< Eksodo 20 >

1 Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:
I mluvil Bůh všecka slova tato, řka:
2 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
Já jsem Hospodin Bůh tvůj, kterýž jsem tě vyvedl z země Egyptské, z domu služby.
3 “Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.”
Nebudeš míti bohů jiných přede mnou.
4 “Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
Neučiníš sobě rytiny, ani jakého podobenství těch věcí, kteréž jsou na nebi svrchu, ani těch, kteréž na zemi dole, ani těch, kteréž u vodách pod zemí.
5 Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane.
Nebudeš se jim klaněti, ani jich ctíti. Nebo já jsem Hospodin Bůh tvůj, Bůh silný, horlivý, navštěvující nepravost otců na synech do třetího i čtvrtého pokolení těch, kteříž nenávidí mne,
6 Koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda, ndi kusunga malamulo anga.
A činící milosrdenství nad tisíci těmi, kteříž mne milují, a ostříhají přikázaní mých.
7 “Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
Nevezmeš jména Hospodina Boha svého nadarmo; neboť nenechá bez pomsty Hospodin toho, kdož by bral jméno jeho nadarmo.
8 “Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.
Pomni na den sobotní, abys jej světil.
9 Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi.
Šest dní pracovati budeš, a dělati všeliké dílo své;
10 Koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi, wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu, ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu.
Ale dne sedmého odpočinutí jest Hospodina Boha tvého. Nebudeš dělati žádného díla, ty i syn tvůj i dcera tvá, služebník tvůj i děvka tvá, hovado tvé i příchozí, kterýž jest v branách tvých.
11 Pakuti Yehova anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo mʼmasiku asanu ndi limodzi. Iye anapuma pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Kotero Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale loyera.
Nebo v šesti dnech učinil Hospodin nebe a zemi, moře a všecko, což v nich jest, a odpočinul dne sedmého; protož požehnal Hospodin dne sobotního, a posvětil ho.
12 “Lemekeza abambo ako ndi amayi ako kuti ukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
Cti otce svého i matku svou, ať se prodlejí dnové tvoji na zemi, kterouž Hospodin Bůh tvůj dá tobě.
13 “Usaphe.
Nezabiješ.
14 “Usachite chigololo.
Nesesmilníš.
15 “Usabe.
Nepokradeš.
16 “Usapereke umboni womunamizira mnzako.
Nepromluvíš proti bližnímu svému křivého svědectví.
17 “Usasirire nyumba ya mnzako. Usasirire mkazi wa mnzako kapena wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
Nepožádáš domu bližního svého, aniž požádáš manželky bližního svého, ani služebníka jeho, ani děvky jeho, ani vola jeho, ani osla jeho, ani cožkoli jest bližního tvého.
18 Pamene anthu ankamva mabingu ndi kuona ziphaliwali ndi kumvanso lipenga ndi kuona utsi umene umafuka mʼphiri, ananjenjemera ndi mantha. Ndipo iwo anayima patali.
Veškeren pak lid viděl hřímání to a blýskání, a zvuk trouby, a horu kouřící se. To když viděl lid, pohnuli se a stáli zdaleka.
19 Ndipo anati kwa Mose, “Iwe utiyankhule ndipo tidzamvera. Koma usalole kuti Mulungu atiyankhule, tingafe.”
A řekli Mojžíšovi: Mluv ty s námi, a poslouchati budeme; a nechť nemluví s námi Bůh, abychom nezemřeli.
20 Koma Mose anati kwa anthuwo, “Musachite mantha. Mulungu wabwera kudzakuyesani kuti mukhale ndi mtima woopa Mulungu kuti musamuchimwire.”
Odpověděl Mojžíš lidu: Nebojte se; nebo pro zkušení vás sám Bůh přišel, aby bázeň jeho byla mezi vámi, abyste nehřešili.
21 Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.
Tedy stál lid zdaleka; Mojžíš pak přistoupil k mrákotě, kdež byl Bůh.
22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Awuze izi Aisraeli: ‘Inu mwaona nokha kuti Ine ndakuyankhulani kuchokera kumwamba.
I řekl Hospodin Mojžíšovi: Tak povíš synům Izraelským: Vy jste sami viděli, že s nebe mluvil jsem s vámi.
23 Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’”
Protož nevyzdvihujte ničehož ku poctě se mnou; bohů stříbrných a bohů zlatých neučiníte sobě.
24 Mundimangire guwa ladothi ndipo muziperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe zanu. Pamalo paliponse pamene Ine ndidzakonza kuti muzinditamandirapo, ndidzabwera ndi kukudalitsani.
Oltář z země uděláš mi a obětovati budeš na něm zápaly své, a pokojné oběti své, ovce své a voly své. Na kterémkoli místě rozkáži slaviti památku jména svého, přijdu k tobě a požehnám tobě.
25 Ngati mudzandimangira guwa lansembe lamiyala, musagwiritse ntchito miyala yosema, pakuti mudzalidetsa mukadzagwiritsa ntchito zida.
Jestliže mi pak vzděláš oltář kamenný, nedělej ho z kamene tesaného; nebo jestliže pozdvihneš železa na něj, poškvrníš ho.
26 Musamakwere pa makwerero popita pa guwa langa lansembe kuti mungaonetse maliseche anu.
Aniž po stupních vstupovati budeš k oltáři mému, aby hanba tvá u něho odkryta nebyla.

< Eksodo 20 >