< Eksodo 21 >
1 “Uwawuze Aisraeli malamulo awa:
“Now these are the decrees that you must set before them:
2 “Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu.
'If you buy a Hebrew servant, he is to serve for six years, and in the seventh year he will go free without paying anything.
3 Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso.
If he came by himself, he must go free by himself; if he is married, then his wife must go free with him.
4 Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.
If his master gave him a wife and she bore him sons or daughters, the wife and her children will belong to her master, and he must go free by himself.
5 “Koma ngati kapoloyo alengeza kuti, ‘Ine sindikufuna kumasulidwa chifukwa ndimakonda mbuye wanga, mkazi wanga ndi ana,’
But if the servant plainly says, “I love my master, my wife, and my children; I will not go out free,”
6 mbuye wakeyo abwere naye kwa Yehova. Abwere naye pa chitseko kapena pa mphuthu zachitseko ndipo abowole khutu lake ndi chitsulo. Ndipo iye adzakhala kapolo wake moyo wake wonse.
then his master must bring him to God. The master must bring him to a door or doorpost, and his master must bore his ear through with an awl. Then the servant will serve him for life.
7 “Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna.
If a man sells his daughter as a female servant, she must not go free as the male servants do.
8 Koma ngati mkaziyo sakukondweretsa bwana wake amene wamusankha kuti amukwatire, amulole kuti awomboledwe. Bwanayo alibe mphamvu zomugulitsa kwa anthu achilendo, chifukwa iyeyo waphwanya pangano lake lomukwatira iye.
If she does not please her master, who has designated her for himself, then he must let her be bought back. He has no right to sell her to a foreign people. He has no such right, since he has treated her deceitfully.
9 Ngati anamusankha kuti akhale mkazi wa mwana wake, ayenera kumusunga ngati mwana wake wamkazi.
If her master designates her as a wife for his son, he must treat her the same as if she were his daughter.
10 Ngati akwatira mkazi wina, asamumane woyambayo chakudya ngakhale chovala ndipo apiritirize kugona naye ngati mkazi wake.
If he takes another wife for himself, he must not diminish her food, clothing, or her marital rights.
11 Koma ngati sangathe kumuchitira zonsezi, ndiye amuleke apite popanda kulipira kanthu.
But if he does not provide these three things for her, then she can go free without paying any money.
12 “Munthu aliyense amene amenya mnzake namupha, iyenso ayenera kuphedwa.
Whoever strikes a man so that he dies, that person must surely be put to death.
13 Koma ngati sanachite dala, ndipo Mulungu analola kuti zichitike, iyeyo athawire ku malo kumene ndidzakupatsani.
If the man did not do it with premeditation, but instead by accident, then I will fix a place to where he can flee.
14 Koma ngati munthu akonza chiwembu ndi kupha mnzake mwadala, ameneyo muchotseni ngakhale ku guwa langa lansembe ndipo aphedwe.
If a man willfully attacks his neighbor and kills him according to a cunning plan, then you must take him, even if he is at God's altar, so that he may die.
15 “Munthu aliyense amene amenya abambo ake kapena mayi ake ayenera kuphedwa.
Whoever hits his father or mother must surely be put to death.
16 “Munthu aliyense amene aba munthu mnzake, ndi kukamugulitsa, kapena kumangomusunga, ayenera kuphedwa.
Whoever kidnaps a person—whether the kidnapper sells him, or that person is found in his hand—that kidnapper must be put to death.
17 “Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.
Whoever curses his father or his mother must surely be put to death.
18 “Ngati anthu awiri akangana ndipo wina amenya mnzake ndi mwala kapena nkhonya koma wosamupha, womenyedwayo akadwala nagona pa bedi,
If men fight and one hits the other with a stone or with his fist, and that person does not die, but is confined to his bed;
19 kenaka nachira ndi kuyamba kuyenda ndi ndodo kutuluka kunja kwa nyumba yake, ndiye kuti womenya mnzakeyo sadzayimbidwa mlandu. Komabe adzayenera kulipira womenyedwayo chifukwa cha nthawi imene anagona pa bedi ija, ndiponso ayenera kumusala mpaka atachiritsitsa.
then if he recovers and is able to walk about using his staff, the man who struck him must pay for the loss of his time; he must also pay for his complete recovery. But that man is not guilty of murder.
20 “Ngati munthu amenya kapolo wake wamwamuna kapena mdzakazi ndi ndodo, kapolo uja ndikufa chifukwa cha kumenyedwako, munthuyo ayenera kulangidwa.
If a man hits his male servant or his female servant with a staff, and if the servant dies as a result of the blow, then that man must surely be punished.
21 Koma ngati kapolo uja akhala ndi moyo tsiku lonse kapena masiku awiri, ndiye kuti mbuye uja asalangidwe chifukwa kapolo ndi chuma chake.
However, if the servant lives for a day or two, the master must not be punished, for he will have suffered the loss of the servant.
22 “Ngati anthu akumenyana ndi kupweteka mayi woyembekezera, mayiyo napita padera, koma osavulala, wolakwayo ayenera kulipira chilichonse chimene mwamuna wake wa mkaziyo adzalamula ndipo bwalo lamilandu lavomereza.
If men fight together and hurt a pregnant woman so that she miscarries, but there is no other injury to her, then the guilty man must surely be fined as the woman's husband demands it from him, and he must pay as the judges determine.
23 Koma ngati wavulazidwa kwambiri, ndiye malipiro ake adzakhala motere: moyo kulipa moyo,
But if there is serious injury, then you must give a life for a life,
24 diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, mkono kulipa mkono, phazi kulipa phazi.
an eye for an eye, a tooth for a tooth, a hand for a hand, a foot for a foot,
25 Kutentha ndi moto kulipa kutentha ndi moto, bala kulipa bala, mkwingwirima kulipa mkwingwirima.
a burn for a burn, a wound for a wound, or a bruise for a bruise.
26 “Ngati munthu amenya wantchito wake wa mwamuna kapena mdzakazi wake pa diso ndi kuliwononga, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a diso lake.
If a man hits the eye of his male servant or of his female servant and destroys it, then he must let the servant go free in compensation for his eye.
27 Ndipo ngati agulula dzino la wantchito wamwamuna kapena mdzakazi, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a dzino lake.
If he knocks out a tooth of his male servant or female servant, he must let the servant go free as compensation for the tooth.
28 “Ngati ngʼombe ipha munthu wamwamuna kapena wamkazi ndi nyanga yake, iponyedwe miyala ndipo nyama yake isadyedwe. Ndipo mwini ngʼombeyo asayimbidwe mlandu.
If an ox gores a man or a woman to death, the ox must surely be stoned, and its flesh must not be eaten; but the ox's owner must be acquitted of guilt.
29 Koma ngati ngʼombeyo inali ndi chizolowezi chogunda anthu ndipo mwini wakeyo anachenjezedwa koma iye sanayimange ndipo yapha mwamuna kapena mkazi, ngʼombeyo iponyedwe miyala ndipo mwini wakeyo aphedwenso.
But if the ox had a habit of goring in the past, and its owner was warned but did not keep it in, and the ox has killed a man or a woman, that ox must be stoned, and its owner also must be put to death.
30 Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake.
If a payment is required for his life, he must pay whatever he is required to pay.
31 Lamulo ili ligwirenso ntchito ngati ngʼombeyo yagunda mwana wamwamuna kapena wamkazi.
If the ox has gored a man's son or daughter, the ox's owner must do what this decree requires him to do.
32 Ngati ngʼombeyo yagunda kapolo wamwamuna kapena mdzakazi, mwini ngʼombeyo apereke masekeli makumi atatu a siliva kwa mwini kapoloyo, ndipo ngʼombeyo iponyedwe miyala.
If the ox gores a male servant or a female servant, the ox's owner must pay thirty shekels of silver, and the ox must be stoned.
33 “Munthu akasiya dzenje lapululu kapena akakumba dzenje koma wosaphimbapo, ndipo ngʼombe kapena bulu nʼkugweramo,
If a man opens a pit, or if a man digs a pit and does not cover it, and an ox or a donkey falls into it,
34 mwini dzenjelo amulipire mwini chiweto chakufacho koma iye atenge chiwetocho.
the owner of the pit must repay the loss. He must give money to the dead animal's owner, and the dead animal will become his.
35 “Ngati ngʼombe ya munthu wina ipha ngʼombe ya mnzake, ngʼombe yamoyo ija igulitsidwe ndipo anthu awiriwo agawane pakati ndalama yake. Achite chimodzimodzi ndi ngʼombe yakufa ija.
If one man's ox hurts another man's ox so that it dies, then they must sell the live ox and divide its price, and they must also divide the dead ox.
36 Koma zikadziwika kuti ngʼombeyo inali ndi khalidwe logunda, ndipo mwini wake samayitsekera mʼkhola, mwini ngʼombeyo alipire ngʼombe ina yamoyo koma atenge yakufayo.”
But if it was known that the ox had a habit of goring in time past, and its owner has not kept it in, he must surely pay ox for ox, and the dead animal will become his own.