< Eksodo 22 >

1 “Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
Jeśli ktoś ukradnie wołu lub owcę i zabije je albo sprzeda, odda pięć wołów za [jednego] wołu i cztery owce za [jedną] owcę.
2 “Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
Jeśli złodziej zostanie przyłapany przy włamaniu i tak pobity, że umrze, ten, [kto zabił], nie będzie winien [przelanej] krwi.
3 Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
Jeśli to [zrobi] po wschodzie słońca, będzie winien krwi, gdyż [złodziej] powinien wypłacić odszkodowanie. Jeśli nic nie ma, będzie sprzedany za swoją kradzież.
4 “Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
Jeśli zostaną znalezione w jego ręku skradzione dobra jeszcze żywe, czy to wół, czy osioł, czy owca, zwróci podwójnie.
5 “Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
Gdyby ktoś wypasł pole lub winnicę, bo puścił swoje bydło, aby się pasło na cudzym polu, wypłaci odszkodowanie z najlepszych [plonów] swego pola i z najlepszych [plonów] swej winnicy.
6 “Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
Jeśli wybuchnie ogień, a trafi na ciernie i spali stóg lub zboże na pniu, lub samo pole, ten, co wzniecił ogień, musi wypłacić odszkodowanie.
7 “Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
Jeśli ktoś da swemu bliźniemu pieniądze lub przedmioty do przechowania i zostanie to ukradzione z domu tego człowieka, to jeśli złodziej zostanie znaleziony, zwróci podwójnie.
8 Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
Jeśli złodziej nie zostanie znaleziony, pan tego domu stawi się przed sędziami, by [okazało się], czy nie wyciągnął ręki po własność swego bliźniego.
9 Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
W każdej spornej sprawie o wołu, osła, owcę, szatę czy jakąkolwiek zgubę, gdyby ktoś powiedział, że to jest [jego], sprawa obydwu ma trafić do sędziów; kogo sędziowie uznają winnym, ten wynagrodzi podwójnie swemu bliźniemu.
10 “Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
Jeśli ktoś odda swemu bliźniemu na przechowanie osła, wołu, owcę lub inne zwierzę, a ono zdechnie, zostanie okaleczone lub uprowadzone i nikt tego nie zobaczy;
11 ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
Wówczas przysięga przed PANEM rozstrzygnie między obydwoma, że nie wyciągnął ręki po własność swego bliźniego. Właściciel przyjmie tę [przysięgę], a [drugi] nie wypłaci odszkodowania.
12 Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
Jeśli jednak to zostało mu skradzione, wypłaci właścicielowi odszkodowanie.
13 Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
Jeśli zostało rozszarpane, to przyniesie [je jako] dowód, a za rozszarpane nie zapłaci.
14 “Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
Jeśli ktoś pożyczy [zwierzę] od swego bliźniego, a [ono] zostanie okaleczone lub zdechnie podczas nieobecności jego właściciela, musi wypłacić odszkodowanie.
15 Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
Jeśli jego właściciel był przy nim, nie zapłaci; a jeśli było wynajęte, zapłaci tylko za wynajem.
16 “Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
Jeśli ktoś uwiedzie dziewicę, która nie jest poślubiona, i położy się z nią, musi jej dać posag [i] weźmie ją sobie za żonę.
17 Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
Jeśli jej ojciec żadną miarą nie zgodzi się dać mu jej, odważy pieniądze według [zwyczaju] panieńskiego posagu.
18 “Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
Nie zostawisz czarownicy przy życiu.
19 “Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
Każdy, kto spółkuje ze zwierzęciem, poniesie śmierć.
20 “Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
Kto składa ofiary bogom, poza samym PANEM, zostanie stracony.
21 “Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
Nie zrobisz krzywdy przybyszowi ani nie będziesz go uciskać, gdyż i wy byliście przybyszami w ziemi Egiptu.
22 “Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
Nie będziecie dręczyć żadnej wdowy ani sieroty.
23 Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
Jeśli będziesz je dręczył, a one będą wołać do mnie, na pewno wysłucham ich wołania.
24 Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
Wtedy rozpali się mój gniew i pobiję was mieczem, i wasze żony będą wdowami, a wasi synowie sierotami.
25 “Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
Jeśli pożyczysz pieniądze ubogiemu z mego ludu, który mieszka wśród was, nie postąpisz wobec niego jak lichwiarz, nie będziesz go obciążać lichwą.
26 Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
Jeśli weźmiesz w zastaw szatę twego bliźniego, oddasz mu ją przed zachodem słońca;
27 chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
Bo to ubranie jest jedynym okryciem jego ciała, w tym też śpi. Jeśli będzie do mnie wołał, wysłucham go, bo jestem litościwy.
28 “Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
Nie będziesz złorzeczyć sędziom, a przełożonego twego ludu nie będziesz przeklinać.
29 “Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
Nie będziesz zwlekał [ze złożeniem] pierwocin twego [zboża] i płynnych zbiorów. Oddasz mi pierworodnego z twoich synów.
30 Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
To samo zrobisz z twoimi wołami i owcami. Siedem dni [pierworodny] będzie ze swoją matką, a ósmego dnia oddasz mi go.
31 “Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”
Będziecie dla mnie świętym ludem i nie będziecie jeść mięsa rozszarpanego na polu; wyrzucicie je psom.

< Eksodo 22 >