< Eksodo 24 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali.
Og han sagde til Moses: "Stig op til HERREN, du og Aron, Nadab og Abih og halvfjerdsindstyve af Israels Ældste, og tilbed i Frastand;
2 Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”
Moses alene skal træde hen til HERREN, de andre ikke, og det øvrige Folk må ikke følge med ham derop."
3 Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.”
Derpå kom Moses og kundgjorde hele Folket alle HERRENs Ord og alle Lovbudene, og hele Folket svarede enstemmigt: "Alle de Ord, HERREN har talet, vil vi overholde."
4 Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena. Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
Da skrev Moses alle HERRENs Ord op; og tidligt næste Morgen rejste han ved Foden af Bjerget et Alter og tolv Stenstøtter svarende til Israels tolv Stammer.
5 Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano.
Derefter sendte han de unge Mænd blandt Israeliterne hen for at bringe Brændofre og slagte unge Tyre som Takofre til HERREN.
6 Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe.
Og Moses tog den ene Halvdel af Blodet og gød det i Offerskålene, men den anden Halvdel sprængte han på Alteret.
7 Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”
Så tog han Pagtsbogen og læste den op i Folkets Påhør, og de sagde: "Vi vil gøre alt, hvad HERREN har talet, og lyde ham!"
8 Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”
Derpå tog Moses Blodet og sprængte det på Folket, idet han sagde: "Se, dette er Pagtens Blod, den Pagt, HERREN har sluttet med eder på Grundlag af alle disse Ord."
9 Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri,
Og Moses, Aron, Nadab og Abihu og halvfjerdsindstyve af Israels Ældste steg op
10 ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo.
og skuede Israels Gud; under hans Fødder var der ligesom Safirfliser, som selve Himmelen i Stråleglans.
11 Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.
Men han lagde ikke Hånd på Israeliternes ypperste Mænd. De skuede Gud, og de spiste og drak.
12 Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”
Og HERREN sagde til Moses: "Stig op til mig på Bjerget og bliv der, så vil jeg give dig Stentavlerne, Loven og Budet, som jeg har opskrevet til Vejledning for dem."
13 Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.
Da bød Moses og Josua, hans Medhjælper op, og Moses steg op på Guds Bjerg;
14 Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”
men til de Ældste sagde han: "Vent på os her, til vi kommer tilbage til eder. Se, Aron og Hur er hos eder; er der nogen, der har en Retstrætte, kan han henvende sig til dem!"
15 Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo.
Derpå steg Moses op på Bjerget. Da indhyllede Skyen Bjerget,
16 Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo.
og HERRENs Herlighed nedlod sig på Sinaj Bjerg. Og Skyen indhyllede Sinaj Bjerg i seks Dage, men den syvende Dag råbte HERREN ud fra Skyen til Moses;
17 Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo.
og medens HERRENs Herlighed viste sig for Israeliternes Øjne som en fortærende Ild på Bjergets Top,
18 Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.
gik Moses ind i Skyen og steg op på Bjerget. Og Moses blev på Bjerget i fyrretyve Dage og fyrretyve Nætter.

< Eksodo 24 >