< Eksodo 2 >
1 Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
Odšel je mož iz Lévijeve hiše in za ženo vzel Lévijevo hčer.
2 Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
Ženska je spočela in rodila sina in ko je videla, da je bil čeden otrok, ga je skrivala tri mesece.
3 Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
Ko pa ga ni mogla več skrivati, je zanj vzela pletenico iz ločja, jo namazala z blatom in s smolo in vanjo položila otroka in to položila v rogoz poleg rečnega brega.
4 Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
Njegova sestra pa je stala daleč stran, da izve kaj se bo z njim zgodilo.
5 Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
In dol je prišla faraonova hči, da se pri reki umije, njene služabnice pa so hodile vzdolž rečnega brega in ko je med rogozom zagledala pletenico, je poslala svojo služabnico, da odide ponjo.
6 Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
Ko jo je ta odprla, je zagledala otroka in glej, dojenček je jokal. Do njega je imela sočutje ter rekla: »To je eden izmed hebrejskih otrok.«
7 Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
Potem je njegova sestra rekla faraonovi hčeri: »Ali naj grem in k tebi pokličem dojiljo izmed hebrejskih žensk, da bo lahko otroka dojila zate?«
8 Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
Faraonova hči ji je rekla: »Pojdi.« Deklica je odšla in poklicala otrokovo mater.
9 Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
Faraonova hči ji je rekla: »Odnesi tega otroka proč in ga dôji zame, jaz pa ti bom dajala tvoja plačila.« In ženska je vzela otroka ter ga dojila.
10 Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
Otrok je zrastel in privedla ga je k faraonovi hčeri in ta je postal njen sin. Njegovo ime je imenovala Mojzes. Rekla je: »Ker sem ga potegnila iz vode.«
11 Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
Pripetilo se je v tistih dneh, ko je Mojzes odrasel, da je odšel k svojim bratom, gledal na njihova bremena in oprezal za Egipčanom, ki je udarjal Hebrejca, enega izmed njegovih bratov.
12 Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
Pogledal je to pot in tisto pot in ko je videl, da tam ni bilo nobenega človeka, je Egipčana usmrtil in ga skril v pesek.
13 Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
Ko je drug dan odšel ven, glej, dva moža izmed Hebrejcev sta se skupaj prepirala in temu, ki je storil napačno, je rekel: »Čemu udarjaš svojega rojaka?«
14 Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
Ta pa je rekel: »Kdo te je naredil princa in sodnika nad nama? Ali me nameravaš ubiti, kakor si ubil Egipčana?« Mojzes se je zbal ter rekel: »Ta stvar se je zagotovo izvedela.«
15 Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
Torej, ko je faraon slišal to stvar, je iskal Mojzesa, da ga ubije. Mojzes pa je pobegnil izpred faraonovega obličja in prebival v midjánski deželi in se usedel poleg vodnjaka.
16 Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
Torej duhovnik iz Midjána je imel sedem hčera in prišle so, zajele vodo in napolnile korita, da bi napojile trop svojega očeta.
17 Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
Prišli pa so pastirji ter jih odgnali proč, toda Mojzes je vstal, jim pomagal in napojil njihov trop.
18 Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
Ko so prišle k svojemu očetu Reguélu, je rekel: »Kako je to, da ste danes prišle tako zgodaj?«
19 Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
Rekle so: »Egipčan nas je osvobodil iz roke pastirjev in nam prav tako zajel dovolj vode in napojil trop.«
20 Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
Svojim hčeram je rekel: »In kje je? Zakaj je to, da ste človeka pustile? Pokličite ga, da bo lahko jedel kruh.«
21 Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
Mojzes je bil zadovoljen, da prebiva s človekom in ta je Mojzesu dal svojo hčer Cipóro.
22 Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
Rodila mu je sina in njegovo ime je imenoval Geršóm, kajti rekel je: »Tujec sem bil v tuji deželi.«
23 Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
Pripetilo se je tekom časa, da je egiptovski kralj umrl, Izraelovi otroci pa so vzdihovali zaradi razloga suženjstva in vpili in njihovo vpitje je zaradi razloga suženjstva prišlo do Boga.
24 Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Bog je slišal njihovo stokanje in Bog se je spomnil svoje zaveze z Abrahamom, Izakom in Jakobom.
25 Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.
Bog je pogledal na Izraelove otroke in Bog je imel do njih spoštovanje.