< Eksodo 27 >
1 “Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
And thou shalt make the altar of shittim wood: five cubits long, and five cubits broad, a foursquare shall the altar be, and three cubits shall be its height.
2 Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
And thou shalt make its horns on its four corners, from itself shall its horns be; and thou shalt overlay it with copper.
3 Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
And thou shalt make its pots to receive its ashes, and its shovels, and its basins, and its forks, and its fire-pans; all its vessels thou shalt make of copper.
4 Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
And thou shalt make for it a grating, of a network of copper; and thou shalt make upon the net four rings of copper, on its four corners.
5 Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
And thou shalt put it under the compass of the altar beneath, and the net shall reach even to the half of the altar.
6 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
And thou shalt make staves for the altar, staves of shittim wood, and overlay them with copper.
7 Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
And the staves shall be put into the rings, and the staves shall be upon the two sides of the altar, when they bear it.
8 Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
Hollow, of boards, shalt thou make it; as it was shown to thee on the mount, so shall they make it.
9 “Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
And thou shalt make the court of the tabernacle: for the south side, on the right, the hangings for the court, of twisted linen, shall be a hundred cubits in length, for the one side.
10 Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
And its pillars shall be twenty, with their twenty sockets of copper; the hooks of the pillars and their fillets shall be of silver.
11 Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
And likewise for the north side in the length there shall be hangings one hundred cubits in length, and its pillars twenty with their twenty sockets of copper; the hooks of the pillars and their fillets shall be of silver.
12 “Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
And [for] the breadth of the court on the west side shall be fifty cubits of hangings; their pillars shall be ten, and their sockets ten.
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
And the breadth of the court on the front side, eastward, shall be fifty cubits.
14 Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
And fifteen cubits of hangings shall be on the one wing; their pillars shall be three and their sockets three.
15 Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
And on the other wing shall be fifteen cubits of hangings; their pillars shall be three, and their sockets three.
16 “Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
And for the gate of the court shall be a hanging of twenty cubits, of blue, and purple, and scarlet yarn, and twisted linen, the work of the embroiderer; with four pillars for the same, and their four sockets.
17 Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
All the pillars round about the court shall be filleted with silver; their hooks shall be of silver and their sockets of copper.
18 Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
The length of the court shall be one hundred cubits, and the breadth fifty by fifty, and the height five cubits, of twisted linen, and the sockets for the same of copper.
19 Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
All the vessels of the tabernacle in all the service thereof, and all its pins, and all the pins of the court, shall be of copper.
20 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
And thou shalt command the children of Israel, that they bring thee pure olive oil, beaten out, for the lighting, to cause a light to burn always.
21 Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”
In the tabernacle of the congregation, without the vail, which is before the testimony, shall Aaron with his sons arrange it [for] from the evening to the morning, before the Lord; as a statute for ever unto their generations, on behalf of the children of Israel.