< Eksodo 28 >

1 “Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe.
"Bring Aaron your brother, and his sons with him, near to you from among the children of Israel, that he may minister to me in the priest's office, even Aaron, Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar, Aaron's sons.
2 Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka.
You shall make holy garments for Aaron your brother, for glory and for beauty.
3 Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe.
You shall speak to all who are wise-hearted, whom I have filled with the spirit of wisdom, that they make Aaron's garments to sanctify him, that he may minister to me in the priest's office.
4 Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe.
These are the garments which they shall make: a breastplate, and an ephod, and a robe, and a coat of checker work, a turban, and a sash: and they shall make holy garments for Aaron your brother, and his sons, that he may minister to me in the priest's office.
5 Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.
They shall take the gold, and the blue, and the purple, and the scarlet, and the fine linen.
6 “Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso.
"They shall make the ephod of gold, of blue, and purple, scarlet, and fine twined linen, the work of the skillful workman.
7 Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
It shall have two shoulder straps joined to the two ends of it, that it may be joined together.
8 Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.
The skillfully woven band, which is on it, that is on him, shall be like its work and of the same piece; of gold, of blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen.
9 “Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli.
You shall take two onyx stones, and engrave on them the names of the sons of Israel:
10 Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo.
six of their names on the one stone, and the names of the six that remain on the other stone, in the order of their birth.
11 Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide.
With the work of an engraver in stone, like the engravings of a signet, you shall engrave the two stones, according to the names of the sons of Israel: you shall make them to be enclosed in settings of gold.
12 Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.
You shall put the two stones on the shoulder straps of the ephod, to be stones of memorial for the sons of Israel: and Aaron shall bear their names before the LORD on his two shoulders for a memorial.
13 Upange zoyikamo za maluwa agolide,
You shall make settings of gold,
14 ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.
and two chains of pure gold; you shall make them like cords of braided work: and you shall put the braided chains on the settings.
15 “Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
"You shall make a breastplate of judgment, the work of the skillful workman; like the work of the ephod you shall make it; of gold, of blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen, you shall make it.
16 Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri.
It shall be square and folded double; a span shall be its length of it, and a span its breadth.
17 Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili.
You shall set in it settings of stones, four rows of stones: a row of ruby, topaz, and beryl shall be the first row;
18 Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
and the second row a turquoise, a sapphire, and an emerald;
19 mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti.
and the third row a jacinth, an agate, and an amethyst;
20 Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide.
and the fourth row a chrysolite, an onyx, and a jasper: they shall be enclosed in gold in their settings.
21 Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
The stones shall be according to the names of the sons of Israel, twelve, according to their names; like the engravings of a signet, everyone according to his name, they shall be for the twelve tribes.
22 “Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
You shall make on the breastplate chains like cords, of braided work of pure gold.
23 Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa.
You shall make on the breastplate two rings of gold, and shall put the two rings on the two ends of the breastplate.
24 Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
You shall put the two braided chains of gold in the two rings at the ends of the breastplate.
25 Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
The other two ends of the two braided chains you shall put on the two settings, and put them on the shoulder straps of the ephod in its forepart.
26 Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
You shall make two rings of gold, and you shall put them on the two ends of the breastplate, on its edge, which is toward the side of the ephod inward.
27 Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
You shall make two rings of gold, and shall put them on the two shoulder straps of the ephod underneath, in its forepart, close by its coupling, above the skillfully woven band of the ephod.
28 Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.
They shall bind the breastplate by its rings to the rings of the ephod with a lace of blue, that it may be on the skillfully woven band of the ephod, and that the breastplate may not swing out from the ephod.
29 “Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse.
Aaron shall bear the names of the sons of Israel on the breastplate for judging over his heart, when he goes in to the holy place, as a continual reminder before God.
30 Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.
You are to put in the breastplate for judging the Urim and the Thummim; and they are to be over Aaron's heart, when he goes in before the LORD. And Aaron will carry the means to make decisions for the children of Israel over his heart before the LORD continually.
31 “Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo.
"You shall make the robe of the ephod all of blue.
32 Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
It shall have a hole for the head in its midst: it shall have a binding of woven work around its hole, as it were the hole of a coat of mail, that it not be torn.
33 Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake.
On its hem you shall make pomegranates of blue, and of purple, and of scarlet, around its hem; and bells of gold between and around them:
34 Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse.
a golden bell and a pomegranate, a golden bell and a pomegranate, around the hem of the robe.
35 Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.
It shall be on Aaron to minister: and its sound shall be heard when he goes in to the holy place before the LORD, and when he comes out, that he not die.
36 “Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, Cohoperekedwa kwa Yehova.
"You shall make a plate of pure gold, and engrave on it, like the engravings of a signet, 'HOLY TO THE LORD.'
37 Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo.
You shall put it on a lace of blue, and it shall be on the sash; on the front of the sash it shall be.
38 Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.
It shall be on Aaron's forehead, and Aaron shall bear the iniquity of the holy things, which the children of Israel shall make holy in all their holy gifts; and it shall be always on his forehead, that they may be accepted before the LORD.
39 “Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso.
You shall weave the coat in checker work of fine linen, and you shall make a turban of fine linen, and you shall make a sash, the work of the embroiderer.
40 Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka.
"You shall make coats for Aaron's sons, and you shall make sashes for them and you shall make headbands for them, for glory and for beauty.
41 Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.
You shall put them on Aaron your brother, and on his sons with him, and shall anoint them, and consecrate them, and sanctify them, that they may minister to me in the priest's office.
42 “Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche.
You shall make them linen breeches to cover the flesh of their nakedness; from the waist even to the thighs they shall reach:
43 Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa. “Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”
They shall be on Aaron, and on his sons, when they go in to the Tent of Meeting, or when they come near to the altar to minister in the holy place; that they do not bear iniquity, and die: it shall be a statute forever to him and to his descendants after him.

< Eksodo 28 >