< Eksodo 17 >
1 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.
Gırgın İzrailin cəmə'ət Sin eyhene sahreençe yəqqı'lqa qığeç'e. Rəbbe manbışik'le uvhuyn xhinne manbı ulyoozar-ulyoozar avayk'an. Manbı Refidim eyhene cigeeqa qabı çadırbı g'iyxə. Maa'ad milletın ulyoğasın xhyan eyxhe deş.
2 Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.” Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”
Mançil-allar manbışe Mısa t'yats'axal hı'ı eyhen: – Şas ulyoğasın xhyan hele! Mısee manbışik'le eyhen: – Nya'a şu zak'le cuvabbı eyhe? Nişil-allane şu Rəbb siliys ı'xı'yxə?
3 Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”
Milletıs xhyan ıkkan eyxhe. Mançil-allad manbışe Mısa t'yats'axal hı'ı eyhen: – Nya'a ğu şi Misirğançe qığav'u? İn ğu şak, şinab, yişin uşaxarıb, həyvanarıd xhineka gyatt'asdemene hı'ı?
4 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”
Mısee Rəbbilqa onu'u eyhen: – İne milletık zı hucoone ha'as? Manbı zalqa g'aye gyooğa'asınçıl qepxha vob.
5 Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka.
Rəbbee Mısays inəxdun alidghıniy qele: – Vakasana sabara milletın ağsaqqalar qopt'ul milletne ögiyl hoora. Nil eyhene damays ı'xı'yn əsayid xılyaqa aleet'e.
6 Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli.
Maane Xorev eyhene ganzıl Zı yiğne ögiyl ulyozaras. Mane yiğne xılene əsaaka ganzıle k'ena it'umda ı'xe, mançeençe milletıs ulyoğasın xhyan qığeç'es. Mısee İzrailyne ağsaqqalaaşine ögiyl həməxüd ha'a.
7 Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”
Mısee mane cigaynıd do Massayiy Meriva (siliys ı'xı'y, cuvabbı uvhiy) giyxhe. Ma'ad İzrailybışe cok'le cuvabbı eyheva, «Rəbbir şakaniyxan deşxhee, de'eşdaniyxanva» uvhu, Rəbbir siliys ı'xı'va man do giyxhe.
8 Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.
Mançile qiyğa Amalekar Refidimeeqa abı İzrailybışika suç'ookanbı.
9 Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”
Mısee Yeşuayk'le eyhen: – Hark'ın milletıke insanar g'əvxe, yişdemee Amalekaaşika saç'uvkecen. Zı g'iyqa Allahne əsaaka tepayne q'oma ulyozarasda.
10 Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri.
Yeşueeyid Mısee uvhuyn xhinne ha'a, hark'ın Amalekaaşika siç'ekkvana. Mısa, Harun, Xur hapk'ın ılqeebaç'enbı tepayne q'omaqa.
11 Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana.
Mısee xıleppı ooqa qı'ımee İzrailybı ğamebaxhenbıniy, mang'un xıleppı ozzur avqa qeetxhamee, ğamebaxhe giviyğalanbı Amalekar.
12 Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa.
Mısayn xıleppı oyzaranbı, mang'usse xıleppı orzuliyvalike ooqa qa'as dəxəmee, Haruneeyiy Xuree g'aye abı Mısa çilqa gya'a. Mang'un sa xıl aqqaqqan Harunee mansad Xuree. Məxüd verığ k'yooçesmee, manbışe mang'un xıleppı xəə aqqaqqa.
13 Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.
Məxüb Yeşuee Amalekbı cune g'ılıncıke alğaa'a.
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”
Rəbbee Mısayk'le eyhen: – İnsanaaşe yik'el aqqecenva kitabeeqa ok'ne. Qiyğad Yeşuayk'le eyhe, Zı Amalekaaşin docad ç'iyene aq'vale hakkal ha'asın.
15 Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).
Mısee q'urban ablya'an ciga ali'ı çin doyud YAHVE Nissi (zas Rəbbee ğamxhesda guc hoole) gixhxhı,
16 Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”
eyhen: – Zı Rəbbilqa k'ın g'iysar, Rəbbee Amalekaaşikana dəv'ə ç'əv ha'as deş.