< Eksodo 26 >

1 “Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
And the tabernacle you will make ten curtains fine linen twisted and violet stuff and purple and scarlet stuff of scarlet cherubim [the] work of a skillful worker you will make them.
2 Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
[the] length of - The curtain one [will be] eight and twenty by the cubit and [the] breadth [will be] four by the cubit the curtain one size one [will belong] to all the curtains.
3 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
Five of the curtains they will be joined each to sister its and five curtains [will be] joined each to sister its.
4 Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
And you will make loops of violet stuff on [the] edge of the curtain one from an end in the joined set and thus you will do on [the] edge of the curtain outermost in the joined set second.
5 Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
Fifty loops you will make on the curtain one and fifty loops you will make at [the] end of the curtain which [is] in the joined set second [will be] opposite the loops each to sister its.
6 Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
And you will make fifty hooks of gold and you will join the curtains each to sister its with the hooks and it will be the tabernacle one.
7 “Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
And you will make curtains of goat hair into a tent over the tabernacle one [plus] ten curtains you will make them.
8 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
[the] length of - The curtain one [will be] thirty by the cubit and [the] breadth [will be] four by the cubit the curtain one size one [will belong] to one [plus] ten curtains.
9 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
And you will join five of the curtains alone and six of the curtains alone and you will fold double the curtain sixth to [the] front of [the] face of the tent.
10 Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
And you will make fifty loops on [the] edge of the curtain one outermost in the joined set and fifty loops on [the] edge of the curtain the joined set second.
11 Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
And you will make hooks of bronze fifty and you will put the hooks in the loops and you will join the tent and it will be one.
12 Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
And [the] overhanging of the surplus in [the] curtains of the tent [the] half of the curtain which is surplus it will overhang over [the] rear of the tabernacle.
13 Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
And the cubit from this and the cubit from this in the surplus in [the] length of [the] curtains of the tent it will be projecting over [the] sides of the tabernacle from this and from this to cover it.
14 Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
And you will make a covering for the tent skins of rams dyed red and a covering of skins of dolphins from to above.
15 “Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
And you will make the frames for the tabernacle wood of acacia standing upright.
16 Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
[will be] ten Cubits [the] length of the frame and [will be] a cubit and [the] half of the cubit [the] breadth of the frame one.
17 Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
Two hands [belonged] to the frame one joined each to sister its thus you will do for all [the] frames of the tabernacle.
18 Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
And you will make the frames for the tabernacle twenty frame[s] for [the] side of south-ward south-ward.
19 Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
And forty bases of silver you will make under twenty the frame[s] two bases under the frame one for [the] two hands its and two bases under the frame one for [the] two hands its.
20 Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
And for [the] side of the tabernacle second for [the] side of [the] north twenty frame[s].
21 Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
And forty bases their silver two bases under the frame one and two bases under the frame one.
22 Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
And for [the] innermost parts of the tabernacle west-ward you will make six frames.
23 Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
And two frames you will make for [the] corners of the tabernacle in the innermost parts.
24 Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
So they may be twins from to downwards and together they will be complete on top its into the ring one thus it will be for both of them [the] two the corners they will become.
25 Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
And they will be eight frames and bases their silver six-teen bases two bases under the frame one and two bases under the frame one.
26 “Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
And you will make bars wood of acacia five [bars] for [the] frames of [the] side of the tabernacle one.
27 mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
And five bars for [the] frames of [the] side of the tabernacle second and five bars for [the] frames of [the] side of the tabernacle for the innermost parts west-ward.
28 Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
And the bar middle in [the] middle of the frames [will be] passing through from the end to the end.
29 Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
And the frames you will overlay gold and rings their you will make gold holders for the bars and you will overlay the bars gold.
30 “Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
And you will set up the tabernacle according to plan its which you have been shown on the mountain.
31 “Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
And you will make a curtain violet stuff and purple and scarlet stuff of scarlet and fine linen twisted [the] work of a skillful worker someone will make it cherubim.
32 Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
And you will put it on four pillars of acacia overlaid gold hooks their [will be] gold on four bases of silver.
33 Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
And you will put the curtain under the hooks and you will bring there from inside to the curtain [the] ark of the testimony and it will separate the curtain for you between the holy place and between [the] holy place of the holy places.
34 Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
And you will put the atonement cover on [the] ark of the testimony in [the] holy place of the holy places.
35 Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
And you will put the table from [the] outside of the curtain and the lampstand opposite to the table on [the] side of the tabernacle south-ward and the table you will put on [the] side of [the] north.
36 “Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
And you will make a screen for [the] entrance of the tent violet stuff and purple and scarlet stuff of scarlet and fine linen twisted [the] work of a worker in colors.
37 Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”
And you will make for the screen five pillars of acacia and you will overlay them gold hooks their [will be] gold and you will cast for them five bases of bronze.

< Eksodo 26 >