< Eksodo 27 >
1 “Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
Tu feras encore un autel de bois de sétim, qui aura cinq coudées en longueur et autant en largeur, c’est-à-dire carré, et trois coudées en hauteur.
2 Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
Mais les cornes en sortiront aux quatre angles; et tu le couvriras d’airain.
3 Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
Et tu feras à son usage des chaudières pour recevoir les cendres, des pincettes, des fourchettes et des brasiers; tu feras tous ces instruments en airain.
4 Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
Tu feras encore une grille d’airain en forme de rets: à ses quatre angles seront des anneaux d’airain,
5 Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
Que tu mettras au-dessous du foyer de l’autel: et la grille viendra jusqu’au milieu de l’autel.
6 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
Tu feras aussi deux leviers d’autel de bois de sétim, que tu couvriras de lames d’airain:
7 Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
Et tu les passeras dans les anneaux; et ils seront des deux côtés de l’autel pour le porter.
8 Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
Tu ne feras point l’autel solide, mais vide et creux au dedans, comme il t’a été montré sur la montagne.
9 “Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
Tu feras aussi le parvis du tabernacle au côté austral duquel seront contre le midi des rideaux de fin lin retors: un seul côté tiendra cent coudées en longueur.
10 Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Et tu y poseras vingt colonnes avec autant de soubassements d’airain, lesquelles auront leurs chapiteaux avec leurs ornements d’argent.
11 Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
De même aussi du côté de l’aquilon il y aura des rideaux de cent coudées de long, vingt colonnes et des soubassements d’airain de même nombre; leurs chapiteaux avec leurs ornements seront d’argent.
12 “Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
Mais dans la largeur du parvis qui regarde l’occident il y aura dans l’espace de cinquante coudées des rideaux, dix colonnes et autant de soubassements.
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
De même, dans la largeur du parvis, laquelle regarde l’orient, il y aura cinquante coudées,
14 Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
Dans lesquelles seront affectés à un côté des rideaux de quinze coudées, trois colonnes et autant de soubassements:
15 Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
Et de l’autre côté seront des rideaux ayant quinze coudées, trois colonnes et autant de soubassements.
16 “Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
Mais à l’entrée du parvis on fera un rideau de vingt coudées d’hyacinthe, de pourpre, d’écarlate deux fois teinte et d’un fin lin retors, en ouvrage de brodeur: cette entrée aura quatre colonnes et autant de soubassements.
17 Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
Toutes les colonnes du parvis seront revêtues tout autour de lames d’argent; elles auront des chapiteaux d’argent et des soubassements d’airain.
18 Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
En longueur le parvis aura cent coudées, en largeur cinquante; sa hauteur sera de cinq coudées; et il sera fait de fin lin retors, et il aura des soubassements d’airain.
19 Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
Tous les vases du tabernacle destinés à tous les usages et à toutes les cérémonies, tant ses pieux que ceux du parvis, tu les feras d’airain.
20 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
Ordonne aux enfants d’Israël qu’ils t’apportent de l’huile d’oliviers très pure, et pilée au mortier, afin qu’une lampe brûle toujours.
21 Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”
Dans le tabernacle de témoignage en dehors du voile qui est suspendu devant le témoignage. Et Aaron et ses fils la placeront, afin qu’elle éclaire jusqu’au matin devant le Seigneur. Ce sera un culte perpétuel durant leurs successions parmi les enfants d’Israël.