tables of stone, inscribed with the finger of God.