< Eksodo 21 >

1 “Uwawuze Aisraeli malamulo awa:
De Lovbud, du skal forelægge dem, er følgende:
2 “Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu.
Naar du køber dig en hebræisk Træl, skal han trælle i seks Aar, men i det syvende skal han frigives uden Vederlag.
3 Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso.
Er han ugift, naar han kommer til dig, skal han frigives alene; er han gift, skal hans Hustru frigives sammen med ham.
4 Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.
Hvis hans Herre giver ham en Hustru og hun føder ham Sønner eller Døtre, da skal Hustruen og hendes Børn tilhøre hendes Herre, og Trællen frigives alene.
5 “Koma ngati kapoloyo alengeza kuti, ‘Ine sindikufuna kumasulidwa chifukwa ndimakonda mbuye wanga, mkazi wanga ndi ana,’
Hvis han imidlertid erklærer: »Jeg har faaet Kærlighed til min Herre, min Hustru og mine Børn, jeg vil ikke have min Frihed!«
6 mbuye wakeyo abwere naye kwa Yehova. Abwere naye pa chitseko kapena pa mphuthu zachitseko ndipo abowole khutu lake ndi chitsulo. Ndipo iye adzakhala kapolo wake moyo wake wonse.
da skal hans Herre føre ham hen til Gud og stille ham op ad Døren eller Dørstolpen, og hans Herre skal gennembore hans Øre med en Syl, og saa skal han være hans Træl for Livstid.
7 “Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna.
Naar en Mand sælger sin Datter som Trælkvinde, skal hun ikke frigives som Trællene.
8 Koma ngati mkaziyo sakukondweretsa bwana wake amene wamusankha kuti amukwatire, amulole kuti awomboledwe. Bwanayo alibe mphamvu zomugulitsa kwa anthu achilendo, chifukwa iyeyo waphwanya pangano lake lomukwatira iye.
Dersom hun paadrager sig sin Herres Mishag, efter at han har haft Omgang med hende, skal han tillade, at hun købes fri; han har ikke Lov at sælge hende til fremmede Folk, naar han har gjort Uret imod hende;
9 Ngati anamusankha kuti akhale mkazi wa mwana wake, ayenera kumusunga ngati mwana wake wamkazi.
hvis han derimod bestemmer, at hun skal være hans Søns Hustru, skal han behandle hende, som det tilkommer Døtre.
10 Ngati akwatira mkazi wina, asamumane woyambayo chakudya ngakhale chovala ndipo apiritirize kugona naye ngati mkazi wake.
Hvis han tager sig en anden, har han ikke Lov at forholde den første den Kødspise, Klædning og ægteskabelige Ret, der tilkommer hende.
11 Koma ngati sangathe kumuchitira zonsezi, ndiye amuleke apite popanda kulipira kanthu.
Forholder han hende nogen af disse tre Ting, skal hun frigives uden Vederlag og Betaling.
12 “Munthu aliyense amene amenya mnzake namupha, iyenso ayenera kuphedwa.
Den, der slaar en Mand ihjel, skal lide Døden.
13 Koma ngati sanachite dala, ndipo Mulungu analola kuti zichitike, iyeyo athawire ku malo kumene ndidzakupatsani.
Gør han det imidlertid ikke med Forsæt, men styres hans Haand af Gud, vil jeg anvise dig et Sted, hvor han kan ty hen.
14 Koma ngati munthu akonza chiwembu ndi kupha mnzake mwadala, ameneyo muchotseni ngakhale ku guwa langa lansembe ndipo aphedwe.
Naar derimod en handler med Overlæg, saa han med List slaar sin Næste ihjel, da skal du rive ham bort fra mit Alter, for at han kan lide Døden.
15 “Munthu aliyense amene amenya abambo ake kapena mayi ake ayenera kuphedwa.
Den, der slaar sin Fader eller Moder, skal lide Døden.
16 “Munthu aliyense amene aba munthu mnzake, ndi kukamugulitsa, kapena kumangomusunga, ayenera kuphedwa.
Den, der stjæler et Menneske, skal lide Døden, hvad enten han har solgt det, eller det endnu findes hos ham.
17 “Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.
Den, der forbander sin Fader eller Moder, skal lide Døden.
18 “Ngati anthu awiri akangana ndipo wina amenya mnzake ndi mwala kapena nkhonya koma wosamupha, womenyedwayo akadwala nagona pa bedi,
Naar der opstaar Strid mellem Mænd, og den ene slaar den anden med en Sten eller med Næven, saa at han vel ikke dør deraf, men dog maa holde Sengen,
19 kenaka nachira ndi kuyamba kuyenda ndi ndodo kutuluka kunja kwa nyumba yake, ndiye kuti womenya mnzakeyo sadzayimbidwa mlandu. Komabe adzayenera kulipira womenyedwayo chifukwa cha nthawi imene anagona pa bedi ija, ndiponso ayenera kumusala mpaka atachiritsitsa.
saa skal Gerningsmanden være sagesløs, hvis han kan staa op og gaa ud støttet til sin Stok; kun skal han godtgøre ham hans Tidsspilde og sørge for hans Helbredelse.
20 “Ngati munthu amenya kapolo wake wamwamuna kapena mdzakazi ndi ndodo, kapolo uja ndikufa chifukwa cha kumenyedwako, munthuyo ayenera kulangidwa.
Naar en Mand slaar sin Træl eller Trælkvinde med sin Stok, saa de dør paa Stedet, skal han straffes derfor;
21 Koma ngati kapolo uja akhala ndi moyo tsiku lonse kapena masiku awiri, ndiye kuti mbuye uja asalangidwe chifukwa kapolo ndi chuma chake.
men hvis de bliver i Live en Dag eller to, skal han ikke straffes; det er jo hans egne Penge.
22 “Ngati anthu akumenyana ndi kupweteka mayi woyembekezera, mayiyo napita padera, koma osavulala, wolakwayo ayenera kulipira chilichonse chimene mwamuna wake wa mkaziyo adzalamula ndipo bwalo lamilandu lavomereza.
Naar Mænd kommer i Slagsmaal og støder til en frugtsommelig Kvinde, saa hun nedkommer i Utide, men der ellers ingen Ulykke sker, da skal han bøde, hvad Kvindens Mand paalægger ham, og give Erstatning for det dødfødte Barn.
23 Koma ngati wavulazidwa kwambiri, ndiye malipiro ake adzakhala motere: moyo kulipa moyo,
Men hvis der sker en Ulykke, skal du bøde Liv for Liv,
24 diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, mkono kulipa mkono, phazi kulipa phazi.
Øje for Øje, Tand for Tand, Haand for Haand, Fod for Fod,
25 Kutentha ndi moto kulipa kutentha ndi moto, bala kulipa bala, mkwingwirima kulipa mkwingwirima.
Brandsaar for Brandsaar, Saar for Saar, Skramme for Skramme.
26 “Ngati munthu amenya wantchito wake wa mwamuna kapena mdzakazi wake pa diso ndi kuliwononga, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a diso lake.
Naar en Mand slaar sin Træl eller sin Trælkvinde i Øjet og ødelægger det, skal han give dem fri til Erstatning for Øjet;
27 Ndipo ngati agulula dzino la wantchito wamwamuna kapena mdzakazi, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a dzino lake.
og hvis han slaar en Tand ud paa sin Træl eller Trælkvinde, skal han give dem fri til Erstatning for Tanden.
28 “Ngati ngʼombe ipha munthu wamwamuna kapena wamkazi ndi nyanga yake, iponyedwe miyala ndipo nyama yake isadyedwe. Ndipo mwini ngʼombeyo asayimbidwe mlandu.
Naar en Okse stanger en Mand eller Kvinde ihjel, skal Oksen stenes, og dens Kød maa ikke spises, men Ejeren er sagesløs;
29 Koma ngati ngʼombeyo inali ndi chizolowezi chogunda anthu ndipo mwini wakeyo anachenjezedwa koma iye sanayimange ndipo yapha mwamuna kapena mkazi, ngʼombeyo iponyedwe miyala ndipo mwini wakeyo aphedwenso.
men hvis Oksen allerede tidligere har villet stange, og dens Ejer er advaret, men alligevel ikke passer paa den, og den saa dræber en Mand eller Kvinde, da skal Oksen stenes, og dens Ejer skal ogsaa lide Døden;
30 Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake.
men hvis der paalægges ham Sonepenge, skal han betale saa stor en Løsesum for sit Liv, som der kræves af ham.
31 Lamulo ili ligwirenso ntchito ngati ngʼombeyo yagunda mwana wamwamuna kapena wamkazi.
Ogsaa hvis den stanger en Dreng eller en Pige, skal han behandles efter samme Lovbud.
32 Ngati ngʼombeyo yagunda kapolo wamwamuna kapena mdzakazi, mwini ngʼombeyo apereke masekeli makumi atatu a siliva kwa mwini kapoloyo, ndipo ngʼombeyo iponyedwe miyala.
Men hvis Oksen stanger en Træl eller Trælkvinde, skal han betale deres Herre tredive Sekel Sølv, og Oksen skal stenes.
33 “Munthu akasiya dzenje lapululu kapena akakumba dzenje koma wosaphimbapo, ndipo ngʼombe kapena bulu nʼkugweramo,
Naar en Mand tager Dækket af en Cisterne eller graver en Cisterne uden at dække den til, og en Okse eller et Æsel saa falder deri,
34 mwini dzenjelo amulipire mwini chiweto chakufacho koma iye atenge chiwetocho.
da skal Brøndens Ejer erstatte det; han skal give Dyrets Ejer Erstatning i Penge, men det døde Dyr skal tilfalde ham,
35 “Ngati ngʼombe ya munthu wina ipha ngʼombe ya mnzake, ngʼombe yamoyo ija igulitsidwe ndipo anthu awiriwo agawane pakati ndalama yake. Achite chimodzimodzi ndi ngʼombe yakufa ija.
Naar en Mands Okse stanger en andens Okse ihjel, skal de sælge den levende Okse og dele Pengene, og ligeledes skal de dele det døde Dyr.
36 Koma zikadziwika kuti ngʼombeyo inali ndi khalidwe logunda, ndipo mwini wake samayitsekera mʼkhola, mwini ngʼombeyo alipire ngʼombe ina yamoyo koma atenge yakufayo.”
Men hvis det er vitterligt, at Oksen tidligere har villet stange, og dens Ejer ikke har passet paa den, da skal han erstatte Okse med Okse, men det døde Dyr skal tilfalde ham.

< Eksodo 21 >