< Eksodo 25 >

1 Yehova ananena kwa Mose kuti,
و خداوند موسی را خطاب کرده، گفت:۱
2 “Uza Aisraeli kuti abweretse chopereka kwa Ine. Iwe ulandire choperekacho mʼmalo mwanga kuchokera kwa munthu amene akupereka mwakufuna kwake.
«به بنی‌اسرائیل بگو که برای من هدایا بیاورند؛ از هر‌که به میل دل بیاورد، هدایای مرا بگیرید.۲
3 Zopereka zimene ulandire kwa anthuwo ndi izi: Golide, siliva ndi mkuwa.
و این است هدایا که از ایشان می‌گیرید: طلا و نقره و برنج،۳
4 Nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa, ubweya wambuzi;
و لاجورد وارغوان و قرمز و کتان نازک و پشم بز،۴
5 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha;
و پوست قوچ سرخ شده و پوست خز و چوب شطیم،۵
6 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
وروغن برای چراغها، و ادویه برای روغن مسح، وبرای بخور معطر،۶
7 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
و سنگهای عقیق و سنگهای مرصعی برای ایفود و سینه بند.۷
8 “Iwo andipangire malo wopatulika, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo.
و مقامی ومقدسی برای من بسازند تا در میان ایشان ساکن شوم.۸
9 Umange chihema ndiponso ziwiya zamʼkatimo monga momwe Ine ndidzakuonetsere.
موافق هر‌آنچه به تو نشان دهم از نمونه مسکن و نمونه جمیع اسبابش، همچنین بسازید.۹
10 “Tsono apange bokosi lamatabwa amtengo wa mkesha, ndipo kutalika kwake kukhale masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
«و تابوتی از چوب شطیم بسازند که طولش دو ذراع و نیم، و عرضش یک ذراع و نیم وبلندیش یک ذراع و نیم باشد.۱۰
11 Bokosilo ulikute ndi golide wabwino kwambiri, mʼkati mwake ndi kunja komwe, ndipo upange mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
و آن را به طلای خالص بپوشان. آن را از درون و بیرون بپوشان، وبر زبرش به هر طرف تاجی زرین بساز.۱۱
12 Upange mphete zinayi zagolide ndipo uzimangirire ku miyendo yake inayi ya bokosilo, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
وبرایش چهار حلقه زرین بریز، و آنها را بر چهارقایمه‌اش بگذار، دو حلقه بر یک طرفش و دوحلقه بر طرف دیگر.۱۲
13 Kenaka upange mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
و دو عصا از چوب شطیم بساز، و آنها را به طلا بپوشان.۱۳
14 Ndipo ulowetse nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
و آن عصاها رادر حلقه هایی که بر طرفین تابوت باشد بگذران، تاتابوت را به آنها بردارند.۱۴
15 Nsichizo zizikhala mʼmphete za bokosilo nthawi zonse, zisamachotsedwe.
و عصاها درحلقه های تابوت بماند و از آنها برداشته نشود.۱۵
16 Ndipo udzayike mʼbokosilo miyala iwiri yolembedwapo malamulo imene Ine ndidzakupatse.
و آن شهادتی را که به تو می‌دهم، در تابوت بگذار.۱۶
17 “Upange chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
و تخت رحمت را از طلای خالص بساز. طولش دو ذراع و نیم، و عرضش یک ذراع ونیم.۱۷
18 Ndipo upange Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo, uwayike mbali ziwiri za chivundikirocho,
و دو کروبی از طلا بساز، آنها را ازچرخکاری از هر دو طرف تخت رحمت بساز.۱۸
19 kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa uwapangire limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
و یک کروبی در این سر و کروبی دیگر در آن سر بساز، کروبیان را از تخت رحمت بر هر دوطرفش بساز.۱۹
20 Mapiko a Akerubiwo adzatambasukire pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo adzakhale choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
و کروبیان بالهای خود را بر زبرآن پهن کنند، و تخت رحمت را به بالهای خودبپوشانند. و رویهای ایشان به سوی یکدیگرباشد، و رویهای کروبیان به طرف تخت رحمت باشد.۲۰
21 Uyike chivundikirocho pamwamba pa bokosi ndipo mʼbokosilo uyikemo miyala ya malamulo, imene ndidzakupatse.
و تخت رحمت را بر روی تابوت بگذارو شهادتی را که به تو می‌دهم در تابوت بنه.۲۱
22 Ndizidzakumana nawe pamenepo, pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo, pakati pa Akerubi awiriwo, ndikumadzakupatsa malamulo onse okhudzana ndi Aisraeli.
ودر آنجا با تو ملاقات خواهم کرد و از بالای تخت رحمت از میان دو کروبی که بر تابوت شهادت می‌باشند، با تو سخن خواهم گفت، درباره همه اموری که بجهت بنی‌اسرائیل تو را امر خواهم فرمود.۲۲
23 “Upange tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
«و خوانی از چوب شطیم بساز که طولش دو ذراع، و عرضش یک ذراع، و بلندیش یک ذراع و نیم باشد.۲۳
24 Tebulolo ulikute ndi golide wabwino kwambiri ndipo upange mkombero wagolide mʼmbali mwake.
و آن را به طلای خالص بپوشان، و تاجی از طلا به هر طرفش بساز.۲۴
25 Upange feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo uyike mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
وحاشیه‌ای به قدر چهار انگشت به اطرافش بساز، و برای حاشیه‌اش تاجی زرین از هر طرف بساز.۲۵
26 Upange mphete zinayi zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya zake zinayi, kumene kuli miyendo yake inayi.
و چهار حلقه زرین برایش بساز، و حلقه‌ها را برچهار گوشه چهار قایمه‌اش بگذار.۲۶
27 Mphetezo uziyike kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
و حلقه هادر برابر حاشیه باشد، تا خانه‌ها باشد بجهت عصاها برای برداشتن خوان.۲۷
28 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
و عصاها را ازچوب شطیم بساز، و آنها را به طلا بپوشان تاخوان را بدانها بردارند.۲۸
29 Upange mbale ndi zipande zagolide wabwino, pamodzinso ndi mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe.
و صحنها و کاسه‌ها وجامها و پیاله هایش را که به آنها هدایای ریختنی می‌ریزند بساز، آنها را از طلای خالص بساز.۲۹
30 Pa tebulopo uyikepo buledi woperekedwa kosalekeza, kuti azikhala pamaso panga nthawi zonse.
ونان تقدمه را بر خوان، همیشه به حضور من بگذار.۳۰
31 “Upange choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zikhale zosulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zipangidwire kumodzi.
«و چراغدانی از طلای خالص بساز، و ازچرخکاری چراغدان ساخته شود، قاعده‌اش وپایه‌اش و پیاله هایش و سیبهایش و گلهایش ازهمان باشد.۳۱
32 Mʼmbali mwake mukhale mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
و شش شاخه از طرفینش بیرون آید، یعنی سه شاخه چراغدان از یک طرف و سه شاخه چراغدان از طرف دیگر.۳۲
33 Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zikhale pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri pakhalenso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zikhale chimodzimodzi ndipo zituluke mʼchoyikapo nyalecho.
سه پیاله بادامی با سیبی و گلی در یک شاخه و سه پیاله بادامی با سیبی و گلی در شاخه دیگر و هم چنین در شش شاخه‌ای که از چراغدان بیرون می‌آید.۳۳
34 Pa choyikapo nyalecho pakhale zikho zinayi zopangidwa ngati maluwa amtowo ali ndi mphukira ndi maluwa.
و درچراغدان چهار پیاله بادامی با سیبها و گلهای آنهاباشد.۳۴
35 Mphukira yoyamba ikhale mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri ikhale mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Ndipo mphukira yachitatu ikhale mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zikhale nthambi zisanu ndi imodzi
و سیبی زیر دو شاخه آن و سیبی زیر دوشاخه آن و سیبی زیر دو شاخه آن بر شش شاخه‌ای که از چراغدان بیرون می‌آید.۳۵
36 Mphukira ndi nthambi zonse zisulidwe kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
وسیبها و شاخه هایش از همان باشد، یعنی از یک چرخکاری طلای خالص.۳۶
37 “Ndipo upange nyale zisanu ndi ziwiri ndi kuziyika pa choyikapo nyalecho kuti ziwunikire kutsogolo.
و هفت چراغ برای آن بساز، و چراغهایش را بر بالای آن بگذار تاپیش روی آن را روشنایی دهند.۳۷
38 Mbaniro ndi zowolera phulusa zikhale zagolide wabwino kwambiri.
و گل گیرها وسینیهایش از طلای خالص باشد.۳۸
39 Choyikapo nyale ndi zipangizo zonse zipangidwe ndi golide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
خودش باهمه اسبابش از یک وزنه طلای خالص ساخته شود.۳۹
40 Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.”
و آگاه باش که آنها را موافق نمونه آنها که در کوه به تو نشان داده شد بسازی.۴۰

< Eksodo 25 >