< Eksodo 22 >

1 “Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
If he will steal anyone an ox or a sheep and he will slaughter it or he has sold it five cattle he will repay in place of the ox and four sheep in place of the sheep.
2 “Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
If in breaking in he will be found the thief and he will be struck and he will die there not for him [will be] blood.
3 Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
If it has risen the sun on him blood [will be] for him certainly he will make restitution if nothing [belongs] to him and he will be sold for theft his.
4 “Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
If actually it will be found in hand his the thing stolen from an ox unto a donkey unto a sheep alive twofold he will make restitution.
5 “Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
If he will cause to be grazed over anyone a field or a vineyard and he will let go (cattle his *Q(K)*) and it will graze in [the] field of another [person] [the] best of field his and [the] best of vineyard his he will make compensation.
6 “Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
If it will go forth a fire and it will find thornbushes and it will be consumed a heap of sheaves or the standing grain or the field certainly he will make compensation the [one who] kindled the fire.
7 “Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
If he will give anyone to neighbor his money or articles to keep [them] and it will be stolen from [the] house of the person if he will be found the thief he will make restitution twofold.
8 Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
If not he will be found the thief and he will be brought near [the] master of the house to the judges if not he had stretched out hand his on [the] property of neighbor his.
9 Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
On every matter of transgression on an ox on a donkey on a sheep on a garment on every thing lost which anyone will say that [is] it this to the judges it will come [the] case of both of them [the one] whom they will condemn as guilty! [the] judges he will make restitution twofold to neighbor his.
10 “Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
If he will give anyone to neighbor his a donkey or an ox or a sheep and every animal to keep [it] and it will die or it was maimed or it was captured there not [was one who] saw.
11 ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
[the] oath of Yahweh it will be between [the] two of them if not he had stretched out hand his on [the] property of neighbor his and he will accept [it] owner its and not he will make compensation.
12 Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
And if certainly it will be stolen from with him he will make restitution to owner its.
13 Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
Certainly [if] it will be torn in pieces he will bring it evidence the torn animal not he will make restitution.
14 “Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
And if he will ask anyone from with neighbor his and it will be maimed or it died owner its not [was] with it certainly he will make restitution.
15 Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
If owner its [was] with it not he will make restitution if [was] hired it it came for hire its.
16 “Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
And if he will seduce a man a virgin who not she was betrothed and he will lie with her certainly he will pay [the] bride-price for her for himself to a wife.
17 Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
If absolutely he will refuse father her to give her to him silver he will weigh out according to [the] bride-price of virgins.
18 “Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
A sorceress not you will let live.
19 “Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
Any [one who] lies with an animal certainly he will be put to death.
20 “Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
[one who] sacrifices To the gods he will be dedicated to destruction except to Yahweh to only him.
21 “Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
And a sojourner not you must maltreat and not you must oppress him for sojourners you were in [the] land of Egypt.
22 “Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
Any widow and a fatherless one not you must afflict!
23 Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
Certainly [if] you will afflict him that except carefully he will cry out to me certainly I will hear cry of distress his.
24 Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
And it will burn anger my and I will kill you with the sword and they will be wives your widows and children your fatherless ones.
25 “Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
If money - you will lend to people my the poor [person] with you not you must be to him like a creditor not you must put! on him interest.
26 Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
Certainly [if] you will take as pledge [the] cloak of neighbor your until goes the sun you will return it to him.
27 chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
For it ([is] covering his *Q(k)*) to alone it it [is] cloak his for skin his in what? will he lie down and it will be that he will cry out to me and I will hear for [am] gracious I.
28 “Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
God not you must curse and a leader among people your not you must curse.
29 “Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
Full produce your and juice your not you must delay [the] firstborn of sons your you will give to me.
30 Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
Thus you will do to ox your to sheep your seven days it will be with mother its on the day eighth you will give it to me.
31 “Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”
And people of holiness you will be! of me and flesh in the field a torn animal not you must eat to the dog[s] you will throw! it.

< Eksodo 22 >