< Eksodo 26 >
1 “Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
“And you make the Dwelling Place [with] ten curtains of twined linen, and blue, and purple, and scarlet; [with] cherubim, the work of a designer, you make them;
2 Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
the length of the one curtain [is] twenty-eight by the cubit, and the breadth of the one curtain [is] four by the cubit, one measure [is] for all the curtains;
3 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
five of the curtains are joining to one another, and five curtains are joining to one another.
4 Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
And you have made loops of blue on the edge of the first curtain, at the end in the joining; and so you make in the edge of the outermost curtain, in the joining of the second.
5 Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
You make fifty loops in the first curtain, and you make fifty loops in the edge of the curtain which [is] in the joining of the second, causing the loops to take hold to one another;
6 Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
and you have made fifty hooks of gold, and have joined the curtains to one another by the hooks, and the Dwelling Place has been one.
7 “Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
And you have made curtains of goats’ [hair] for a tent over the Dwelling Place; you make eleven curtains:
8 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
the length of one curtain [is] thirty by the cubit, and the breadth of one curtain [is] four by the cubit; one measure [is] for the eleven curtains;
9 Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
and you have joined the five curtains apart, and the six curtains apart, and have doubled the six curtains at the front of the tent.
10 Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
And you have made fifty loops on the edge of the first curtain, the outermost in the joining, and fifty loops on the edge of the curtain which is joining the second;
11 Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
and you have made fifty hooks of bronze, and have brought in the hooks into the loops, and have joined the tent, and it has been one.
12 Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
And the excess remaining in the curtains of the tent—the half of the curtain which is remaining—has spread over the back part of the Dwelling Place;
13 Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
and the cubit on this [side], and the cubit on that [side], in the remaining [part] of the length of the curtains of the tent, is spread out over the sides of the Dwelling Place, on this [side] and on that [side], to cover it;
14 Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
and you have made a covering for the tent of rams’ skins made red, and a covering of tachashim skins above.
15 “Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
And you have made the boards for the Dwelling Place of shittim wood, standing up;
16 Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
ten cubits [is] the length of the board, and a cubit and a half the breadth of one board;
17 Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
two handles [are] to one board, joined to one another; so you make for all the boards of the Dwelling Place;
18 Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
and you have made the boards of the Dwelling Place—twenty boards for the south side southward;
19 Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
and you make forty sockets of silver under the twenty boards, two sockets under one board for its two handles, and two sockets under the other board for its two handles.
20 Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
And for the second side of the Dwelling Place, for the north side, [are] twenty boards,
21 Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
and their forty sockets of silver, two sockets under one board, and two sockets under another board.
22 Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
And for the sides of the Dwelling Place westward, you make six boards.
23 Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
And you make two boards for the corners of the Dwelling Place in the two sides.
24 Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
And they are pairs beneath, and together they are pairs above its head to one ring; so is it for them both, they are for the two corners.
25 Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
And they have been eight boards, and their sockets of silver [are] sixteen sockets, two sockets under one board, and two sockets under another board.
26 “Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
And you have made bars of shittim wood: five for the boards of the first side of the Dwelling Place,
27 mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
and five bars for the boards of the second side of the Dwelling Place, and five bars for the boards of the side of the Dwelling Place at the two sides, westward;
28 Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
and one has caused the middle bar in the midst of the boards to reach from end to end;
29 Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
and you overlay the boards [with] gold, and you make their rings of gold [for] places for bars, and have overlaid their bars with gold;
30 “Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
and you have raised up the Dwelling Place according to its fashion which you have been shown on the mountain.
31 “Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
And you have made a veil of blue, and purple, and scarlet, and twined linen, the work of a designer; he makes it [with] cherubim;
32 Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
and you have put it on four pillars of shittim wood, overlaid [with] gold, their pegs [are] of gold, on four sockets of silver.
33 Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
And you have put the veil under the hooks, and have brought in the Ark of the Testimony there within the veil; and the veil has made a separation for you between the holy and the Holy of Holies.
34 Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
And you have put the propitiatory covering on the Ark of the Testimony in the Holy of Holies.
35 Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
And you have set the table at the outside of the veil, and the lampstand opposite the table on the side of the Dwelling Place southward, and you put the table on the north side.
36 “Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
And you have made a covering for the opening of the tent of blue, and purple, and scarlet, and twined linen, the work of an embroiderer;
37 Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”
and you have made five pillars of shittim [wood] for the covering, and have overlaid them [with] gold, their pegs [are] of gold, and you have cast five sockets of bronze for them.”