< Eksodo 18 >
1 Yetero wansembe wa ku Midiyani amenenso anali mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu anachitira Mose ndi anthu ake a Aisraeli ndi mmene Yehova anawatulutsira mʼdziko la Igupto.
and to hear: hear Jethro priest Midian relative Moses [obj] all which to make: do God to/for Moses and to/for Israel people his for to come out: send LORD [obj] Israel from Egypt
2 Mose atamubweza Zipora, mkazi wake, Yetero, mpongozi wake anamulandira
and to take: take Jethro relative Moses [obj] Zipporah woman: wife Moses after parting gift her
3 mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”
and [obj] two son: child her which name [the] one Gershom for to say sojourner to be in/on/with land: country/planet foreign
4 Ndipo mwana wake wachiwiri anamupatsa dzina loti Eliezara, pakuti anati, “Mulungu wa makolo anga anali thandizo langa. Iye anandipulumutsa ku lupanga la Farao.”
and name [the] one Eliezer for God father my in/on/with helper my and to rescue me from sword Pharaoh
5 Yetero, mpongozi wa Mose pamodzi ndi ana a Mose aamuna awiri ndi mkazi wake anabwera kwa Mose ku chipululu pa phiri la Mulungu kumene Mose anamanga misasa.
and to come (in): come Jethro relative Moses and son: child his and woman: wife his to(wards) Moses to(wards) [the] wilderness which he/she/it to camp there mountain: mount [the] God
6 Yetero anali atatumiza uthenga kwa Mose kuti, “Ine Yetero, mpongozi wako, ndikubwera ndi mkazi wako ndi ana ake awiri.”
and to say to(wards) Moses I relative your Jethro to come (in): come to(wards) you and woman: wife your and two son: child her with her
7 Kotero Mose anatuluka kukakumana ndi mpongozi wake ndipo anawerama ndi kupsompsona. Atalonjerana anakalowa mu tenti
and to come out: come Moses to/for to encounter: meet relative his and to bow and to kiss to/for him and to ask man: anyone to/for neighbor his to/for peace: well-being and to come (in): come [the] tent [to]
8 Mose anafotokozera mpongozi wake zonse zimene Yehova anamuchita Farao ndi Aigupto chifukwa cha Israeli komanso zowawa zonse anakumana nazo mʼnjira. Mose anafotokozanso momwe Yehova anawapulumutsira.
and to recount Moses to/for relative his [obj] all which to make: do LORD to/for Pharaoh and to/for Egypt upon because Israel [obj] all [the] hardship which to find them in/on/with way: journey and to rescue them LORD
9 Yetero anakondwa kwambiri atamva zabwino zonse zimene Yehova anachitira Aisraeli powapulumutsa mʼdzanja la Aigupto.
and to rejoice Jethro upon all [the] welfare which to make: do LORD to/for Israel which to rescue him from hand: power Egypt
10 Iye anati, “Alemekezeke Yehova amene wakupulumutsani mʼdzanja la Aigupto ndi Farao. Wapulumutsanso anthuwa mʼdzanja la Aigupto.
and to say Jethro to bless LORD which to rescue [obj] you from hand: owner Egypt and from hand: owner Pharaoh which to rescue [obj] [the] people from underneath: owning hand: owner Egypt
11 Tsopano ndikudziwa kuti Yehova ndi wopambana milungu ina yonse, pakuti anachita izi kwa amene ananyoza Israeli.”
now to know for great: large LORD from all [the] God for in/on/with word: because which to boil upon them
12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Mulungu. Aaroni ndi akuluakulu onse a Israeli anabwera kudzadya chakudya pamodzi ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
and to take: bring Jethro relative Moses burnt offering and sacrifice to/for God and to come (in): come Aaron and all old: elder Israel to/for to eat food: bread with relative Moses to/for face: before [the] God
13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.
and to be from morrow and to dwell Moses to/for to judge [obj] [the] people and to stand: stand [the] people upon Moses from [the] morning till [the] evening
14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”
and to see: see relative Moses [obj] all which he/she/it to make: do to/for people and to say what? [the] word: thing [the] this which you(m. s.) to make: do to/for people why? you(m. s.) to dwell to/for alone you and all [the] people to stand upon you from morning till evening
15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.
and to say Moses to/for relative his for to come (in): come to(wards) me [the] people to/for to seek God
16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”
for to be to/for them word: case to come (in): come to(wards) me and to judge between man: anyone and between neighbor his and to know [obj] statute: decree [the] God and [obj] instruction his
17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.
and to say relative Moses to(wards) him not pleasant [the] word: thing which you(m. s.) to make: do
18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.
to wither to wither also you(m. s.) also [the] people [the] this which with you for heavy from you [the] word: thing not be able to make: do him to/for alone you
19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.
now to hear: obey in/on/with voice my to advise you and to be God with you to be you(m. s.) to/for people opposite [the] God and to come (in): bring you(m. s.) [obj] [the] word: case to(wards) [the] God
20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.
and to warn [obj] them [obj] [the] statute: decree and [obj] [the] instruction and to know to/for them [obj] [the] way: conduct to go: walk in/on/with her and [obj] [the] deed: work which to make: do [emph?]
21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.
and you(m. s.) to see from all [the] people human strength afraid God human truth: faithful to hate unjust-gain and to set: put upon them ruler thousand ruler hundred ruler fifty and ruler ten
22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.
and to judge [obj] [the] people in/on/with all time and to be all [the] word: thing [the] great: large to come (in): bring to(wards) you and all [the] word: thing [the] small to judge they(masc.) and to lighten from upon you and to lift: bear with you
23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”
if [obj] [the] word: thing [the] this to make: do and to command you God and be able to stand: stand and also all [the] people [the] this upon place his to come (in): come in/on/with peace
24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.
and to hear: hear Moses to/for voice relative his and to make: do all which to say
25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.
and to choose Moses human strength from all Israel and to give: make [obj] them head: leader upon [the] people ruler thousand ruler hundred ruler fifty and ruler ten
26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.
and to judge [obj] [the] people in/on/with all time [obj] [the] word: case [the] severe to come (in): bring [emph?] to(wards) Moses and all [the] word: case [the] small to judge they(masc.)
27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.
and to send: depart Moses [obj] relative his and to go: went to/for him to(wards) land: country/planet his