< Eksodo 26 >
1 “Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
“[Tell the people to] make the Sacred Tent using ten long strips of fine linen. They must take blue, purple, and red thread (OR, weave the strips from blue, purple, and red thread), and [a skilled craftsman] must embroider these strips with [designs that represent] the winged creatures [that are above the chest].
2 Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
Each strip is to be (14 yards/twelve meters) long and (2 yards/1.8 meters) wide.
3 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
[Tell them to] sew five strips together to make one set, and sew the other five strips together to make another set.
4 Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
For each set, [they must] make loops of blue [cloth] and fasten them along the outer edge of the strip, at the end of each set.
5 Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
[They must] put 50 loops on the edge of the first set, and 50 loops on the edge of the second set.
6 Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
[Tell them to] make 50 gold clasps/fasteners, to fasten both of the sets together. As a result, the inside of the Sacred Tent will be [as though it was] one piece.
7 “Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
Also, [tell them to] make a cover for the Sacred Tent from eleven pieces of cloth made from goats’ hair.
8 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
Each piece of cloth is to be (15 yards/13.5 meters) long and (2 yards/1.8 meters) wide.
9 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
[Tell them to] sew five of these pieces of cloth together to make one set, and sew the other six pieces of cloth together to make another set. [They] must fold the sixth piece [of cloth] in half to make it double over the front of the Sacred Tent.
10 Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
[Tell them to] make 100 loops [of blue cloth], and to fasten 50 of them to the outer edge of the one set and fasten 50 to the outer edge of the other set.
11 Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
[Tell them to] make fifty bronze clasps/fasteners and put them in the cloth loops to join the two sets together. As a result, the cover for the Sacred Tent will be [as though it was] one piece.
12 Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
[Let] the extra part of the cover, the part that extends beyond [the linen cloth], hang over the back of the Sacred Tent.
13 Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
The extra half yard/meter of each cover, the part that extends beyond [the linen cloth] on each side, must hang over the two sides of the Sacred Tent, to protect the sides.
14 Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
[Tell them to] make two more covers for the Sacred Tent. One is to be made from rams’ skins that have been (tanned/dyed red), and the top cover is to be made from goatskin leather.”
15 “Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
“[Tell them to] make frames from acacia wood, frames that will be set up [from which to hang the Sacred Tent covers].
16 Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
Each frame is to be (five yards/four meters) long and (27 in./66 cm.) wide.
17 Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
[They] must make two projections at the bottom of each frame. These will be to fasten the frames to the bases underneath them. They must make these projections at the bottom of each frame.
18 Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
Make 20 frames for the south side of the Sacred Tent.
19 Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
[Tell them to] make 40 silver bases to go underneath them. Two bases will go under each frame. The projections [at the bottom] of each frame are [to be made] to fit into the bases.
20 Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
[Similarly], [tell them to] make twenty frames for the north side of the Sacred Tent.
21 Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
[They] must make 40 silver bases for them also, with two bases to be put under each frame.
22 Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
For the rear of the Sacred Tent, on the west side, [tell them to] make six frames.
23 Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
Also, [tell them to] make two extra frames, one for each corner of the rear of the Sacred Tent, [to provide extra support].
24 Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
The two corner frames must be joined from the bottom to the top (OR, joined at both the bottom and the top). At the top of each of the two corner frames there must be a gold ring for holding the crossbar.
25 Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
In that way, [for the rear of the Sacred Tent] there will be eight frames, and there will be 16 bases, two under each frame.
26 “Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
[Tell them to] make 15 crossbars from acacia wood.
27 mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
Five of them will be for the frames on the north side of the Sacred Tent, five will be for the south side, and five for the frames at the rear of the Sacred Tent, the west side.
28 Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
Tell them to fasten the crossbars on the north, south, and west sides of the Sacred Tent to the middle of the frames. The two long ones must extend from one end of the Sacred Tent to the other, and the crossbar on the west side must extend from one side of the Sacred Tent to the other.
29 Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
[Tell them to] cover the frames with gold, and make gold rings to fasten the crossbars to the frames. The crossbars must [also] be covered with gold.
30 “Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
Erect the Sacred Tent in the way that I have shown you [here] on [this] mountain.”
31 “Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
“[Tell them to] make a curtain from fine linen. A skilled craftsman must embroider it with blue, purple, and red yarn/thread, making [designs to represent] the winged creatures [that are above the chest].
32 Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
[Tell them to] suspend/hang the curtain from four posts made from acacia wood and covered with gold. Set [each] post in a silver base.
33 Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
[They] must suspend/hang the [top of the] curtain by hooks that are fastened to the roof of the Sacred Tent. Behind the curtain, in the [room called the] Very Holy Place, [they] must put the chest containing the [two stone slabs on which I have written my] commandments. That curtain will separate the Holy Place from the Very Holy Place.
34 Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
On top of the chest in the Very Holy Place [they] must put the lid which will be the place where [blood will be sprinkled to] forgive people’s sins.
35 Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
[In the room that is] outside of the Very Holy Place, [they] must put the table [for the sacred] bread on the north side, and put the lampstand on the south side.
36 “Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
[Tell them to] make a curtain to [cover] the entrance of the Sacred Tent. They must make it from fine linen, and a skilled weaver must embroider it with blue, purple, and red yarn/thread.
37 Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”
To hold up this curtain, [they] must make five posts from acacia wood. [They] must cover them with gold, and fasten gold clasps/fasteners to them. Also [they] must make a bronze base for each of these posts.”