< Eksodo 27 >
1 “Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
El altar lo harás cuadrado, de madera de acacia de 2,25 metros de largo y de ancho, y de 1,35 metros de alto.
2 Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
Le harás cuernos en sus cuatro esquinas. Los cuernos serán de una misma pieza, recubiertos de bronce.
3 Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
También harás sus vasijas para recibir la ceniza, y sus paletas, tazones, tenedores y braseros. Todos sus utensilios los harás de bronce.
4 Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
Le harás una rejilla de bronce en forma de red. Sobre la rejilla en sus cuatro esquinas, harás cuatro argollas de bronce.
5 Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
La pondrás debajo del borde del altar, y llegará hasta la mitad del altar.
6 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
Harás varas de madera de acacia recubiertas de bronce para el altar.
7 Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
Sus varas se meterán por las argollas, y cuando sea transportado, las varas estarán a ambos lados del altar.
8 Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
Lo harás hueco, de tablas. Lo harán como te fue mostrado en la Montaña.
9 “Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
También harás el patio del Tabernáculo. Por el lado sur, el patio tendrá cortinas de cordoncillo de lino de 45 metros de largo por cada lado.
10 Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Sus 20 columnas y sus 20 basas serán de bronce, pero los capiteles de las columnas y sus molduras, de plata.
11 Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
También en el lado norte habrá a lo largo cortinas de 45 metros de largo. Sus columnas serán 20, con sus 20 basas de bronce, pero los capiteles de las columnas y sus molduras serán de plata.
12 “Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
A lo ancho del patio, por el extremo del occidente, habrá cortinas de 22,5 metros. Sus columnas serán diez, con sus diez basas.
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
El patio de la puerta por el lado del oriente será de 22,5 metros.
14 Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
Las cortinas para un lado serán de 6,75 metros. Sus columnas serán tres, con sus tres basas y
15 Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
al otro lado, cortinas de 6,75 metros, sus tres columnas, con sus tres basas.
16 “Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
En la entrada del patio habrá una cortina de 9 metros de [tela] azul, púrpura y carmesí y cordoncillo de lino, obra de bordador. Sus columnas serán cuatro, con sus cuatro basas.
17 Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
Todas las columnas alrededor del patio tendrán abrazaderas de plata. Sus capiteles serán de plata y sus basas serán de bronce.
18 Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
La longitud del patio será de 45 metros, la anchura de 22,5 metros por ambos lados y la altura de 2,25 metros. Sus cortinas serán de cordoncillo de lino y sus basas de bronce.
19 Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
Todos los utensilios del Tabernáculo para todo su servicio, todas sus estacas y todas las estacas del patio serán de bronce.
20 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
Y tú ordenarás a los hijos de Israel que te traigan aceite puro de olivas machacadas para el alumbrado, a fin de que la lámpara arda continuamente
21 Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”
en el Tabernáculo de Reunión, afuera del velo que está antes del Testimonio. Desde la noche hasta la mañana Aarón y sus hijos la mantendrán delante de Yavé. Será un estatuto perpetuo para los hijos de Israel en todas sus generaciones.