< Eksodo 18 >

1 Yetero wansembe wa ku Midiyani amenenso anali mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu anachitira Mose ndi anthu ake a Aisraeli ndi mmene Yehova anawatulutsira mʼdziko la Igupto.
And Jithro, the priest of Midian, Moses' father-in-law, heard all that God had done for Moses, and for Israel his people, that the Lord had brought forth Israel out of Egypt.
2 Mose atamubweza Zipora, mkazi wake, Yetero, mpongozi wake anamulandira
Then took Jithro, the father-in-law of Moses, Zipporah, the wife of Moses, after he had sent her back,
3 mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”
And her two sons; of whom the name of the one was Gershom; for he said, I have been a stranger in a foreign land:
4 Ndipo mwana wake wachiwiri anamupatsa dzina loti Eliezara, pakuti anati, “Mulungu wa makolo anga anali thandizo langa. Iye anandipulumutsa ku lupanga la Farao.”
And the name of the other was Eliezer; for the God of my father was my help, and delivered me from the sword of Pharaoh.
5 Yetero, mpongozi wa Mose pamodzi ndi ana a Mose aamuna awiri ndi mkazi wake anabwera kwa Mose ku chipululu pa phiri la Mulungu kumene Mose anamanga misasa.
And Jithro, the father-in-law of Moses, came with his sons and his wife unto Moses, unto the wilderness, where he was encamped at the mount of God.
6 Yetero anali atatumiza uthenga kwa Mose kuti, “Ine Yetero, mpongozi wako, ndikubwera ndi mkazi wako ndi ana ake awiri.”
And he sent word unto Moses, I thy father-in-law Jithro am coming unto thee, with thy wife, and her two sons with her.
7 Kotero Mose anatuluka kukakumana ndi mpongozi wake ndipo anawerama ndi kupsompsona. Atalonjerana anakalowa mu tenti
And Moses went out to meet his father-in-law, and bowed himself, and kissed him; and they asked each other after their welfare; and they went into the tent.
8 Mose anafotokozera mpongozi wake zonse zimene Yehova anamuchita Farao ndi Aigupto chifukwa cha Israeli komanso zowawa zonse anakumana nazo mʼnjira. Mose anafotokozanso momwe Yehova anawapulumutsira.
And Moses told his father-in-law all which the Lord had done unto Pharaoh and to the Egyptians on account of Israel, all the hardship which had come upon them by the way, and how the Lord had delivered them.
9 Yetero anakondwa kwambiri atamva zabwino zonse zimene Yehova anachitira Aisraeli powapulumutsa mʼdzanja la Aigupto.
And Jithro rejoiced over all the goodness which the Lord had done to Israel, that he had delivered it out of the hand of the Egyptians.
10 Iye anati, “Alemekezeke Yehova amene wakupulumutsani mʼdzanja la Aigupto ndi Farao. Wapulumutsanso anthuwa mʼdzanja la Aigupto.
And Jithro said, Blessed be the Lord, who hath delivered you out of the hand of the Egyptians, and out of the hand of Pharaoh, who hath delivered the people from under the hand of the Egyptians.
11 Tsopano ndikudziwa kuti Yehova ndi wopambana milungu ina yonse, pakuti anachita izi kwa amene ananyoza Israeli.”
Now I know that the Eternal is great above all gods; for by the very thing wherein they sinned presumptuously was punishment brought upon them.
12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Mulungu. Aaroni ndi akuluakulu onse a Israeli anabwera kudzadya chakudya pamodzi ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
And Jithro, the father-in-law of Moses, offered a burnt-offering and sacrifices unto God; and Aaron came, with all the elders of Israel, to eat bread with the father-in-law of Moses, before God.
13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.
And it came to pass on the morrow, that Moses sat to judge the people; and the people stood around Moses from the morning unto the evening.
14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”
And the father-in-law of Moses saw all that he did to the people; and he said, What is this thing that thou doest to the people? why sittest thou thyself alone, and all the people standeth around thee from morning until evening?
15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.
And Moses said unto his father-in-law, Because the people cometh unto me to inquire of God.
16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”
When they have a matter of dispute, they come unto me; and I judge between one and the other, and I make them know the statutes of God, and his laws.
17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.
And the father-in-law of Moses said unto him, The thing that thou doest is not good.
18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.
Thou wilt surely wear away, both thou, and this people that is with thee; for the thing is too heavy for thee; thou wilt not be able to perform it by thyself alone.
19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.
Now hearken unto my voice, I will give thee counsel, and may God be with thee, Be thou for the people a mediator with God, that thou mayest bring the causes unto God.
20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.
And thou shalt explain to them the statutes and the laws; and thou shalt make them know the way wherein they must walk, and the work that they must do.
21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.
Moreover, thou shalt select out of all the people able men, such as fear God, men of truth, hating [their own] gain; and place these over them, as rulers of thousands, rulers of hundreds, rulers of fifties, and rulers of tens.
22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.
And let them judge the people at all times; and it shall be, that every great matter they shall bring unto thee, but every small matter they shall judge themselves: so shall it be easier for thee, when they shall bear with thee.
23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”
If thou wilt do this thing, and God commandeth it thee, then wilt thou be able to endure; and also the whole of this people will come to its place in peace.
24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.
And Moses hearkened to the voice of his father-in-law, and did all that he had said.
25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.
And Moses chose able men out of all Israel, and placed them as heads over the people, rulers of thousands, rulers of hundreds, rulers of fifties, and rulers of tens.
26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.
And they judged the people at all times; any difficult cause they brought unto Moses, but every small cause they judged themselves.
27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.
And Moses dismissed his father-in-law; and he went his way unto his own land.

< Eksodo 18 >