< Eksodo 24 >
1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali.
Also he seide to Moises, `Stie thou to the Lord, thou, and Aaron, and Nadab, and Abyu, and seuenti eldere men of Israel; and ye schulen worschipe afer,
2 Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”
and Moises aloone stie to the Lord, and thei schulen not neiye, nether the puple schal stie with hym.
3 Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.”
Therfore Moises cam, and telde to the puple alle the wordis and domes of the Lord; and al the puple answeride with o vois, We schulen do alle the wordis of the Lord, whiche he spak.
4 Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena. Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
Forsothe Moises wroot alle the wordis of the Lord; and he roos eerli, and bildide an auter to the Lord at the rootis of the hil, and he bildide twelue titlis bi twelue lynagis of Israel.
5 Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano.
And he sente yonge men of the sones of Israel, and thei offriden brent sacrifices, and `thei offriden pesible sacrifices `to the Lord, twelue calues.
6 Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe.
And so Moises took half the part of the blood, and sente in to grete cuppis; forsothe he schedde the residue part on the auter.
7 Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”
And he took the book of the boond of pees, and redde, while the puple herde; whiche seiden, We schulen do alle thingis which the Lord spak, and we schulen be obedient.
8 Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”
Forsothe he took, and sprengide `the blood on the puple, and seide, This is the blood of the boond of pees, which the Lord couenauntide with yow on alle these wordis.
9 Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri,
And Moises, and Aaron, and Nadab, and Abyu, and seuenti of the eldere men of Israel stieden,
10 ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo.
and seiyen God of Israel, vndur hise feet, as the werk of safire stoon, and as heuene whanne it is cleer.
11 Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.
And he sente not his hond on hem of the sones of Israel, that hadden go fer awei; and thei sien God, and eeten and drunkun.
12 Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”
Forsothe the Lord seide to Moises, `Stie thou to me in to the hil, and be thou there, and Y schal yyue to thee tablis of stoon, and the lawe, and comaundementis, whiche Y haue write, that thou teche the children of Israel.
13 Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.
Moises and Josue his mynystre risen, and Moises stiede in to the hil of God,
14 Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”
and seide to the eldere men, Abide ye here, til we turnen ayen to you; ye han Aaron and Hur with you, if ony thing of questioun is maad, ye schulen telle to hem.
15 Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo.
And whanne Moises hadde stied,
16 Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo.
a cloude hilide the hil, and the glorie of the Lord dwellide on Synai, and kyueride it with a cloude sixe daies; forsothe in the seuenthe dai the Lord clepide hym fro the myddis of the cloude; forsothe the licnesse of glorie of the Lord
17 Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo.
was as fier brennynge on the cop of the hil in the siyt of the sones of Israel.
18 Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.
And Moises entride into the myddis of the cloude, and stiede in to the hil, and he was there fourti daies and fourti nyytis.