< Eksodo 26 >

1 “Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
"Puis tu feras le tabernacle, savoir dix tapis, qui seront faits de lin retors, de fils d’azur, de pourpre et d’écarlate et artistement damassés de chérubins.
2 Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
La longueur de chaque tapis sera de vingt-huit coudées; la largeur, de quatre coudées par tapis: dimension uniforme pour tous les tapis.
3 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
Cinq des tapis seront attachés l’un à l’autre et les cinq autres seront joints de la même manière.
4 Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
Tu adapteras des noeuds d’étoffe azurée au bord du tapis qui termine un assemblage et de même au bord du dernier tapis de l’autre assemblage.
5 Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
Tu mettras cinquante noeuds à un tapis et cinquante autres au bord du tapis terminant le second assemblage; ces nœuds se correspondront l’un à l’autre.
6 Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
Tu feras cinquante agrafes d’or; tu joindras les tapis l’un à l’autre au moyen de ces agrafes, de sorte que l’enceinte sera continue.
7 “Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
Puis tu feras des tapis en poil de chèvre, servant de pavillon au tabernacle; tu les feras au nombre de onze.
8 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
La longueur de chaque tapis sera de trente coudées; la largeur, de quatre coudées par tapis: même dimension pour les onze tapis.
9 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
Tu joindras cinq de ces tapis à part et à part les six autres, le sixième tapis devant être rabattu sur le devant de la tente.
10 Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
Tu disposeras cinquante nœuds au bord du tapis extrême d’un assemblage et cinquante noeuds au bord, du tapis terminant le second assemblage.
11 Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
Tu confectionneras cinquante agrafes de cuivre; tu les feras entrer dans les noeuds et réuniras ainsi le pavillon en un seul corps.
12 Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
Les tapis du pavillon dépassant les autres d’une certaine longueur, le demi-tapis qui sera en plus descendra sur la face postérieure du tabernacle.
13 Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
Et la coudée d’un côté et la coudée de l’autre, qui se trouveront en excès dans la longueur des tapis du pavillon, retomberont sur les côtés du tabernacle, de part et d’autre, pour le couvrir.
14 Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
Tu ajouteras, pour couvrir le pavillon, des peaux de bélier teintes en rouge et, par-dessus, une couverture de peaux de tahach.
15 “Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
"Tu feras ensuite les solives destinées au tabernacle: ce seront des ais de chittîm perpendiculaires.
16 Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
Dix coudées seront la longueur de chaque solive; une coudée et demie la largeur de chacune.
17 Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
Chaque solive aura deux tenons parallèles l’un à l’autre; ainsi feras-tu pour toutes les solives du tabernacle.
18 Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
Tu disposeras ces solives pour le tabernacle, comme il suit: vingt solives dans le sens du sud ou midi;
19 Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
sous ces vingt solives tu placeras quarante socles d’argent: deux socles sous une solive, pour recevoir ses deux tenons et deux socles sous une autre, pour ses deux tenons.
20 Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
De même, pour le second côté du tabernacle, à la face nord, vingt solives,
21 Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
avec leurs quarante socles d’argent: deux socles sous une solive et deux socles sous la solive suivante.
22 Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
Pour le côté postérieur du tabernacle, à l’occident, tu prépareras six solives;
23 Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
puis, tu en prépareras deux pour les angles postérieurs du tabernacle.
24 Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
Elles seront accouplées par en bas et également accouplées, au sommet, par un seul anneau; même disposition pour ces deux solives, placées aux deux angles.
25 Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
Il y aura donc huit solives, avec leurs socles d’argent, soit seize socles: deux socles sous une solive et deux socles sous l’autre.
26 “Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
Tu feras ensuite des traverses de bois de chittîm: cinq pour les solives d’un côté du tabernacle,
27 mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
cinq autres pour les solives du second côté du tabernacle et cinq traverses pour les solives du côté postérieur, occidental.
28 Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
La traverse du milieu passera dans l’intérieur des solives, les reliant d’une extrémité à l’autre.
29 Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
Ces solives, tu les recouvriras d’or; tu feras en or leurs anneaux, où passeront les traverses et ces traverses tu les recouvriras d’or.
30 “Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
Tu érigeras ainsi le tabernacle, suivant la disposition qui t’a été enseignée sur cette montagne.
31 “Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
"Tu feras ensuite un voile en étoffe d’azur, de pourpre, d’écarlate et de lin retors; on le fabriquera artistement, en le damassant de chérubins.
32 Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
Tu le suspendras à quatre piliers de chittîm, recouverts d’or, à crochets d’or et soutenus par quatre socles d’argent.
33 Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
Tu fixeras ce voile au-dessous des agrafes; c’est là, dans l’enceinte protégée par le voile, que tu feras entrer l’arche du Statut et le voile séparera ainsi pour vous le sanctuaire d’avec le Saint des saints.
34 Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
Tu poseras le propitiatoire sur l’arche du Statut, dans le Saint des saints.
35 Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
Tu placeras la table en dehors du voile et le candélabre en face de la table au côté méridional du tabernacle, la table étant placée au côté septentrional.
36 “Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
Puis, tu confectionneras un rideau pour l’entrée de la Tente, en azur, pourpre, écarlate et lin retors, artistement brodés.
37 Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”
Tu feras, pour ce rideau, cinq piliers de chittîm; tu les revêtiras d’or, leurs crochets seront d’or et tu mouleras pour eux cinq socles de cuivre.

< Eksodo 26 >