< Eksodo 27 >
1 “Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
Et tu feras l’autel de bois de sittim: [il aura] cinq coudées de long, et cinq coudées de large; l’autel sera carré, et sa hauteur sera de trois coudées.
2 Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
Et tu feras ses cornes à ses quatre coins; ses cornes seront [tirées] de lui; et tu le plaqueras d’airain.
3 Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
Et tu feras ses vases à cendre, et ses pelles, et ses bassins, et ses fourchettes, et ses brasiers; tous ses ustensiles, tu les feras d’airain.
4 Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
Et tu lui feras une grille en ouvrage de treillis, d’airain; et tu feras au treillis quatre anneaux d’airain, à ses quatre bouts;
5 Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
et tu le mettras au-dessous du contour de l’autel, en bas, et le treillis ira jusqu’au milieu de l’autel.
6 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
Et tu feras des barres pour l’autel, des barres de bois de sittim, et tu les plaqueras d’airain.
7 Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
Et on fera entrer ses barres dans les anneaux; et les barres seront aux deux côtés de l’autel, pour le porter.
8 Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
Tu le feras creux, avec des planches, comme il t’a été montré sur la montagne; on le fera ainsi.
9 “Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
Et tu feras le parvis du tabernacle: pour le côté du midi vers le sud, des tentures de fin coton retors pour le parvis, de 100 coudées en longueur pour un côté,
10 Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
et ses 20 piliers, et leurs 20 bases d’airain; les crochets des piliers et leurs baguettes d’attache seront en argent.
11 Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Et de même pour le côté du nord, dans la longueur, [tu feras] des tentures de 100 [coudées] en longueur, et ses 20 piliers, et leurs 20 bases d’airain; les crochets des piliers et leurs baguettes d’attache seront en argent.
12 “Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
Et [pour] la largeur du parvis du côté de l’occident, [tu feras] 50 coudées de tentures, leurs dix piliers et leurs dix bases.
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
Et la largeur du parvis du côté de l’orient, vers le levant, sera de 50 coudées:
14 Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
[tu feras], pour l’un des côtés, 15 coudées de tentures, leurs trois piliers et leurs trois bases,
15 Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
et pour l’autre côté, 15 [coudées] de tentures, leurs trois piliers et leurs trois bases,
16 “Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
et pour la porte du parvis, un rideau de 20 coudées, de bleu, et de pourpre, et d’écarlate, et de fin coton retors, en ouvrage de brodeur, ses quatre piliers et leurs quatre bases.
17 Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
Tous les piliers du parvis, à l’entour, auront des baguettes d’attache en argent, leurs crochets, d’argent, et leurs bases, d’airain.
18 Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
La longueur du parvis sera de 100 coudées, et la largeur de 50 tout le long, et la hauteur de cinq coudées, en fin coton retors; et les bases des piliers seront d’airain.
19 Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
Tous les ustensiles du tabernacle, pour tout son service, et tous ses pieux, et tous les pieux du parvis, seront d’airain.
20 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
Et toi, tu commanderas aux fils d’Israël, et ils t’apporteront de l’huile d’olive pure, broyée, pour le luminaire, pour faire luire les lampes continuellement.
21 Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”
Aaron et ses fils les arrangeront devant l’Éternel, depuis le soir jusqu’au matin, dans la tente d’assignation, en dehors du voile qui est devant le témoignage. Ce sera de la part des fils d’Israël un statut perpétuel, en leurs générations.