< Eksodo 16 >

1 Pambuyo pake gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Elimu, ndipo pa tsiku la khumi ndi chisanu mwezi wachiwiri chichokere mʼdziko la Igupto, anafika ku chipululu cha Sini chimene chinali pakati pa Elimu ndi Sinai.
And they journeyed from Elim, and the whole assembly of the children of Israel came into the wilderness of Sin, which is between Elim and Sinai, on the fifteenth day of the second month after their departure out of the land of Egypt.
2 Mʼchipululumo gulu lonse linadandaulira Mose ndi Aaroni
And the whole assembly of the children of Israel murmured against Moses and against Aaron in the wilderness.
3 kuti, “Kukanakhala bwino Yehova akanatiphera mʼdziko la Igupto! Kumeneko timadya nyama ndi buledi mpaka kukhuta, koma inu mwabwera nafe ku chipululu kudzapha mpingo wonsewu ndi njala!”
And the children of Israel said to them, Would that we had died by the hand of Jehovah in the land of Egypt, when we sat by the flesh-pots, when we ate bread to the full; for ye have brought us out into this wilderness, to kill this whole congregation with hunger!
4 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzakupatsani buledi wogwa kuchokera kumwamba ngati mvula. Anthu azituluka tsiku lililonse kukatola buledi wokwanira tsiku limenelo. Ine ndidzawayesa mʼnjira imeneyi kuti ndione ngati adzatsatira malangizo anga.
Then said Jehovah to Moses, Behold, I will rain bread from heaven for you; and the people shall go out and gather the daily need on its day, that I may prove them, whether they will walk in my law, or not.
5 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, pamene azidzakonza buledi amene abwera naye, adzapeza kuti ndi wokwanira masiku awiri.”
And it shall come to pass on the sixth day, that they shall prepare what they have brought in; and it shall be twice as much as they shall gather daily.
6 Kotero Mose ndi Aaroni anati kwa Aisraeli onse, “Nthawi yamadzulo inu mudzadziwa kuti ndi Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.
And Moses and Aaron said to all the children of Israel, In the evening, then shall ye know that Jehovah has brought you out from the land of Egypt;
7 Ndipo mmawa mudzaona ulemerero wa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu. Kodi ife ndi yani kuti muzitidandaulira?”
and in the morning, then shall ye see the glory of Jehovah; for he has heard your murmurings against Jehovah; — and what are we, that ye murmur against us?
8 Mose anati, “Yehova adzakupatsani nyama madzulo aliwonse ndi buledi mmawa uliwonse kuti mukhute chifukwa Iye wamva madandawulo anu. Nanga ife ndi yani? Kudandaula kwanu simudandaulira ife, koma Yehova.”
And Moses said, When Jehovah gives you in the evening flesh to eat, and in the morning bread to the full; for Jehovah hears your murmurings which ye murmur against him...and what [are] we? your murmurings are not against us, but against Jehovah.
9 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Bwerani pamaso pa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu.’”
And Moses spoke to Aaron, Say to all the assembly of the children of Israel, Come near into the presence of Jehovah; for he has heard your murmurings.
10 Pamene Aaroni amayankhula ndi gulu lonse la Aisraeli, iwo anayangʼana ku chipululu, ndipo ulemerero wa Yehova umaoneka mu mtambo.
And it came to pass, when Aaron spoke to the whole assembly of the children of Israel, that they turned toward the wilderness, and behold, the glory of Jehovah appeared in the cloud.
11 Yehova anati kwa Mose,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
12 “Ine ndamva kudandaula kwa Aisraeli. Awuze kuti, ‘Madzulo mudzadya nyama ndipo mmawa mudzakhuta buledi. Pamenepo mudzadziwa kuti ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
I have heard the murmurings of the children of Israel: speak to them, saying, Between the two evenings ye shall eat flesh, and in the morning ye shall be filled with bread; and ye shall know that I am Jehovah your God.
13 Madzulo amenewo panatuluka zinziri zimene zinali ponseponse pa misasa yawo, ndipo mmawa panali mame kuzungulira misasa yawo.
And it came to pass in the evening, that quails came up, and covered the camp; and in the morning the dew lay round the camp.
14 Mamewo atachoka, pa nthaka mʼchipululumo panaoneka tinthu tina topyapyala komanso totuwa ngati chipale.
And when the dew that lay [round it] was gone up, behold, on the face of the wilderness there was [something] fine, granular, fine as hoar-frost, on the ground.
15 Aisraeli atationa anafunsana wina ndi mnzake nati, “Kodi timeneti nʼchiyani?” Popeza sanatidziwe. Mose anawawuza kuti, “Uyu ndi buledi amene Yehova wakupatsani kuti mudye.
And the children of Israel saw [it], and said one to another, What is it? for they did not know what it was. And Moses said to them, This is the bread which Jehovah has given you to eat.
16 Yehova walamula kuti, ‘Aliyense atole zomukwanira kudya, malita awiri pa munthu mmodzi molingana ndi chiwerengero cha anthu amene ali mu tenti yanu.’”
This is the thing which Jehovah has commanded: Gather of it every man according to what he can eat, an omer a poll, [according to] the number of your persons: ye shall take every man for those that are in his tent.
17 Aisraeli anachita zonse anawawuza. Ena anatola zambiri ena zochepa.
And the children of Israel did so, and gathered, some much, some little.
18 Ndipo iwo atayeza ndi muyeso wa malita awiri, iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere. Aliyense anatola zomukwanira kudya.
And they measured with the omer: then he that gathered much had nothing over, and he that gathered little wanted nothing: they had gathered every man according to the measure of his eating.
19 Ndipo Mose anawawuza kuti, “Wina aliyense asasunge mpaka mmawa.”
And Moses said to them, Let no man leave [any] of it until the morning.
20 Komabe ena sanamvere Mose, anasungako mpaka mmawa. Koma mmawa mwake tonse tinali mphutsi zokhazokha. Kotero Mose anawapsera mtima.
But they did not hearken to Moses; and some men left of it until the morning; then worms bred in it and it stank. And Moses was wroth with them.
21 Mmawa uliwonse aliyense amatola zimene amazifuna, ndipo dzuwa likatentha zimasungunuka.
And they gathered it every morning, every man as much as he could eat; and when the sun became hot, it melted.
22 Tsiku lachisanu ndi chimodzi anatuta malita anayi munthu aliyense, ndipo atsogoleri a mpingo wonse anabwera kudzawuza Mose za zimenezi.
And it came to pass on the sixth day, that they gathered twice as much bread, two omers for one; and all the princes of the assembly came and told Moses.
23 Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova analamula, ‘Mawa ndi tsiku lopumula, Sabata Loyera la Yehova, choncho wotchani ndi kuphika zimene mukufuna. Sungani zotsala mpaka mmawa.’”
And he said to them, This is what Jehovah has said: To-morrow is the rest, the holy sabbath, of Jehovah: bake what ye will bake, and cook what ye will cook; and lay up for yourselves all that remains over, to be kept for the morning.
24 Choncho anasunga mpaka mmawa monga Mose anawalamulira, ndipo sananunkhe kapena kuchita mphutsi.
And they laid it up for the morning, as Moses had commanded; and it did not stink, neither was there any worm in it.
25 Mose anati, “Idyani lero chifukwa lero ndi Sabata la Yehova. Lero simukapeza chilichonse kunjaku.
And Moses said, Eat it to-day; for to-day is sabbath to Jehovah: to-day ye shall not find it in the field.
26 Muzitola chakudya masiku asanu ndi limodzi koma tsiku la chisanu ndi chiwiri ndi la Sabata, simukapeza chilichonse kunjaku.”
Six days shall ye gather it; but on the seventh day is sabbath: on it there shall be none.
27 Komabe anthu ena anapita kuti akatole chakudya tsiku lachisanu ndi chiwiri, koma sanapeze kanthu.
And it came to pass on the seventh day that there went out [some] from the people to gather [it], and they found none.
28 Ndipo Yehova anafunsa Mose nati, “Kodi inu muzipitirira kukana kusunga malamulo ndi malangizo anga mpaka liti?
And Jehovah said to Moses, How long do ye refuse to keep my commandments and my laws?
29 Taonani, popeza Yehova wakupatsani Sabata nʼchifukwa chake tsiku lachisanu ndi chimodzi amakupatsani chakudya cha masiku awiri. Aliyense azikhala pamene ali pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, pasapezeke wotuluka kunja.”
See, for Jehovah hath given you the sabbath; therefore he giveth you on the sixth day the bread for two days. Abide every man in his place: let no man go from his place on the seventh day.
30 Kotero anthu anapuma tsiku lachisanu ndi chiwiri.
And the people rested on the seventh day.
31 Aisraeli anatchula chakudyacho Mana. Chakudyacho chinkaoneka ngati mbewu zamapira, zoyera. Ndipo chinkakoma ngati chothira uchi.
And the house of Israel called its name Manna; and it was like coriander-seed, white; and the taste of it was like cake with honey.
32 Mose anati, “Chimene Yehova walamula ndi ichi: ‘Tengani muyeso wa malita awiri a mana ndi kusungira mibado imene ikubwera, kuti iwo adzaone chakudya chimene Ine ndinakupatsani kuti mudye mʼchipululu pamene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
And Moses said, This is the thing which Jehovah has commanded: Fill an omer of it to be kept for your generations; that they may see the bread that I gave you to eat in the wilderness, when I brought you out of the land of Egypt.
33 Choncho Mose anati kwa Aaroni, “Tenga mtsuko ndipo uyikemo malita awiri a mana. Ndipo uyike manawo pamaso pa Yehova kusungira mibado imene ikubwera.”
And Moses said to Aaron, Take a pot, and put in it an omer full of manna, and deposit it before Jehovah, to be kept for your generations.
34 Monga momwe Yehova analamulira Mose, Aaroni anayika mtsuko uja pafupi ndi bokosi la Chipangano kuti manawo asungike.
As Jehovah had commanded Moses, so Aaron deposited it before the Testimony, to be kept.
35 Aisraeli anadya mana zaka 40, mpaka pamene anafika ku dziko kumene amati akakhazikeko. Iwo anadya mana mpaka pamene anafika mʼmalire a Kanaani.
And the children of Israel ate the manna forty years, until they came into an inhabited land: they ate the manna until they came to the borders of the land of Canaan.
36 (Malita awiri amafanana ndi gawo lakhumi la efa).
Now an omer is the tenth [part] of an ephah.

< Eksodo 16 >