< Eksodo 21 >

1 “Uwawuze Aisraeli malamulo awa:
And these [are] the judgments which you will set before them.
2 “Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu.
For you will buy a slave Hebrew six years he will serve and in the seventh [year] he will go out to free [person] without paying.
3 Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso.
If with body his he will come with body his he will go out if [is the] husband of a wife he and she will go out wife his with him.
4 Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.
If master his he will give to him a wife and she will bear to him sons or daughters the woman and children her she will belong to master her and he he will go out with body his.
5 “Koma ngati kapoloyo alengeza kuti, ‘Ine sindikufuna kumasulidwa chifukwa ndimakonda mbuye wanga, mkazi wanga ndi ana,’
And if carefully he will say the slave I love master my wife my and children my not I will go out a free [person].
6 mbuye wakeyo abwere naye kwa Yehova. Abwere naye pa chitseko kapena pa mphuthu zachitseko ndipo abowole khutu lake ndi chitsulo. Ndipo iye adzakhala kapolo wake moyo wake wonse.
And he will bring near him master his to God and he will bring near him to the door or to the doorpost and he will pierce master his ear his with the awl and he will serve him for ever.
7 “Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna.
And if he will sell a man daughter his to a female slave not she will go out when go out the [male] slaves.
8 Koma ngati mkaziyo sakukondweretsa bwana wake amene wamusankha kuti amukwatire, amulole kuti awomboledwe. Bwanayo alibe mphamvu zomugulitsa kwa anthu achilendo, chifukwa iyeyo waphwanya pangano lake lomukwatira iye.
If she is bad in [the] eyes of master her who (for himself *Q(K)*) he designated her and he will let be ransomed her to a people foreign not he will have dominion to sell her because has dealt treacherously he with her.
9 Ngati anamusankha kuti akhale mkazi wa mwana wake, ayenera kumusunga ngati mwana wake wamkazi.
And if for son his he will designate her according to [the] custom of daughters he will do to her.
10 Ngati akwatira mkazi wina, asamumane woyambayo chakudya ngakhale chovala ndipo apiritirize kugona naye ngati mkazi wake.
If another [woman] he will take for himself food her covering her and right to intercourse her not he will reduce.
11 Koma ngati sangathe kumuchitira zonsezi, ndiye amuleke apite popanda kulipira kanthu.
And if three [things] these not he will do for her and she will go out without paying not money.
12 “Munthu aliyense amene amenya mnzake namupha, iyenso ayenera kuphedwa.
[one who] will strike anyone And he will die certainly he will be put to death.
13 Koma ngati sanachite dala, ndipo Mulungu analola kuti zichitike, iyeyo athawire ku malo kumene ndidzakupatsani.
And that not he was lying in wait and God he allowed to happen to hand his and I will designate for you a place where he will flee there.
14 Koma ngati munthu akonza chiwembu ndi kupha mnzake mwadala, ameneyo muchotseni ngakhale ku guwa langa lansembe ndipo aphedwe.
And if he will act presumptuously anyone on neighbor his to kill him with cunning from with altar my you will take him to die.
15 “Munthu aliyense amene amenya abambo ake kapena mayi ake ayenera kuphedwa.
And [one who] will strike father his and mother his certainly he will be put to death.
16 “Munthu aliyense amene aba munthu mnzake, ndi kukamugulitsa, kapena kumangomusunga, ayenera kuphedwa.
And [one who] will steal anyone and he will sell him and he will be found in hand his certainly he will be put to death.
17 “Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.
And [one who] will curse father his and mother his certainly he will be put to death.
18 “Ngati anthu awiri akangana ndipo wina amenya mnzake ndi mwala kapena nkhonya koma wosamupha, womenyedwayo akadwala nagona pa bedi,
And if they will quarrel! men and he will strike anyone neighbor his with a stone or with a fist and not he will die and he will fall to a bed.
19 kenaka nachira ndi kuyamba kuyenda ndi ndodo kutuluka kunja kwa nyumba yake, ndiye kuti womenya mnzakeyo sadzayimbidwa mlandu. Komabe adzayenera kulipira womenyedwayo chifukwa cha nthawi imene anagona pa bedi ija, ndiponso ayenera kumusala mpaka atachiritsitsa.
If he will arise and he will walk about on the outside on staff his and he will be free from guilt the [one who] struck only sitting still his he will pay for and certainly he will have [him] healed.
20 “Ngati munthu amenya kapolo wake wamwamuna kapena mdzakazi ndi ndodo, kapolo uja ndikufa chifukwa cha kumenyedwako, munthuyo ayenera kulangidwa.
And if he will strike anyone [male] slave his or female slave his with the rod and he will die under hand his certainly he will be avenged.
21 Koma ngati kapolo uja akhala ndi moyo tsiku lonse kapena masiku awiri, ndiye kuti mbuye uja asalangidwe chifukwa kapolo ndi chuma chake.
Nevertheless if a day or two days he will remain not he will be avenged for [is] money his he.
22 “Ngati anthu akumenyana ndi kupweteka mayi woyembekezera, mayiyo napita padera, koma osavulala, wolakwayo ayenera kulipira chilichonse chimene mwamuna wake wa mkaziyo adzalamula ndipo bwalo lamilandu lavomereza.
And if they will struggle together men and they will strike a woman pregnant and they will come out children her and not it will be harm certainly he will be fined just as he will impose on him [the] husband of the woman and he will give for [the] estimate.
23 Koma ngati wavulazidwa kwambiri, ndiye malipiro ake adzakhala motere: moyo kulipa moyo,
And if harm it will be and you will give a life in place of a life.
24 diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, mkono kulipa mkono, phazi kulipa phazi.
An eye in place of an eye a tooth in place of a tooth a hand in place of a hand a foot in place of a foot.
25 Kutentha ndi moto kulipa kutentha ndi moto, bala kulipa bala, mkwingwirima kulipa mkwingwirima.
Burning in place of burning bruise in place of bruise wound in place of wound.
26 “Ngati munthu amenya wantchito wake wa mwamuna kapena mdzakazi wake pa diso ndi kuliwononga, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a diso lake.
And if he will strike anyone [the] eye of [male] slave his or [the] eye of female slave his and he will destroy it to free [person] he will set free him in place of eye his.
27 Ndipo ngati agulula dzino la wantchito wamwamuna kapena mdzakazi, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a dzino lake.
And if [the] tooth of [male] slave his or [the] tooth of female slave his he will knock out to free [person] he will set free him in place of tooth his.
28 “Ngati ngʼombe ipha munthu wamwamuna kapena wamkazi ndi nyanga yake, iponyedwe miyala ndipo nyama yake isadyedwe. Ndipo mwini ngʼombeyo asayimbidwe mlandu.
And if it will gore an ox a man or a woman and he will die certainly it will be stoned to death the ox and not it will be eaten meat its and [the] owner of the ox [will be] free from guilt.
29 Koma ngati ngʼombeyo inali ndi chizolowezi chogunda anthu ndipo mwini wakeyo anachenjezedwa koma iye sanayimange ndipo yapha mwamuna kapena mkazi, ngʼombeyo iponyedwe miyala ndipo mwini wakeyo aphedwenso.
And if [will be] an ox prone to gore it from yesterday three days ago and it has been protested on owner its and not he will guard it and it will kill a man or a woman the ox it will be stoned to death and also owner its he will be put to death.
30 Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake.
If a ransom it will be imposed on him and he will give [the] ransom of life his according to all that it will be imposed on him.
31 Lamulo ili ligwirenso ntchito ngati ngʼombeyo yagunda mwana wamwamuna kapena wamkazi.
Or a son it will gore or a daughter it will gore according to the judgment this it will be done to him.
32 Ngati ngʼombeyo yagunda kapolo wamwamuna kapena mdzakazi, mwini ngʼombeyo apereke masekeli makumi atatu a siliva kwa mwini kapoloyo, ndipo ngʼombeyo iponyedwe miyala.
If a [male] slave it will gore the ox or a female slave silver - thirty shekels he will give to master his and the ox it will be stoned to death.
33 “Munthu akasiya dzenje lapululu kapena akakumba dzenje koma wosaphimbapo, ndipo ngʼombe kapena bulu nʼkugweramo,
And if he will open anyone a pit or for he will dig anyone a pit and not he will cover it and it will fall there an ox or a donkey.
34 mwini dzenjelo amulipire mwini chiweto chakufacho koma iye atenge chiwetocho.
[the] owner of The pit he will make compensation silver he will repay to owner its and the dead [animal] it will be[long] to him.
35 “Ngati ngʼombe ya munthu wina ipha ngʼombe ya mnzake, ngʼombe yamoyo ija igulitsidwe ndipo anthu awiriwo agawane pakati ndalama yake. Achite chimodzimodzi ndi ngʼombe yakufa ija.
And if it will strike [the] ox of anyone [the] ox of neighbor his and it will die and they will sell the ox living and they will divide silver its and also the dead [animal] they will divide!
36 Koma zikadziwika kuti ngʼombeyo inali ndi khalidwe logunda, ndipo mwini wake samayitsekera mʼkhola, mwini ngʼombeyo alipire ngʼombe ina yamoyo koma atenge yakufayo.”
Or it is known that [is] an ox prone to gore it from yesterday three days ago and not he guarded it owner its certainly he will make compensation an ox in place of the ox and the dead [animal] it will be[long] to him.

< Eksodo 21 >