< Eksodo 18 >

1 Yetero wansembe wa ku Midiyani amenenso anali mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu anachitira Mose ndi anthu ake a Aisraeli ndi mmene Yehova anawatulutsira mʼdziko la Igupto.
And Jethro priest of Midian, father-in-law of Moses, hears all that God has done for Moses and for His people Israel, that YHWH has brought out Israel from Egypt,
2 Mose atamubweza Zipora, mkazi wake, Yetero, mpongozi wake anamulandira
and Jethro, father-in-law of Moses, takes Zipporah, wife of Moses, after her parting,
3 mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”
and her two sons, of whom the name of one [is] Gershom, for he said, “I have been a sojourner in a strange land”;
4 Ndipo mwana wake wachiwiri anamupatsa dzina loti Eliezara, pakuti anati, “Mulungu wa makolo anga anali thandizo langa. Iye anandipulumutsa ku lupanga la Farao.”
and the name of the other [is] Eliezer, for, “The God of my father [is] for my help, and He delivers me from the sword of Pharaoh.”
5 Yetero, mpongozi wa Mose pamodzi ndi ana a Mose aamuna awiri ndi mkazi wake anabwera kwa Mose ku chipululu pa phiri la Mulungu kumene Mose anamanga misasa.
And Jethro, father-in-law of Moses, comes, and his sons, and his wife, to Moses, to the wilderness where he is encamping—the mountain of God;
6 Yetero anali atatumiza uthenga kwa Mose kuti, “Ine Yetero, mpongozi wako, ndikubwera ndi mkazi wako ndi ana ake awiri.”
and he says to Moses, “I, your father-in-law Jethro, am coming to you, and your wife, and her two sons with her.”
7 Kotero Mose anatuluka kukakumana ndi mpongozi wake ndipo anawerama ndi kupsompsona. Atalonjerana anakalowa mu tenti
And Moses goes out to meet his father-in-law, and bows himself, and kisses him, and they ask of one another of welfare, and come into the tent;
8 Mose anafotokozera mpongozi wake zonse zimene Yehova anamuchita Farao ndi Aigupto chifukwa cha Israeli komanso zowawa zonse anakumana nazo mʼnjira. Mose anafotokozanso momwe Yehova anawapulumutsira.
and Moses recounts to his father-in-law all that YHWH has done to Pharaoh, and to the Egyptians, on account of Israel, all the travail which has found them in the way, and [how] YHWH delivers them.
9 Yetero anakondwa kwambiri atamva zabwino zonse zimene Yehova anachitira Aisraeli powapulumutsa mʼdzanja la Aigupto.
And Jethro rejoices for all the good which YHWH has done to Israel, whom He has delivered from the hand of the Egyptians;
10 Iye anati, “Alemekezeke Yehova amene wakupulumutsani mʼdzanja la Aigupto ndi Farao. Wapulumutsanso anthuwa mʼdzanja la Aigupto.
and Jethro says, “Blessed [is] YHWH, who has delivered you from the hand of the Egyptians, and from the hand of Pharaoh—who has delivered this people from under the hand of the Egyptians;
11 Tsopano ndikudziwa kuti Yehova ndi wopambana milungu ina yonse, pakuti anachita izi kwa amene ananyoza Israeli.”
now I have known that YHWH [is] greater than all the gods, for in the thing they have acted proudly—[He is] above them!”
12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Mulungu. Aaroni ndi akuluakulu onse a Israeli anabwera kudzadya chakudya pamodzi ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
And Jethro, father-in-law of Moses, takes a burnt-offering and sacrifices [it] for God; and Aaron comes in, and all [the] elderly of Israel, to eat bread with the father-in-law of Moses, before God.
13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.
And it comes to pass on the next day, that Moses sits to judge the people, and the people stand before Moses from the morning to the evening;
14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”
and the father-in-law of Moses sees all that he is doing for the people and says, “What [is] this thing which you are doing for the people? Why are you sitting by yourself, and all the people standing by you from morning until evening?”
15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.
And Moses says to his father-in-law, “Because the people come to me to seek God;
16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”
when they have a matter, it has come to me, and I have judged between a man and his neighbor, and made known the statutes of God, and His laws.”
17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.
And the father-in-law of Moses says to him, “The thing which you are doing [is] not good;
18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.
you surely wear away, both you, and this people which [is] with you, for the thing is too heavy for you, you are not able to do it by yourself.
19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.
Now listen to my voice, I counsel you, and God is with you: be for the people before God, and you have brought in the things to God;
20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.
and you have warned them [concerning] the statutes and the laws, and have made known to them the way in which they go, and the work which they do.
21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.
And you provide out of all the people men of ability, fearing God, men of truth, hating dishonest gain, and have placed [these] over them [for] heads of thousands, heads of hundreds, heads of fifties, and heads of tens,
22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.
and they have judged the people at all times; and it has come to pass, they bring every great matter to you, and they judge every small matter themselves; and lighten it from off yourself, and they have borne with you.
23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”
If you do this thing, and God has commanded you, then you have been able to stand, and all this people also goes to its place in peace.”
24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.
And Moses listens to the voice of his father-in-law, and does all that he said,
25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.
and Moses chooses men of ability out of all Israel, and makes them chiefs over the people [for] heads of thousands, heads of hundreds, heads of fifties, and heads of tens,
26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.
and they have judged the people at all times; they bring the hard matter to Moses, and they judge every small matter themselves.
27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.
And Moses sends his father-in-law away, and he goes away to his own land.

< Eksodo 18 >