< Eksodo 27 >

1 “Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
“You shall make the altar of acacia wood, five cubits [7.5 ft; 22.9 m] long, and five cubits [7.5 ft; 22.9 m] wide; the altar shall be square: and its height shall be three cubits [4.5 ft; 13.7 m].
2 Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
You shall make its horns on its four corners; its horns shall be of one piece with it; and you shall overlay it with bronze.
3 Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
You shall make its pots to take away its ashes, its shovels, its basins, its meat hooks, and its fire pans: all its utensils you shall make of bronze.
4 Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
You shall make a grating for it of network of bronze: and on the net you shall make four bronze rings in its four corners.
5 Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
You shall put it under the ledge around the altar beneath, that the net may reach halfway up the altar.
6 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
You shall make poles for the altar, poles of acacia wood, and overlay them with bronze.
7 Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
Its poles shall be put into the rings, and the poles shall be on the two sides of the altar, when carrying it.
8 Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
You shall make it with hollow planks. They shall make it as it has been shown you on the mountain.
9 “Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
“You shall make the court of the tabernacle: for the south side southward there shall be hangings for the court of fine twined linen one hundred cubits [150 ft; 457.2 m] long for one side:
10 Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
and its pillars shall be twenty, and their sockets twenty, of bronze; the hooks of the pillars and their fillets shall be of silver.
11 Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Likewise for the north side in length there shall be hangings one hundred cubits [150 ft; 457.2 m] long, and its pillars twenty, and their sockets twenty, of bronze; the hooks of the pillars, and their fillets, of silver.
12 “Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
For the width of the court on the west side shall be hangings of fifty cubits [75 ft; 228.6 m]; their pillars ten cubits [15 ft; 45.72 m], and their sockets ten cubits [15 ft; 45.72 m].
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
The width of the court on the east side eastward shall be fifty cubits [75 ft; 228.6 m].
14 Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
The hangings for the one side of the gate shall be fifteen cubits [22.5 ft; 68.58 m]; their pillars three cubits [4.5 ft; 13.7 m], and their sockets three cubits [4.5 ft; 13.7 m].
15 Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
For the other side shall be hangings of fifteen cubits [22.5 ft; 68.58 m]; their pillars three, and their sockets three cubits [4.5 ft; 13.7 m].
16 “Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
For the gate of the court shall be a screen of twenty cubits [30 ft; 91.44 m], of blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen, the work of the embroiderer; their pillars four cubits [6 ft; 18.29 m], and their sockets four cubits [6 ft; 18.29 m].
17 Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
All the pillars of the court around shall have chasak ·joints for binding· made with silver; their hooks of silver, and their sockets of bronze.
18 Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
The length of the court shall be one hundred cubits [150 ft; 457.2 m], and the width fifty cubits [75 ft; 228.6 m] every where, and the height five cubits [7.5 ft; 22.9 m], of fine twined linen, and their sockets of bronze.
19 Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
All the instruments of the tabernacle in all its service, and all its pins, and all the pins of the court, shall be of bronze.
20 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
“You shall enjoin the children of Israel [God prevails], that they bring to you pure olive oil beaten for the light, to cause a menorah ·lamp· to burn continually.
21 Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”
In the Tent of Meeting, outside the veil which is before the testimony, Aaron [Light-bringer] and his sons shall keep it in order from evening to morning before Adonai: it shall be a regulation forever throughout their generations on the behalf of the children of Israel [God prevails].

< Eksodo 27 >