< Eksodo 31 >
1 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
Og Herren talede til Mose og sagde:
2 “Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
Se, jeg har kaldet Bezaleel, en Søn af Uri, som var en Søn af Hur, af Juda Stamme, ved Navn.
3 Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
Og jeg har opfyldt ham med Guds Aand, med Visdom og med Forstand og med Kundskab, og det i alle Haande Gerning,
4 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
til at udtænke Kunstværker, til at arbejde i Guld og i Sølv og i Kobber
5 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
og til at udskære Stene, til at indfatte, og til at udskære Træ, til at gøre alle Haande Gerning.
6 Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
Og jeg, se, jeg har medgivet ham Oholiab, Ahisamaks Søn af Dans Stamme, og i hvers Hjerte, som er forstandig, har jeg givet Visdom; og de skulle gøre alt det, som jeg har befalet dig:
7 Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
Nemlig Forsamlingens Paulun og Vidnesbyrdets Ark og Naadestolen, som er derpaa, og alt Redskab til Paulunet,
8 tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
og Bordet med dets Redskab og den rene Lysestage med alt dens Redskab og Røgelsealteret
9 guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
og Brændofferets Alter med alt dets Redskab og Kedelen med dens Fod
10 ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
og Tjenestens Klæder og Arons, Præstens, hellige Klæder og hans Sønners Klæder til at gøre Præstetjeneste udi
11 ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
og Salveolien og Røgelsen af vellugtende Urter til Helligdommen; efter alt det, som jeg har befalet dig, skulle de gøre det.
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose,
Og Herren talede til Mose og sagde:
13 “Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
Og du, tal til Israels Børn og sig: I skulle visselig holde mine Sabbater; thi det er et Tegn imellem mig og imellem eder hos eders Efterkommere, at I skulle vide, at jeg er Herren, som helliger eder.
14 “Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
Derfor skulle I holde Sabbaten, thi den skal være eder hellig; den der vanhelliger den, skal visselig dødes; thi hver som gør Arbejde paa den, den Sjæl skal udryddes af sit Folks Midte.
15 Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
Seks Dage skal al Gerning gøres, men paa den syvende Dag er Sabbatshvile, en Hellighed for Herren; hver den, som gør Arbejde paa Sabbatsdagen, skal visselig dødes.
16 Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
Derfor skulle Israels Børn tage Vare paa Sabbaten, saa at de holde Sabbaten, hos deres Efterkommere til en evig Pagt.
17 Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
Den er et evigt Tegn imellem mig og imellem Israels Børn; thi i seks Dage gjorde Herren Himmelen og Jorden, og paa den syvende Dag hvilede han og vederkvægede sig.
18 Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.
Og han gav Mose, der han havde endt at tale med ham paa Sinai Bjerg, to Vidnesbyrdets Tavler, Stentavler, skrevne med Guds Finger.