< Eksodo 17 >

1 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.
Så brød hele Israels Menighed op fra Sins Ørken og drog fra Lejrplads til Lejrplads efter HERRENs Bud. Men da de lejrede sig i Refidim, havde Folket intet Vand at drikke.
2 Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.” Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”
Da kivedes Folket med Moses og sagde: "Skaf os Vand at drikke!" Men Moses svarede dem: "Hvorfor kives I med mig, hvorfor frister I HERREN?"
3 Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”
Og Folket tørstede der efter Vand og knurrede mod Moses og sagde: "Hvorfor har du ført os op fra Ægypten? Mon for at lade os og vore Børn og vore Hjorde dø af Tørst?"
4 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”
Da råbte Moses til HERREN: "Hvad skal jeg gøre med dette Folk? Det er ikke langt fra, at de vil stene mig."
5 Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka.
Men HERREN sagde til Moses: "Træd frem for Folket med nogle af Israels Ældste og tag den Stav, du slog Nilen med, i din Hånd og kom så!
6 Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli.
Se, jeg vil stå foran dig der på Klippen ved Horeb, og når du slår på Klippen, skal der strømme Vand ud af den, så Folket kan få noget at drikke." Det gjorde Moses så i Påsyn af Israels Ældste.
7 Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”
Og han kaldte dette Sted Massa og Meriba, fordi Israeliterne der havde kivedes og fristet HERREN ved at sige: "Er HERREN iblandt os eller ej?"
8 Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.
Derefter kom Amalekiterne og angreb Israel i Refdim.
9 Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”
Da sagde Moses til Josua: "Udvælg dig Mænd og ryk i. Morgen ud til Kamp mod Amalekiterne; jeg vil stille mig på Toppen af Højen med Guds Stav i Hånden!"
10 Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri.
Josua gjorde, som Moses bød, og rykkede ud til Kamp mod Amalekiterne. Men Moses, Aron og Hur gik op på Toppen af Højen.
11 Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana.
Når nu Moses løftede Hænderne i Vejret, fik Israeliterne Overtaget, men når han lod Hænderne synke, fik Amalekiterne Overtaget.
12 Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa.
Og da Moses's Hænder blev trætte, tog de en Sten og lagde under ham; så satte han sig på den, og Aron og Hur støttede hans Hænder, hver på sin Side; således var hans Hænder stadig løftede til Solen gik ned,
13 Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.
og Josua huggede Amalekiterne og deres Krigsfolk ned med Sværdet.
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”
Da sagde HERREN til Moses: "Optegn dette i en Bog, for at det kan mindes, og indskærp Josua, at jeg fuldstændig vil udslette Amalekiternes Minde under Himmelen!"
15 Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).
Derpå byggede Moses et Alter og kaldte det: "HERREN er mit Banner!"
16 Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”
Og han sagde: "Der er en udrakt Hånd på HERRENs Trone! HERREN har Krig med Amalek fra Slægt til Slægt!"

< Eksodo 17 >