< Eksodo 18 >

1 Yetero wansembe wa ku Midiyani amenenso anali mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu anachitira Mose ndi anthu ake a Aisraeli ndi mmene Yehova anawatulutsira mʼdziko la Igupto.
梅瑟的岳父,米德楊的司祭耶特洛,聽說天主為梅瑟和自己的百姓以色列所行的一切,聽說上主將以色列人領出了埃及,
2 Mose atamubweza Zipora, mkazi wake, Yetero, mpongozi wake anamulandira
梅瑟的岳父耶特洛便帶回梅瑟送回去的妻子漆頗辣和
3 mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”
他兩個兒子:─一個名叫革爾雄,因為梅瑟說:「我在外方作了旅客;」
4 Ndipo mwana wake wachiwiri anamupatsa dzina loti Eliezara, pakuti anati, “Mulungu wa makolo anga anali thandizo langa. Iye anandipulumutsa ku lupanga la Farao.”
一個名叫厄里厄則爾,意謂:「我父親的天主是我的救援,救我脫離了法朗的刀劍。」─
5 Yetero, mpongozi wa Mose pamodzi ndi ana a Mose aamuna awiri ndi mkazi wake anabwera kwa Mose ku chipululu pa phiri la Mulungu kumene Mose anamanga misasa.
梅瑟的岳父耶特洛同梅瑟的兒子和妻子來到了梅瑟那裏,來到曠野,近天主的山,梅瑟安營的地方,
6 Yetero anali atatumiza uthenga kwa Mose kuti, “Ine Yetero, mpongozi wako, ndikubwera ndi mkazi wako ndi ana ake awiri.”
便叫人告訴梅瑟說:「看,你的岳父耶特洛來見你,你的妻子和兩個兒子也一同來了。」
7 Kotero Mose anatuluka kukakumana ndi mpongozi wake ndipo anawerama ndi kupsompsona. Atalonjerana anakalowa mu tenti
梅瑟就出來迎接他的岳父,向他下拜,口親他,彼此問安,隨後進了營幕。
8 Mose anafotokozera mpongozi wake zonse zimene Yehova anamuchita Farao ndi Aigupto chifukwa cha Israeli komanso zowawa zonse anakumana nazo mʼnjira. Mose anafotokozanso momwe Yehova anawapulumutsira.
梅瑟給他岳父講述了上主為以色列的原故,對法朗和埃及人所行的一切,以及路上遭遇的一切困難,上主怎樣整救了他們。
9 Yetero anakondwa kwambiri atamva zabwino zonse zimene Yehova anachitira Aisraeli powapulumutsa mʼdzanja la Aigupto.
耶特洛聽了上主賜給以色列的各種恩惠,從埃及人手中整救了他們,很是高興。
10 Iye anati, “Alemekezeke Yehova amene wakupulumutsani mʼdzanja la Aigupto ndi Farao. Wapulumutsanso anthuwa mʼdzanja la Aigupto.
耶特洛說:「上主應受讚頌,他從埃及人和法朗手中拯救了你們,由埃! 人手中救出了這百姓。
11 Tsopano ndikudziwa kuti Yehova ndi wopambana milungu ina yonse, pakuti anachita izi kwa amene ananyoza Israeli.”
現今我知道「雅威」是眾神中最大的,因為他由那些傲慢對待以色列人的埃及手中,救出這百姓。」
12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Mulungu. Aaroni ndi akuluakulu onse a Israeli anabwera kudzadya chakudya pamodzi ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
梅瑟的岳父耶特洛向天主獻了全燔祭和犧牲,亞郎和以色列眾長老都來到天主前,同梅瑟的岳父聚餐。耶特洛的建議
13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.
次日,梅瑟坐著審判百姓的案件,百姓從早晨到晚上站在梅瑟前。
14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”
梅瑟的岳父看見他對百姓所行的種種,就說:「你對百姓所作的是什麼事﹖為什麼你獨自一人管理,叫眾百姓從早晨到晚上站在你前﹖」
15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.
梅瑟回答他岳父說:「因為百姓到我跟前詢問天主。
16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”
他們有訴訟的事,就來到我跟前,我便在兩造之間施行審判,講明天主的典章和法律。」
17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.
梅瑟的岳父對他說:「你這樣作不對。
18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.
不但使你自己疲乏,而且也使你同你一起的百姓疲勞不堪,因為這事超過你的力量,你獨自一人是不能勝任的。
19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.
現在你聽我的話,我給你出一個主意。願天主與你同在! 你在天主前代表這個百姓,將他們的案件呈到天主前;
20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.
也將典章和法律教訓他們,告訴他們應走的正路,應行的事項。
21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.
你要從百姓中挑選有才能,敬畏天主,忠實可靠,捨己無私的人,派他們作千夫長、百夫長,五十夫長、十夫長,
22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.
叫他們隨時審斷百姓的案件。若有任何重大案件,呈交你處理;其餘一切小案件,可由他們自己處理;叫他們與你分擔,你就輕鬆多了。
23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”
你若這樣作,─天主也這樣命你─你就抵受得住,眾百姓也能平安,各歸其所。」
24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.
梅瑟聽從了他岳父的話,也都照他說的行了。
25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.
梅瑟從全以色列人選拔了有才能的人,立他們作百姓的頭目,作千夫長、百夫長、五十夫長和十夫長,
26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.
叫它們隨時審斷百姓的案件;重大的案件,呈交梅瑟處理;一切小案件,由他們自己處理。
27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.
以後梅瑟送他岳父回了本地。

< Eksodo 18 >