< Eksodo 16 >
1 Pambuyo pake gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Elimu, ndipo pa tsiku la khumi ndi chisanu mwezi wachiwiri chichokere mʼdziko la Igupto, anafika ku chipululu cha Sini chimene chinali pakati pa Elimu ndi Sinai.
Et ils partirent d’Elim, et toute la multitude des enfants d’Israël vint au désert de Sin, qui est entre Elim et Sinaï, le quinzième jour du second mois après qu’ils furent sortis de la terre d’Egypte.
2 Mʼchipululumo gulu lonse linadandaulira Mose ndi Aaroni
Et toute l’assemblée des enfants d’Israël murmura contre Moïse et Aaron dans le désert.
3 kuti, “Kukanakhala bwino Yehova akanatiphera mʼdziko la Igupto! Kumeneko timadya nyama ndi buledi mpaka kukhuta, koma inu mwabwera nafe ku chipululu kudzapha mpingo wonsewu ndi njala!”
Et les enfants d’Israël leur dirent: Plût à Dieu que nous fussions morts par la main du Seigneur dans la terre d’Egypte, quand nous étions assis près des marmites de viandes, et que nous mangions du pain à satiété! Pourquoi nous avez-vous amenés dans ce désert, pour faire mourir toute cette multitude de faim?
4 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzakupatsani buledi wogwa kuchokera kumwamba ngati mvula. Anthu azituluka tsiku lililonse kukatola buledi wokwanira tsiku limenelo. Ine ndidzawayesa mʼnjira imeneyi kuti ndione ngati adzatsatira malangizo anga.
Or le Seigneur dit à Moïse: Voici que moi, je ferai pleuvoir pour vous du pain du ciel; que le peuple sorte, et qu’il en amasse ce qui lui suffira pour chaque jour, afin que j’éprouve s’il marche en ma loi, ou non.
5 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, pamene azidzakonza buledi amene abwera naye, adzapeza kuti ndi wokwanira masiku awiri.”
Mais qu’au sixième jour ils apprêtent ce qu’ils auront apporté, et que ce soit le double de ce qu’ils avaient coutume d’amasser chaque jour.
6 Kotero Mose ndi Aaroni anati kwa Aisraeli onse, “Nthawi yamadzulo inu mudzadziwa kuti ndi Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.
Et Moïse et Aaron dirent à tous les enfants d’Israël: Ce soir vous saurez que c’est le Seigneur qui vous a retirés de la terre d’Egypte;
7 Ndipo mmawa mudzaona ulemerero wa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu. Kodi ife ndi yani kuti muzitidandaulira?”
Et au matin vous verrez la gloire du Seigneur; car il a entendu votre murmure contre lui; mais nous, qui sommes-nous, pour que vous murmuriez contre nous?
8 Mose anati, “Yehova adzakupatsani nyama madzulo aliwonse ndi buledi mmawa uliwonse kuti mukhute chifukwa Iye wamva madandawulo anu. Nanga ife ndi yani? Kudandaula kwanu simudandaulira ife, koma Yehova.”
Et Moïse ajouta: Le Seigneur vous donnera ce soir de la chair à manger, et au matin du pain à satiété, parce qu’il a entendu vos murmures par lesquels vous avez murmuré contre lui; car, nous, que sommes-nous? ce n’est donc pas contre nous qu’est votre murmure, mais contre le Seigneur.
9 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Bwerani pamaso pa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu.’”
Moïse dit aussi à Aaron: Dis à toute l’assemblée des enfants d’Israël: Approchez-vous devant le Seigneur car il a entendu votre murmure.
10 Pamene Aaroni amayankhula ndi gulu lonse la Aisraeli, iwo anayangʼana ku chipululu, ndipo ulemerero wa Yehova umaoneka mu mtambo.
Et lorsque Aaron parlait à toute l’assemblée des enfants d’Israël, ils regardèrent vers le désert, et voilà que la gloire du Seigneur apparut dans la nuée.
11 Yehova anati kwa Mose,
Or le Seigneur parla à Moïse, disant:
12 “Ine ndamva kudandaula kwa Aisraeli. Awuze kuti, ‘Madzulo mudzadya nyama ndipo mmawa mudzakhuta buledi. Pamenepo mudzadziwa kuti ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
J’ai entendu les murmures des enfants d’Israël, dis-leur: Ce soir vous mangerez de la chair, et au matin vous serez rassasiés de pain, et vous saurez que je suis le Seigneur votre Dieu.
13 Madzulo amenewo panatuluka zinziri zimene zinali ponseponse pa misasa yawo, ndipo mmawa panali mame kuzungulira misasa yawo.
Le soir vint donc, et les cailles montant couvrirent le camp: le matin aussi la rosée se trouva répandue autour du camp.
14 Mamewo atachoka, pa nthaka mʼchipululumo panaoneka tinthu tina topyapyala komanso totuwa ngati chipale.
Et lorsqu’elle eut couvert la surface de la terre, il apparut dans le désert quelque chose de menu et comme pilé au mortier, ressemblant à la gelée blanche sur la terre.
15 Aisraeli atationa anafunsana wina ndi mnzake nati, “Kodi timeneti nʼchiyani?” Popeza sanatidziwe. Mose anawawuza kuti, “Uyu ndi buledi amene Yehova wakupatsani kuti mudye.
Ce qu’ayant vu les enfants d’Israël, ils se dirent les uns aux autres: Manhu, ce qui signifie: Qu’est-ceci? ils ignoraient, en effet, ce que c’était. Moïse leur dit: C’est le pain que le Seigneur vous a donné à manger.
16 Yehova walamula kuti, ‘Aliyense atole zomukwanira kudya, malita awiri pa munthu mmodzi molingana ndi chiwerengero cha anthu amene ali mu tenti yanu.’”
Voici les paroles que le Seigneur a ordonnées: Que chacun en amasse autant qu’il suffit pour manger: un gomor pour chaque tête, selon le nombre de vos âmes qui habitent dans leur tente; voilà ce que vous recueillerez.
17 Aisraeli anachita zonse anawawuza. Ena anatola zambiri ena zochepa.
Et les enfants d’Israël firent ainsi, et ils en amassèrent, l’un plus, l’autre moins.
18 Ndipo iwo atayeza ndi muyeso wa malita awiri, iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere. Aliyense anatola zomukwanira kudya.
Et ils la mesurèrent à la mesure du gomor: or celui qui en avait plus amassé, n’en eut pas davantage, et celui qui en avait moins amassé, n’en trouva pas moins, car chacun en recueillit selon ce qu’il pouvait manger.
19 Ndipo Mose anawawuza kuti, “Wina aliyense asasunge mpaka mmawa.”
Moïse leur dit aussi: Que nul n’en laisse pour le malin.
20 Komabe ena sanamvere Mose, anasungako mpaka mmawa. Koma mmawa mwake tonse tinali mphutsi zokhazokha. Kotero Mose anawapsera mtima.
Tous ne l’écoutèrent pas, mais quelques-uns d’entre eux en laissèrent jusqu’au matin; or elle commença par fourmiller de vers, puis elle se corrompit; et Moïse fut irrité contre eux.
21 Mmawa uliwonse aliyense amatola zimene amazifuna, ndipo dzuwa likatentha zimasungunuka.
Chacun en amassait donc le matin autant qu’il pouvait suffire pour manger; et lorsque le soleil était devenu chaud, elle se fondait.
22 Tsiku lachisanu ndi chimodzi anatuta malita anayi munthu aliyense, ndipo atsogoleri a mpingo wonse anabwera kudzawuza Mose za zimenezi.
Mais, au sixième jour, ils amassèrent le double de cette nourriture, c’est-à-dire, deux gomors pour chaque personne: tous les chefs de la multitude vinrent, et l’annoncèrent à Moïse,
23 Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova analamula, ‘Mawa ndi tsiku lopumula, Sabata Loyera la Yehova, choncho wotchani ndi kuphika zimene mukufuna. Sungani zotsala mpaka mmawa.’”
Qui leur dit: Voici ce qu’a dit le Seigneur: C’est demain le repos du sabbat, consacré au Seigneur; ce qui doit être fait, faites-le aujourd’hui; et ce qui doit être cuit, faites-le cuire, mais tout ce qui sera de reste, serrez-le jusqu’au matin.
24 Choncho anasunga mpaka mmawa monga Mose anawalamulira, ndipo sananunkhe kapena kuchita mphutsi.
Ils firent donc selon qu’avait ordonné Moïse, et la manne ne se corrompit point; et on n’y trouva pas de ver.
25 Mose anati, “Idyani lero chifukwa lero ndi Sabata la Yehova. Lero simukapeza chilichonse kunjaku.
Et Moïse dit: Mangez-la aujourd’hui, parce que c’est le sabbat du Seigneur; il ne s’en trouvera pas aujourd’hui dans la campagne.
26 Muzitola chakudya masiku asanu ndi limodzi koma tsiku la chisanu ndi chiwiri ndi la Sabata, simukapeza chilichonse kunjaku.”
Pendant six jours ramassez-en, car au septième jour, c’est le sabbat du Seigneur; c’est pourquoi on n’en trouvera pas.
27 Komabe anthu ena anapita kuti akatole chakudya tsiku lachisanu ndi chiwiri, koma sanapeze kanthu.
Or vint le septième jour, et quelques-uns du peuple étant sortis pour en amasser, ils n’en trouvèrent point.
28 Ndipo Yehova anafunsa Mose nati, “Kodi inu muzipitirira kukana kusunga malamulo ndi malangizo anga mpaka liti?
Alors le Seigneur dit à Moïse: Jusqu’à quand ne voudrez vous point garder mes commandements et ma loi?
29 Taonani, popeza Yehova wakupatsani Sabata nʼchifukwa chake tsiku lachisanu ndi chimodzi amakupatsani chakudya cha masiku awiri. Aliyense azikhala pamene ali pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, pasapezeke wotuluka kunja.”
Voyez que le Seigneur vous a donné le sabbat, et à cause de cela au sixième jour il vous a accordé le double de nourriture: que chacun demeure chez soi, et que nul ne sorte de son lieu au septième jour.
30 Kotero anthu anapuma tsiku lachisanu ndi chiwiri.
Ainsi le peuple sabbatisa au septième jour.
31 Aisraeli anatchula chakudyacho Mana. Chakudyacho chinkaoneka ngati mbewu zamapira, zoyera. Ndipo chinkakoma ngati chothira uchi.
Et la maison d’Israël appela cette nourriture du nom de Man; elle était blanche comme une graine de coriandre, et son goût, celui de la fleur de farine mêlée avec du miel.
32 Mose anati, “Chimene Yehova walamula ndi ichi: ‘Tengani muyeso wa malita awiri a mana ndi kusungira mibado imene ikubwera, kuti iwo adzaone chakudya chimene Ine ndinakupatsani kuti mudye mʼchipululu pamene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
Or Moïse dit: Voici les paroles qu’a ordonnées le Seigneur: Emplis-en un gomor, et qu’il soit gardé dans les générations qui doivent venir dans la suite, afin qu’elles connaissent le pain dont je vous ai nourris dans le désert, quand vous avez été retirés de la terre d’Egypte.
33 Choncho Mose anati kwa Aaroni, “Tenga mtsuko ndipo uyikemo malita awiri a mana. Ndipo uyike manawo pamaso pa Yehova kusungira mibado imene ikubwera.”
Et Moïse dit à Aaron: Prends un vase et mets-y de la Manne, autant que peut en contenir un gomor; et place-le devant le Seigneur, afin de le conserver en vos générations,
34 Monga momwe Yehova analamulira Mose, Aaroni anayika mtsuko uja pafupi ndi bokosi la Chipangano kuti manawo asungike.
Comme a ordonné le Seigneur à Moïse. Et Aaron le plaça dans le tabernacle pour être réservé.
35 Aisraeli anadya mana zaka 40, mpaka pamene anafika ku dziko kumene amati akakhazikeko. Iwo anadya mana mpaka pamene anafika mʼmalire a Kanaani.
Or, les enfants d’Israël mangèrent la Manne pendant quarante ans, jusqu’à ce qu’ils vinrent en une terre habitable; c’est de cet aliment qu’ils furent nourris, jusqu’à ce qu’ils touchèrent aux confins de la terre de Chanaan.
36 (Malita awiri amafanana ndi gawo lakhumi la efa).
Or, le gomor est la dixième partie de l’éphi.