< Eksodo 22 >

1 “Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
Si quelqu’un vole un bœuf ou une brebis, et qu’il les tue ou les vende, il restituera cinq bœufs pour un bœuf et quatre brebis pour une brebis.
2 “Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
Si le voleur est trouvé forçant une maison ou la minant, et qu’il meure d’une blessure reçue, celui qui l’a frappé ne sera pas coupable de son sang.
3 Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
Que s’il a fait cela, le soleil levé, il a commis un homicide, et il mourra lui-même. S’il n’a pas de quoi rendre pour le larcin, il sera vendu lui-même.
4 “Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
Si ce qu’il a volé est trouvé chez lui, vivant, soit un bœuf, soit un âne, soit une brebis, il restituera le double.
5 “Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
Si quelqu’un endommage un champ ou une vigne, et qu’il laisse aller sa bête, pour qu’elle paisse ce qui est à autrui, il rendra tout ce qu’il aura de meilleur dans son champ, ou dans sa vigne, selon l’estimation du dommage.
6 “Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
Si un feu qui s’élève trouve des épines et gagne un tas de gerbes, ou bien les blés sur pied dans les champs, celui qui a allumé le feu réparera le dommage.
7 “Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
Si quelqu’un confie en garde à son ami de l’argent ou un objet quelconque, et qu’il soit volé à celui qui l’a reçu, si le voleur est trouvé, il rendra le double.
8 Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
Si le voleur reste inconnu, le maître de la maison sera conduit aux dieux, et il jurera qu’il n’a pas étendu sa main sur le bien de son prochain,
9 Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
Pour commettre le vol, soit d’un bœuf, soit d’un âne, d’une brebis, d’un vêtement et de tout ce qui peut porter dommage; c’est devant les dieux que viendra la cause de l’un et de l’autre; et si ceux-ci le condamnent, il restituera le double à son prochain.
10 “Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
Si quelqu’un confie en garde à son prochain un âne, un bœuf, une brebis, ou toute autre bête, et qu’elle meure, ou dépérisse, ou bien soit prise par les ennemis, et que personne ne l’ait vu,
11 ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
Interviendra le serment qu’il n’a pas étendu sa main sur le bien de son prochain, et le maître recevra le serment, et celui-là ne sera pas contraint de rendre.
12 Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
Que si c’est par un vol que la bête a été enlevée, il réparera le dommage envers le maître.
13 Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
Si elle a été mangée par une bête sauvage, qu’il lui apporte ce qui sera resté, et il ne restituera pas.
14 “Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
Si quelqu’un demande en prêt à son prochain quelqu’une de ses bêtes, et qu’elle dépérisse ou meure, le maître n’étant pas présent, il sera forcé de la rendre.
15 Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
Que si le maître se trouve présent, il ne restituera pas, surtout s’il était venu la louer, pour le prix de son travail.
16 “Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
Si quelqu’un séduit une vierge non encore fiancée, et dort avec elle, il la dotera et la prendra pour femme.
17 Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
Si le père de la vierge ne veut pas la donner, il rendra de l’argent selon la dot que les vierges ont coutume de recevoir.
18 “Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
Tu ne laisseras pas vivre ceux qui usent de maléfices.
19 “Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
Que celui qui commet un crime avec une bête, meure de mort.
20 “Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
Celui qui sacrifie à d’autres dieux qu’au Seigneur seul sera mis à mort.
21 “Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
Tu ne contristeras point l’étranger, et tu ne l’affligeras point; car vous avez été étrangers vous-mêmes dans la terre d’Egypte.
22 “Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
Vous ne nuirez point à la veuve et à l’orphelin.
23 Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
Si vous les offensez, ils crieront fortement vers moi, et j’entendrai leur clameur;
24 Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
Et ma fureur s’indignera, puis je vous frapperai du glaive, et vos femmes seront veuves et vos fils orphelins.
25 “Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
Si tu prêtes de l’argent à mon peuple pauvre qui habite avec toi, tu ne le presseras point comme un exacteur, et tu ne l’accableras point d’usures.
26 Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
Si tu prends en gage de ton prochain un vêtement, tu lui rendras avant le coucher du soleil.
27 chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
Car c’est le seul dont il se couvre, le seul vêtement de sa chair, et il n’en a pas un autre dans lequel il dorme: s’il crie vers moi, je l’exaucerai, parce que je suis miséricordieux.
28 “Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
Tu ne parleras point mal des dieux, et tu ne maudiras point le prince de ton peuple.
29 “Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
Tu ne différeras point à rendre tes dîmes et tes prémices: tu me donneras le premier-né de tes fils.
30 Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
Pour tes bœufs aussi et tes brebis tu feras de même: que pendant sept jours le premier-né soit avec sa mère, et au huitième jour tu me le rendras.
31 “Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”
Vous me serez des hommes consacrés; vous ne mangerez point de la chair dont les bêtes sauvages auront déjà goûté, mais vous la jetterez aux chiens.

< Eksodo 22 >