< Eksodo 26 >

1 “Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
Also the habitation shalt thou make, with ten curtains, of twined linen, and blue, and purple, and crimson, with cherubim, the work of a skilful weaver, shalt thou make them.
2 Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
The length of each curtain twenty-eight cubits, and, the breadth four cubits, of each curtain, one measure, for all the curtains.
3 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
The five curtains, shall be joined, one to another, and, the other five curtains, joined, one to another.
4 Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
And thou shalt make loops of blue on the border of each curtain, at the edge of the set, —and, thus, shalt thou do in the border of the curtain, that is outmost in the second set:
5 Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
fifty loops, shalt thou make, in the one curtain, and fifty loops, shalt thou make in the edge of the curtain which is in the second set, the loops being opposite, one to another.
6 Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
And thou shalt make fifty clasps of gold, —so shalt thou join the curtains one to another, with the clasps, and thus shall the habitation be one.
7 “Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
And thou shalt make curtains of goat’s hair, for a tent, over the habitation—eleven curtains, shalt thou make them.
8 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
The length of each curtain, thirty cubits, and the breadth, four cubits, of each curtain, —one measure, to the eleven curtains.
9 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
And thou shalt join the five curtains by themselves, and the six curtains by themselves, and thou shalt fold back the sixth curtain, in the forefront of the tent.
10 Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
And thou shalt make fifty loops on the border of the one curtain, that is outmost in the set, and fifty loops on the border of the curtain, of the second set.
11 Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
And thou shalt make fifty clasps of bronze, and bring the clasps into the loops, so shalt thou join the tent, and it shall be one.
12 Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
And the overplus that remaineth in the curtains of the tent, —the half curtain that remaineth, shall hang over at the back of the habitation.
13 Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
And, the cubit on the one side, and the cubit on the other side of that which remaineth, in the length of the curtains of the tent shall be hung over the sides of the habitation on this side and on that side to make a covering.
14 Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
And thou shalt make a covering, for the tent, of rams’ skins dyed red, —and a covering of badger’s skins, above.
15 “Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
And thou shalt make boards for the habitation, —of acacia wood to stand up:
16 Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
ten cubits, the length of the board, and a cubit and a half cubit the breadth of each board:
17 Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
two tenons, to each board, united one to another, —thus, shalt thou make, for all the boards of the habitation,
18 Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
So then thou shalt make the boards for the habitation, twenty boards, on the south side southwards.
19 Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
And forty sockets of silver, shalt thou make under the twenty boards, —two sockets under the one board for its two tenons, and two sockets, under the next board, for its two tenons.
20 Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
And on the second side of the habitation, towards the north, twenty boards;
21 Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
and their forty sockets of silver, —two sockets, under the one board, and, two sockets, under the next board.
22 Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
And for the hinderpart of the habitation, westward, shalt thou make six boards.
23 Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
And, two boards, shalt thou make, for the corners of the habitation, —in the hinderpart:
24 Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
that they may be double beneath, and at the same time, they shall be entire on the top thereof, into each ring, —thus, shall it be for them both, for the two corners, shall they be.
25 Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
So shall they be eight boards, and, their sockets of silver, sixteen sockets, —two sockets, under the one board, and, two sockets, under the next board.
26 “Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
And thou shalt make bars, of acacia wood, —five, for the boards of the one side of the habitation,
27 mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
and five bars, for the boards of the other side of the habitation, and five bars, for the boards of the side of the habitation, at the hinderpart westward;
28 Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
with the middle bar in the midst of the boards, —running along from end to end.
29 Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
And the boards, shalt thou overlay with gold, and their rings, shalt thou make of gold, as receptacles for the bars, —and thou shalt overlay the bars with gold.
30 “Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
So shalt thou rear up the habitation, according to the fashion thereof, which thou wast caused to see in the mount.
31 “Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
And thou shalt make a veil, of blue and purple, and crimson and fine-twined linen, —of the work of a skilful weaver, shall it be made, with cherubim;
32 Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
and thou shalt hang it upon four pillars of acacia overlaid with gold, with their hooks of gold, —upon four sockets of silver,
33 Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
And thou shalt hang up the veil under the clasps, —and shalt bring in thither, within the veil the ark of the testimony; and the veil shall make a division for you between the holy [place] and the most holy.
34 Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
And thou shalt place the propitiatory, upon the ark of the testimony, —in the most holy [place].
35 Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
And thou shalt set the table outside the veil, and the lampstand over against the table, on the side of the habitation, southward, —and the table, shalt thou place on the north side.
36 “Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
And thou shalt make a screen for the opening of the tent, of blue, and purple and crimson, and fine-twined linen, —the work of an embroiderer.
37 Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”
And thou shalt make for the screen five pillars of acacia, and shalt overlay them with gold, and their hooks [shall be] of gold, —and thou shalt cast for them five sockets of bronze.

< Eksodo 26 >