< Eksodo 20 >

1 Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:
God spoke all these words, saying,
2 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
“I am Adonai your God, who brought you out of the land of Egypt [Abode of slavery], out of the house of bondage.
3 “Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.”
“You shall have no other elohim ·deities, judges· before me.
4 “Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
“You shall not make for yourselves an idol, nor any image of anything that is in the heavens above, or that is in the earth beneath, or that is in the water under the earth:
5 Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane.
you shall not hawa ·bow low, prostrate· yourself down to them, nor abad ·serve· them, for I, Adonai your God, am a jealous God, visiting the iniquity of the fathers on the children, on the third and on the fourth generation of those who hate me,
6 Koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda, ndi kusunga malamulo anga.
and showing cheshed ·loving-kindness· to thousands of those who 'ahav ·affectionately love· me and keep my mitzvot ·instructions·.
7 “Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
“You shall not take the name of Adonai your God in vain, for Adonai will not hold him guiltless who takes his name in vain.
8 “Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.
“Remember the Sabbath day, to keep it holy.
9 Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi.
You shall labor six days, and do all your work,
10 Koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi, wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu, ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu.
but the seventh day is a Sabbath to Adonai your God. You shall not do any work in it, you, nor your son, nor your daughter, your male servant, nor your female servant, nor your livestock, nor your stranger who is within your gates;
11 Pakuti Yehova anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo mʼmasiku asanu ndi limodzi. Iye anapuma pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Kotero Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale loyera.
for in six days Adonai made heaven and earth, the sea, and all that is in them, and rested the seventh day; therefore Adonai blessed the Sabbath ·To cease· day, and made it holy.
12 “Lemekeza abambo ako ndi amayi ako kuti ukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
“Honor your father and your mother, so that your days may be long in the land which Adonai your God gives you.
13 “Usaphe.
“You shall not murder.
14 “Usachite chigololo.
“You shall not commit adultery.
15 “Usabe.
“You shall not steal.
16 “Usapereke umboni womunamizira mnzako.
“You shall not give false witness against your neighbor.
17 “Usasirire nyumba ya mnzako. Usasirire mkazi wa mnzako kapena wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
“You shall not covet your neighbor’s house. You shall not covet your neighbor’s wife, nor his male servant, nor his female servant, nor his ox, nor his donkey, nor anything that is your neighbor’s.”
18 Pamene anthu ankamva mabingu ndi kuona ziphaliwali ndi kumvanso lipenga ndi kuona utsi umene umafuka mʼphiri, ananjenjemera ndi mantha. Ndipo iwo anayima patali.
All the people perceived the thunder, the lightnings, the sound of the shofar ·ram horn·, and the mountain smoking. When the people saw it, they trembled, and stayed at a distance.
19 Ndipo anati kwa Mose, “Iwe utiyankhule ndipo tidzamvera. Koma usalole kuti Mulungu atiyankhule, tingafe.”
They said to Moses [Drawn out], “Speak with us yourself, and we will sh'ma ·hear obey·; but don’t let God speak with us, lest we die.”
20 Koma Mose anati kwa anthuwo, “Musachite mantha. Mulungu wabwera kudzakuyesani kuti mukhale ndi mtima woopa Mulungu kuti musamuchimwire.”
Moses [Drawn out] said to the people, “Don’t be afraid, for God has come to test you, and that his fear may be before you, that you won’t sin.”
21 Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.
The people stayed at a distance, and Moses [Drawn out] came near to the thick darkness where God was.
22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Awuze izi Aisraeli: ‘Inu mwaona nokha kuti Ine ndakuyankhulani kuchokera kumwamba.
Adonai said to Moses [Drawn out], “This is what you shall tell the children of Israel [God prevails]: ‘You yourselves have seen that I have talked with you from heaven.
23 Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’”
You shall most certainly not make alongside of me deities of silver, or deities of gold for yourselves.
24 Mundimangire guwa ladothi ndipo muziperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe zanu. Pamalo paliponse pamene Ine ndidzakonza kuti muzinditamandirapo, ndidzabwera ndi kukudalitsani.
You shall make an altar of earth for me, and shall sacrifice on it your burnt offerings and your peace offerings, your sheep and your cattle. In every place where I record my name I will come to you and I will bless you.
25 Ngati mudzandimangira guwa lansembe lamiyala, musagwiritse ntchito miyala yosema, pakuti mudzalidetsa mukadzagwiritsa ntchito zida.
If you make me an altar of stone, you shall not build it of cut stones; for if you lift up your tool on it, you have polluted it.
26 Musamakwere pa makwerero popita pa guwa langa lansembe kuti mungaonetse maliseche anu.
You shall not go up by steps to my altar, that your nakedness may not be exposed to it.’

< Eksodo 20 >