< Eksodo 18 >

1 Yetero wansembe wa ku Midiyani amenenso anali mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu anachitira Mose ndi anthu ake a Aisraeli ndi mmene Yehova anawatulutsira mʼdziko la Igupto.
And whanne Jetro, the prest of Madian, `the alye of Moises, hadde herd alle thingis which God hadde do to Moises, and to Israel his puple, for the Lord hadde led Israel out of the lond of Egipt,
2 Mose atamubweza Zipora, mkazi wake, Yetero, mpongozi wake anamulandira
he took Sefora, `the wijf of Moises, whom he hadde sent ayen,
3 mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”
and hise twei sones, of which oon was clepid Gersan, for the fadir seide, Y was a comelyng in alien lond,
4 Ndipo mwana wake wachiwiri anamupatsa dzina loti Eliezara, pakuti anati, “Mulungu wa makolo anga anali thandizo langa. Iye anandipulumutsa ku lupanga la Farao.”
forsothe the tother was clepid Eliezer, for Moises seide, God of my fadir is myn helpere, and he delyuerede me fro the swerd of Farao.
5 Yetero, mpongozi wa Mose pamodzi ndi ana a Mose aamuna awiri ndi mkazi wake anabwera kwa Mose ku chipululu pa phiri la Mulungu kumene Mose anamanga misasa.
Therfor Jetro, `alie of Moises, cam, and the sones of Moises and his wijf camen to Moises, in to deseert, where Jetro settide tentis bisidis the hil of God;
6 Yetero anali atatumiza uthenga kwa Mose kuti, “Ine Yetero, mpongozi wako, ndikubwera ndi mkazi wako ndi ana ake awiri.”
and sente to Moises, and seide, Y Jetro, thin alie, come to thee, and thi wijf, and thi twei sones with hir.
7 Kotero Mose anatuluka kukakumana ndi mpongozi wake ndipo anawerama ndi kupsompsona. Atalonjerana anakalowa mu tenti
And Moises yede out into the comyng of his alie, and worschipide, and kiste hym, and thei gretten hem silf to gidere with pesible wordis.
8 Mose anafotokozera mpongozi wake zonse zimene Yehova anamuchita Farao ndi Aigupto chifukwa cha Israeli komanso zowawa zonse anakumana nazo mʼnjira. Mose anafotokozanso momwe Yehova anawapulumutsira.
And whanne he hadde entrid in to the tabernacle, Moises tolde to `his alie alle thingis whiche God hadde do to Farao, and to Egipcians, for Israel, and he tolde al the trauel which bifelle to hem in the weie, of which the Lord delyuerede hem.
9 Yetero anakondwa kwambiri atamva zabwino zonse zimene Yehova anachitira Aisraeli powapulumutsa mʼdzanja la Aigupto.
And Jetro was glad on alle the goodis whiche the Lord hadde do to Israel, for he delyuerede Israel fro the hond of Egipcians.
10 Iye anati, “Alemekezeke Yehova amene wakupulumutsani mʼdzanja la Aigupto ndi Farao. Wapulumutsanso anthuwa mʼdzanja la Aigupto.
And Jetro seide, Blessid be `the Lord, that delyuerede you fro the hond of Egipcians, and fro `the hond of Farao, which Lord delyuered his puple fro the hond of Egipt;
11 Tsopano ndikudziwa kuti Yehova ndi wopambana milungu ina yonse, pakuti anachita izi kwa amene ananyoza Israeli.”
now Y knowe that the Lord is greet aboue alle goddis, for `thei diden proudli ayens hem.
12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Mulungu. Aaroni ndi akuluakulu onse a Israeli anabwera kudzadya chakudya pamodzi ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
Therfor Jetro, `alie of Moises, offride brent sacrifices and offryngis to God; and Aaron, and alle the eldere men of Israel, camen to ete breed with hym bifore God.
13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.
Forsothe in the tother dai Moises sat that he schulde deme the puple, that stood niy Moises, fro the morewtid til to euentid.
14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”
And whanne `his alie hadde seyn this, that is, alle thingis `whiche he dide in the puple, he seide, What is this that thou doist in the puple? whi sittist thou aloone, and al the puple abidith fro the morewtid til to euentid?
15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.
To whom Moises answeride, The puple cometh to me, and axith the sentence of God;
16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”
and whanne ony strijf bifallith to hem, thei comen to me, that Y deme bitwixe hem, and schewe `the comaundementis of God, and hise lawis.
17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.
And Jetro seide, Thou doist a thing not good,
18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.
thou art wastid with a fonned trauel, bothe thou and this puple which is with thee; the werk is a boue thi strengthis, thou aloone maist not suffre it.
19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.
But here thou my wordis and counseils, and the Lord schal be with thee; be thou to the puple in these thingis that perteynen to God, that thou telle the thingis that ben seid to the puple;
20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.
and schewe to the puple the cerymonyes, and custom of worschipyng, and the weie bi which `thei owen to go, and the werk which `thei owen to do.
21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.
Forsothe puruey thou of al the puple myyti men, and dredynge God, in whiche is treuthe, and whiche haten auarice; and ordeyne thou of hem tribunes, and centuriouns, and quinquagenaries, and deenys,
22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.
whiche schulen deme the puple in al tyme; sotheli what ever thing is grettere, telle thei to thee, and deme thei ooneli lesse thingis, and be it esiere to thee, whanne the burthun is departid in to othere men.
23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”
If thou schalt do this, thou schalt fille the comaundement of God, and thou schalt mowe bere hise comaundementis; and al this puple schal turne ayen with pees to her places.
24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.
And whanne these thingis weren herd, Moises dide alle thingis whiche Jetro counselide.
25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.
And whanne noble men of al Israel weren chosun Moises ordeynede hem princis of the puple, tribunes, and centuriouns, and quinquagenaries, and denes,
26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.
whiche demeden the puple in al tyme; forsothe, whateuer thing was hardere, thei telden to Moises, and thei demeden esiere thingis oneli.
27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.
And Moises lefte `his alie, which turnede ayen, and yede in to his lond.

< Eksodo 18 >